< Malachi 4 >

1 For behold, the day commeth that shall burne as an ouen, and all the proude, yea, and all that doe wickedly, shall be stubble, and the day that commeth, shall burne them vp, sayeth the Lord of hostes, and shall leaue them neither roote nor branche.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ndithu tsiku likubwera; lidzayaka ngati ngʼanjo. Anthu onse odzikuza, ndi aliyense ochita zoyipa adzapsa ngati chiputu, ndipo pa tsiku limene likubweralo adzapserera ndi moto. Sipadzatsalira muzu kapena nthambi.
2 But vnto you that feare my Name, shall the sunne of righteousnesse arise, and health shall be vnder his wings, and ye shall goe forth, and growe vp as fat calues.
Koma inu amene mumaopa dzina langa, dzuwa lachilungamo lidzakutulukirani lili ndi kuwala kokuchiritsani. Ndipo inu mudzatuluka ndi kulumphalumpha ngati ana angʼombe amene atulutsidwa mʼkhola.
3 And ye shall treade downe the wicked: for they shall be dust vnder the soles of your feete in the day that I shall doe this, sayeth the Lord of hostes.
Tsiku limenelo inu mudzapondereza anthu oyipa; adzakhala phulusa ku mapazi anu pa tsiku limene Ine ndidzachite zinthu zimenezi,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
4 Remember the lawe of Moses my seruant, which I commanded vnto him in Horeb for all Israel with the statutes and iudgements.
Kumbukirani zophunzitsa za mtumiki wanga Mose, malamulo ndi malangizo amene ndinamupatsa pa Horebu kuti awuze Aisraeli onse.
5 Beholde, I will sende you Eliiah the Prophet before the comming of the great and fearefull day of the Lord.
“Taonani, ndidzakutumizirani mneneri Eliya lisanafike tsiku lalikulu ndi loopsa la Yehova.
6 And he shall turne the heart of the fathers to the children, and the heart of the children to their fathers, lest I come and smite the earth with cursing.
Iye adzabweza mitima ya makolo kwa ana awo, ndi mitima ya ana kwa makolo awo. Kupanda kutero ndidzabwera kudzakantha dziko lanu ndi temberero.”

< Malachi 4 >