< Luke 20 >
1 And it came to passe, that on one of those dayes, as he taught the people in the Temple, and preached the Gospel, the hie Priests and the Scribes came vpon him with the Elders,
Tsiku lina pamene Iye ankaphunzitsa anthu mʼmabwalo a Nyumba ya Mulungu ndi kuphunzitsa Uthenga Wabwino, akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo, pamodzi ndi akuluakulu anabwera kwa Iye.
2 And spake vnto him, saying, Tell vs by what authoritie thou doest these things, or who is hee that hath giuen thee this authoritie?
Iwo anati, “Mutiwuze mukuchita izi ndi ulamuliro wayani? Ndani anakupatsani ulamuliro uwu?”
3 And he answered, and sayde vnto them, I also will aske you one thing: tell me therefore:
Iye anayankha kuti, “Inenso ndikufunsani, mundiyankhe,
4 The baptisme of Iohn, was it from heauen, or of men?
‘Kodi ubatizo wa Yohane, unali wochokera kumwamba, kapena wochokera kwa anthu?’”
5 And they reasoned within themselues, saying, If we shall say, From heauen, he will say, Why then beleeued ye him not?
Iwo anakambirana pakati pawo ndikuti, “Ngati ife tinena kuti, ‘Kuchokera kumwamba’ Iye akatifunsa kuti, ‘chifukwa chiyani simunamukhulupirire iye?’
6 But if we shall say, Of men, all the people will stone vs: for they be perswaded that Iohn was a Prophet.
Koma ngati ife tinena kuti, ‘kuchokera kwa anthu,’ anthu onse atigenda miyala, chifukwa amatsimikiza kuti Yohane anali mneneri.”
7 Therefore they answered, that they could not tell whence it was.
Pamenepo iwo anayankha kuti, “Ife sitidziwa kumene unachokera.”
8 Then Iesus sayd vnto them, Neither tell I you, by what authoritie I doe these things.
Yesu anati, “Ngakhale Inenso sindikuwuzani kuti ndi ulamuliro wanji umene ndikuchitira zimenezi.”
9 Then began he to speake to ye people this parable, A certaine man planted a vineyarde, and let it forth to husbandmen: and went into a strange countrey, for a great time.
Iye anapitirira kuwawuza anthu fanizo ili: “Munthu wina analima munda wamphesa, nabwereketsa kwa alimi ena ndipo anachoka kwa nthawi yayitali.
10 And at the time conuenient he sent a seruant to the husbandmen, that they should giue him of the fruite of the vineyard: but the husbandmen did beate him, and sent him away emptie.
Pa nthawi yokolola, iye anatumiza wantchito wake kwa alimi aja kuti amupatseko zina mwa zipatso za munda wamphesawo. Koma alimi aja anamumenya namubweza wopanda kanthu.
11 Againe he sent yet another seruant: and they did beate him, and foule entreated him, and sent him away emptie.
Iye anatumiza wantchito wina, koma uyunso anamumenya namuchita zachipongwe ndi kumubweza wopanda kanthu.
12 Moreouer he sent the third, and him they wounded, and cast out.
Iye anatumizanso wina wachitatu ndipo iwo anamuvulaza namuponya kunja.
13 Then sayd the Lord of the vineyard, What shall I doe? I will send my beloued sonne: it may be that they will doe reuerence, when they see him.
“Kenaka mwini mundawo anati, ‘Kodi ndichite chiyani? Ndidzatumiza mwana wanga wamwamuna, amene ndimukonda; mwina iwo adzamuchitira ulemu.’
14 But when the husbandmen sawe him, they reasoned with themselues, saying, This is the heire: come, let vs kill him, that the inheritance may be ours.
“Koma alimiwo ataona mwanayo, anakambirananso. Iwo anati, ‘Uyu ndiye wodzamusiyira chumachi. Tiyeni timuphe ndipo chumachi chikhala chathu.’
15 So they cast him out of the vineyarde, and killed him. What shall the Lord of the vineyarde therefore doe vnto them?
Ndipo anamuponya kunja kwa mundawo ndi kumupha. “Nanga tsono mwini munda wamphesayo adzawatani anthuwa?
16 He will come and destroy these husbandmen, and wil giue out his vineyard to others. But when they heard it, they sayd, God forbid.
Iye adzabwera ndi kupha alimi aja ndi kupereka mundawo kwa ena.” Pamene anthu anamva izi, anati, “Musatero ayi.”
17 And he beheld them, and said, What meaneth this then that is written, The stone that the builders refused, that is made the head of the corner?
Yesu anawayangʼanitsitsa ndipo anafunsa kuti, “Kodi tanthauzo lake ndi chiyani la zimene zinalembedwa kuti, “‘Mwala umene omanga nyumba anawukana wasanduka mwala wa pa ngodya.
18 Whosoeuer shall fall vpon that stone, shall be broken: and on whomsoeuer it shall fall, it will grinde him to pouder.
Aliyense amene agwa pa mwalawu adzapweteka, koma iye amene udzamugwera udzamuphwanya.’”
19 Then the hie Priests, and the Scribes the same houre went about to lay hands on him: (but they feared the people) for they perceiued that he had spoken this parable against them.
Aphunzitsi amalamulo ndi akulu a ansembe amafuna njira yoti amuphe nthawi yomweyo, chifukwa anadziwa kuti ananena fanizo ili powatsutsa iwo. Koma iwo anali ndi mantha chifukwa cha anthu.
20 And they watched him, and sent forth spies, which should faine themselues iust men, to take him in his talke, and to deliuer him vnto the power and authoritie of the gouernour.
Pamene ankamulondalonda Iye, iwo anatumiza akazitape amene amaoneka ngati achilungamo. Iwo ankafuna kumutapa mʼkamwa Yesu mu china chilichonse chimene Iye ananena kuti amupereke Iye kwa amene anali ndi mphamvu ndi ulamuliro oweruza.
21 And they asked him, saying, Master, we know that thou sayest, and teachest right, neither doest thou accept mans person, but teachest the way of God truely.
Potero akazitapewo anamufunsa Iye kuti, “Aphunzitsi, tidziwa kuti mumayankhula ndi kuphunzitsa zimene zili zoonadi, ndi kuti simuonetsa tsankho koma mumaphunzitsa njira ya Mulungu mwachoonadi.
22 Is it lawfull for vs to giue Cesar tribute or no?
Kodi ndi bwino kwa ife kumapereka msonkho kwa Kaisara kapena kusapereka?”
23 But he perceiued their craftines, and sayd vnto them, Why tempt ye me?
Iye anaona chinyengo chawo ndipo anawawuza kuti,
24 Shew me a penie. Whose image and superscription hath it? They answered, and sayd, Cesars.
“Onetseni ndalama. Chithunzi ndi malembawa ndi zayani?”
25 Then he sayd vnto them, Giue then vnto Cesar the things which are Cesars, and to God those which are Gods.
Iwo anayankha kuti, “Za Kaisara.” Iye anawawuza kuti, “Ndiye perekani kwa Kaisara zake za Kaisara ndi kwa Mulungu zimene ndi za Mulungu.”
26 And they could not reproue his saying before the people: but they marueiled at his answere, and helde their peace.
Iwo analephera kumupeza cholakwa pa zimene ankayankhula pamaso pa anthu. Ndipo pothedwa nzeru ndi yankho lake, iwo anakhala chete.
27 Then came to him certaine of the Sadduces (which denie that there is any resurrection) and they asked him,
Ena mwa Asaduki, amene ankanena kuti kulibe kuuka kwa akufa, anabwera kwa Yesu ndi funso.
28 Saying, Master, Moses wrote vnto vs, If any mans brother die hauing a wife, and hee die without children, that his brother should take his wife, and raise vp seede vnto his brother.
Iwo anati, “Aphunzitsi, Mose anatilembera kuti munthu akamwalira ndi kusiya mkazi wopanda ana, mʼbale wa munthu womwalirayo akuyenera kukwatira mkaziyo kuti amuberekere ana mʼbale wakeyo.
29 Now there were seuen brethren, and the first tooke a wife, and he dyed without children.
Tsopano panali abale asanu ndi awiri. Woyambayo anakwatira mkazi ndipo anafa wopanda mwana.
30 And the second tooke the wife, and he dyed childelesse.
Wachiwiri
31 Then the third tooke her: and so likewise the seuen dyed, and left no children.
ndipo kenaka wachitatuyo anamukwatira iye, ndipo chimodzimodzi asanu ndi awiri aja anafa osasiya ana.
32 And last of all the woman dyed also.
Pa mapeto pake mkaziyo anafanso.
33 Therefore at the resurrection, whose wife of them shall she be? for seuen had her to wife.
Tsopano, pa nthawi ya kuukanso, kodi mkaziyu adzakhala wayani popeza onse asanu ndi awiri anamukwatirapo?”
34 Then Iesus answered, and sayd vnto them, The children of this world marry wiues, and are married. (aiōn )
Yesu anayankha kuti, “Anthu a mʼbado uno amakwatira ndi kukwatiwa. (aiōn )
35 But they which shalbe counted worthy to enioy that world, and the resurrection from the dead, neither marry wiues, neither are married. (aiōn )
Koma mʼmoyo umene ukubwerawo, anthu amene adzaukitsidwe kwa akufa sadzakwatira kapena kukwatiwa. (aiōn )
36 For they can die no more, forasmuch as they are equall vnto the Angels, and are the sonnes of God, since they are the children of the resurrection.
Ndipo sadzafanso, pakuti adzakhala ngati angelo. Iwo ndi ana a Mulungu, chifukwa adzakhala ataukitsidwa kwa akufa.
37 And that the dead shall rise againe, euen Moses shewed it besides the bush, when he said, The Lord is the God of Abraham, and the God of Isaac, and the God of Iacob.
Ngakhale pa nkhani yachitsamba choyaka moto, Mose anaonetsa kuti akufa amauka, pakuti anatcha Ambuye ‘Mulungu wa Abrahamu, Mulungu wa Isake ndi Mulungu wa Yakobo.’
38 For he is not the God of the dead, but of them which liue: for all liue vnto him.
Mulungu si Mulungu wa akufa, koma wa amoyo, pakuti kwa Iye onse ali ndi moyo.”
39 Then certaine of the Scribes answered, and sayd, Master, thou hast well sayd.
Ena mwa aphunzitsi amalamulo anayankha kuti, “Mwanena bwino mphunzitsi!”
40 And after that, durst they not aske him any thing at all.
Ndipo panalibe wina amene akanalimba mtima kumufunsa Iye mafunso ena.
41 Then sayd he vnto them, Howe say they that Christ is Dauids sonne?
Kenaka Yesu anawawuza kuti, “Zikutheka bwanji kuti aziti Khristu ndi mwana wa Davide?
42 And Dauid himselfe sayth in the booke of the Psalmes, The Lord sayd vnto my Lord, Sit at my right hand,
Davide mwini wake akunenetsa mʼbuku la Masalimo kuti, “Ambuye anati kwa Ambuye anga: ‘Khalani ku dzanja langa lamanja,
43 Till I shall make thine enemies thy footestoole.
mpaka Ine nditasandutsa adani anu chopondapo mapazi anu?’
44 Seeing Dauid called him Lord, howe is he then his sonne?
Davide akumutcha Iye ‘Ambuye.’ Nanga zingatheke bwanji kuti Iye akhale mwana wake?”
45 Then in the audience of all the people he sayd vnto his disciples,
Pamene anthu onse ankamvetsera, Yesu anati kwa ophunzira ake,
46 Beware of the Scribes, which willingly go in long robes, and loue salutations in the markets, and the highest seates in the assemblies, and the chiefe roomes at feastes:
“Chenjerani ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo amakonda kuyenda atavala mikanjo ndipo amakonda kulonjeredwa mʼmisika ndipo amakhala mʼmipando yofunika mʼmasunagoge ndi mʼmalo aulemu mʼmaphwando.
47 Which deuoure widowes houses, and in shewe make long prayers: These shall receiue greater damnation.
Amawadyera akazi amasiye chuma chawo ndi kuchita mapemphero aatali kuti awaone. Anthu oterewa adzalangidwa kwambiri.”