< Luke 17 >

1 Then said he to his disciples, It can not be auoided, but that offences will come, but wo be to him by whome they come.
Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zinthu zimene zimachimwitsa sizingalephere kubwera, koma tsoka kwa munthu wozibweretsayo.
2 It is better for him that a great milstone were hanged about his necke, and that he were cast into ye sea, then that he should offende one of these litle ones.
Kukanakhala bwino kwa iye kuti aponyedwe mʼnyanja atamangiriridwa mwala wamphero mʼkhosi mwake kusiyana kuti achimwitse mmodzi mwa ana aangʼonowa.
3 Take heede to your selues: if thy brother trespasse against thee, rebuke him: and if hee repent, forgiue him.
Nʼchifukwa chake dziyangʼanireni nokha. “Ngati mʼbale wanu achimwa, mudzudzuleni, ndipo ngati alapa, mukhululukireni.
4 And though he sinne against thee seuen times in a day, and seuen times in a day turne againe to thee, saying, It repenteth mee, thou shalt forgiue him.
Ngati iye akulakwira kasanu ndi kawiri pa tsiku, ndipo ngati nʼkubweranso kwa iwe kasanu ndi kawiri nati, ‘Ndalapa,’ umukhululukire.”
5 And the Apostles saide vnto the Lord, Increase our faith.
Atumwiwo anati kwa Ambuye, “Kulitsani chikhulupiriro chathu!”
6 And the Lord said, If ye had faith, as much as is a graine of mustard seede, and should say vnto this mulberie tree, Plucke thy selfe vp by the rootes, and plant thy selfe in the sea, it should euen obey you.
Yesu anayankha kuti, “Ngati muli ndi chikhulupiriro chachingʼono ngati kambewu kampiru, mukhoza kulamula mtengo wamkuyu uwu kuti, ‘Zulidwa ndi kukadzalidwa mʼnyanja,’ ndipo udzakumverani.
7 Who is it also of you, that hauing a seruant plowing or feeding cattell, woulde say vnto him by and by, when hee were come from the fielde, Goe, and sit downe at table?
“Tiyerekeze kuti mmodzi mwa inu anali ndi wantchito wolima kapena woweta nkhosa, kodi angawuze wantchitoyo atabwera ku munda kuti, ‘Tsopano bwera kuno khala pansi kuti udye?’
8 And woulde not rather say to him, Dresse wherewith I may suppe, and girde thy selfe, and serue mee, till I haue eaten and drunken, and afterward eate thou, and drinke thou?
Kodi sangamuwuze kuti, ‘Konzere chakudya cha madzulo, iweyo ukonzeke ndipo undidikirire pamene ndikudya ndi kumwa; kenaka ukhoza kudya ndi kumwa?’
9 Doeth he thanke that seruant, because hee did that which was commanded vnto him? I trowe not.
Kodi iye angathokoze wantchitoyo chifukwa chochita chimene anawuzidwa kuchita?
10 So likewise yee, when yee haue done all those things, which are commanded you, say, We are vnprofitable seruants: wee haue done that which was our duetie to doe.
Chimodzimodzi inunso, mukachita zonse zimene munawuzidwa, muzinena kuti, ‘Ndife antchito osayenera; tangogwira ntchito yathu basi.’”
11 And so it was when he went to Hierusalem, that he passed through the middes of Samaria, and Galile.
Tsopano Yesu anayenda mʼmalire a pakati pa Samariya ndi Galileya pa ulendo wake wa ku Yerusalemu.
12 And as hee entred into a certaine towne, there met him tenne men that were lepers, which stoode a farre off.
Akulowa mʼmudzi wina, amuna khumi amene anali ndi khate anakumana naye. Iwo anayima patali
13 And they lift vp their voyces and saide, Iesus, Master, haue mercie on vs.
ndipo anafuwula ndi mawu okweza kuti, “Yesu, Ambuye, tichitireni chifundo!”
14 And when he saw them, he said vnto them, Goe, shewe your selues vnto the Priestes. And it came to passe, that as they went, they were clensed.
Iye atawaona, anati, “Pitani kadzionetseni nokha kwa ansembe.” Ndipo pamene iwo ankapita, anachiritsidwa.
15 Then one of them, when hee sawe that hee, was healed, turned backe, and with a loude voyce praised God,
Mmodzi wa iwo, ataona kuti wachiritsidwa, anabwerera, nayamika Mulungu ndi mawu okweza.
16 And fell downe on his face at his feete, and gaue him thankes: and he was a Samaritan.
Anagwetsa nkhope yake nagwa pa mapazi a Yesu ndi kumuthokoza. Ndipo iye anali Msamariya.
17 And Iesus answered, and said, Are there not tenne clensed? but where are the nine?
Yesu anafunsa kuti, “Kodi amene anachiritsidwa sanalipo khumi? Nanga asanu ndi anayi ena ali kuti?
18 There is none founde that returned to giue God praise, saue this stranger.
Kodi palibe mmodzi mwa iwo amene anabwerera kudzalemekeza Mulungu kupatula mlendoyu?”
19 And he saide vnto him, Arise, goe thy way, thy faith hath saued thee.
Pamenepo anati kwa iye, “Imirira ndipo pita; chikhulupiriro chako chakuchiritsa iwe.”
20 And when hee was demaunded of the Pharises, when the kingdome of God shoulde come, he answered them, and said, The kingdome of God commeth not with obseruation.
Ndipo Afarisi atamufunsa Iye kuti, ufumu wa Mulungu udzabwera liti, Yesu anayankha kuti, “Mulungu sakhazikitsa ufumu wake mooneka ndi maso,
21 Neither shall men say, Loe here, or lo there: for behold, the kingdome of God is within you.
kapenanso kuti anthu adzati, ‘Uwu uli apa,’ kapena ‘Uwo uli apo,’ Pakuti taonani ufumu wa Mulungu uli pakati panu.”
22 And he saide vnto the disciples, The dayes will come, when ye shall desire to see one of the dayes of the Sonne of man, and ye shall not see it.
Kenaka Iye anati kwa ophunzira ake, “Masiku akubwera pamene inu mudzalakalaka mutaona tsiku limodzi la masiku a Mwana wa Munthu, koma simudzaliona.
23 Then they shall say to you, Behold here, or beholde there: but goe not thither, neither follow them.
Anthu adzakuwuzani kuti, ‘Uyo ali apoyo!’ kapena ‘Uyu ali apa!’ Musawathamangire iwo.
24 For as the lightening that lighteneth out of the one part vnder heauen, shineth vnto the other part vnder heauen, so shall the Sonne of man be in his day.
Pakuti monga mphenzi ingʼanima ndi kuwala kuchokera mbali ina ya thambo kufikira inzake, koteronso adzakhala ali Mwana wa Munthu pa tsiku lake.
25 But first must he suffer many things, and be reprooued of this generation.
Koma poyamba ayenera kuzunzika mu zambiri ndi kukanidwa ndi mʼbado uno.
26 And as it was in the dayes of Noe, so shall it be in the dayes of the Sonne of man.
“Monga mmene zinkachitikira nthawi ya Nowa, momwemonso zidzachitikanso nthawi ya Mwana wa Munthu.
27 They ate, they dranke, they married wiues, and gaue in marriage vnto the day that Noe went into the Arke: and the flood came, and destroyed them all.
Anthu ankadya, kumwa, kukwatira ndi kukwatiwa mpaka tsiku limene Nowa analowa mʼchombo. Pomwepo chigumula chinafika ndi kuwawononga onsewo.
28 Likewise also, as it was in the dayes of Lot: they ate, they dranke, they bought, they solde, they planted, they built.
“Zinalinso chimodzimodzi nthawi ya Loti. Anthu ankadya ndi kumwa, kugula ndi kugulitsa, kudzala ndi kumanga.
29 But in the day that Lot went out of Sodom, it rained fire and brimstone from heauen, and destroyed them all.
Koma tsiku limene Loti anachoka ku Sodomu, moto ndi sulufule zinavumbwa kuchokera kumwamba ndi kuwawononga onsewo.
30 After these ensamples shall it be in the day when the Sonne of man is reueiled.
“Zidzakhalanso choncho Mwana wa Munthu akadzaonekera.
31 At that day hee that is vpon the house, and his stuffe in ye house, let him not come downe to take it out: and he that is in the fielde likewise, let him not turne backe to that he left behinde.
Tsiku limenelo munthu amene ali pa denga la nyumba yake, ndi katundu wake ali mʼnyumbamo, asadzatsike kukatenga. Chimodzimodzinso, munthu amene adzakhale ali ku munda asadzabwerere kukatenga chilichonse.
32 Remember Lots wife.
Kumbukirani mkazi wa Loti!
33 Whosoeuer will seeke to saue his soule, shall loose it: and whosoeuer shall loose it, shall get it life.
Aliyense amene ayesetsa kusunga moyo wake adzawutaya, ndipo aliyense amene ataya moyo wake adzawusunga.
34 I tell you, in that night there shall be two in one bed: the one shalbe receiued, and the other shalbe left.
Ine ndikukuwuzani inu, usiku umenewo anthu awiri adzagona pa mphasa imodzi; wina adzatengedwa ndipo wina adzasiyidwa.
35 Two women shalbe grinding together: the one shalbe taken, and the other shalbe left.
Amayi awiri adzakhala pamodzi akusinja; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.
36 Two shalbe in the fielde: one shalbe receiued, and another shalbe left.
Amuna awiri adzakhala akulima mʼmunda; wina adzatengedwa ndi wina adzasiyidwa.”
37 And they answered, and saide to him, Where, Lord? And he said vnto them, Wheresoeuer the body is, thither shall also the eagles bee gathered together.
Iwo anafunsa kuti, “Ambuye, kodi zimenezi zidzachitikira kuti?” Iye anayankha kuti, “Kumene kuli mtembo, nʼkumene makwangwala amasonkhanako.”

< Luke 17 >