< Leviticus 7 >
1 Likewise this is the lawe of the trespasse offering, it is most holy.
“‘Malamulo a nsembe yopepesera kupalamula imene ndi nsembe yopatulika kwambiri ndi awa:
2 In the place where they kill the burnt offering, shall they kill the trespasse offering, and the blood thereof shall he sprinkle rounde about vpon the altar.
Nsembe yopepesera machimo iziphedwa pamalo pomwe amaphera nsembe yopsereza ndipo awaze magazi ake mbali zonse za guwa.
3 All the fat thereof also shall he offer, the rumpe, and the fat that couereth the inwardes.
Tsono apereke mafuta ake onse: mchira wamafuta ndi mafuta amene amakuta matumbo.
4 After he shall take away the two kidneis, with the fat that is on them and vpon the flankes, and the kall on the liuer with the kidneis.
Aperekenso impsyo ziwiri, mafuta ake pamodzi ndi mafuta onse amene ali chamʼchiwuno, ndiponso mafuta onse amene aphimba chiwindi.
5 Then the Priest shall burne them vpon the altar, for an offring made by fire vnto the Lord: this is a trespasse offring.
Wansembe azitenthe pa guwa kuti zikhale nsembe yotentha pa moto, yoperekedwa kwa Yehova. Imeneyi ndi nsembe yopepesera tchimo lopalamula.
6 All the males among the Priestes shall eate thereof, it shalbe eaten in the holy place, for it is most holy.
Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kudyako nsembeyo koma adyere ku malo opatulika. Imeneyi ndi nsembe yopatulika kwambiri.
7 As the sinne offring is, so is the trespasse offring, one lawe serueth for both: that wherewith the Priest shall make atonement, shalbe his.
“‘Nsembe yopepesera tchimo lopalamula ndi yofanana ndi nsembe yoperekedwa chifukwa cha tchimo. Ndipo nsembe ziwiri zonsezi zili ndi lamulo limodzi lokha. Wansembe amene wachita mwambo wa nsembe yopepesera machimo a kupalamula atenge nyamayo ngati yake.
8 Also the Priest that offereth any mans burnt offring, shall haue the skinne of the burnt offring which he hath offered.
Wansembe wopereka nsembe yopsereza ya munthu wina aliyense, atenge chikopa cha nsembe yopserezayo kuti chikhale chake.
9 And all the meate offring that is baken in the ouen, and that is dressed in the pan, and in the frying pan, shall be the Priestes that offereth it.
Chopereka chilichonse cha chakudya chophika mu uvuni kapena chokazinga mu mʼphika kapena mu chiwaya ndi cha wansembe amene wapereka nsembezo.
10 And euery meate offering mingled with oyle, and that is dry, shall pertaine vnto all the sonnes of Aaron, to all alike.
Ndipo chopereka china chilichonse cha chakudya chosakaniza ndi mafuta kapena chowuma, chikhale cha ana onse a Aaroni ndipo anawo achigawane mofanana.
11 Furthermore, this is the lawe of the peace offrings, which he shall offer vnto the Lord.
“‘Malamulo a nsembe ya chiyanjano imene munthu angathe kupereka kwa Yehova ndi awa:
12 If he offer it to giue thankes, then he shall offer for his thankes offering, vnleauened cakes mingled with oyle, and vnleauened wafers anointed with oyle, and fine floure fryed with the cakes mingled with oyle.
“‘Ngati munthuyo apereka chifukwa cha kuthokoza, apereke nsembeyo pamodzi ndi makeke wopanda yisiti, osakaniza ndi mafuta; timitanda ta buledi wopanda yisiti, topyapyala, topaka mafuta, ndiponso makeke a ufa wosalala wophikidwa bwino, wosakaniza ndi mafuta.
13 He shall offer also his offring with cakes of leauened bread, for his peace offrings, to giue thankes.
Pamodzi ndi nsembe yachiyanjano yothokozerayo abwerenso ndi makeke opangidwa ndi yisiti ngati chopereka chake.
14 And of all the sacrifice he shall offer one cake for an heaue offering vnto the Lord, and it shalbe the Priestes that sprinckleth the blood of the peace offrings.
Munthuyo atenge mtanda umodzi pa mtanda wa buledi wa mtundu uliwonse kuti ukhale nsembe yopereka kwa Yehova. Tsono mtanda umenewo ndi wake wa wansembe amene awaze magazi a nsembe yachiyanjano.
15 Also the flesh of his peace offerings, for thankesgiuing, shalbe eaten the same day that it is offered: he shall leaue nothing thereof vntill the morning.
Nyama ya nsembe yachiyanjano yothokozera idyedwe pa tsiku lomwe nsembeyo yaperekedwa ndipo isatsaleko mpaka mmawa.
16 But if the sacrifice of his offring be a vow, or a free offering, it shalbe eaten the same day that he offreth his sacrifice: and so in the morning the residue thereof shalbe eaten.
“‘Koma ngati nsembe yakeyo apereka chifukwa cha lumbiro kapena mwaufulu, nsembeyo adye tsiku lomwe yaperekedwalo. Koma yotsala angathe kuyidya mmawa mwake.
17 But as much of the offered flesh as remaineth vnto the third day, shalbe burnt with fire.
Ngati nyama ina ya nsembe yatsalabe mpaka tsiku lachitatu, imeneyo itenthedwe pa moto.
18 For if any of the flesh of his peace offrings be eaten in the third day, he shall not be accepted that offereth it, neither shall it be reckoned vnto him, but shalbe an abomination: therefore ye person that eateth of it shall beare his iniquitie.
Ngati munthu adya nyama yachiyanjano pa tsiku lachitatu, nsembeyo sidzalandiridwa. Amene wayipereka nsembeyo Mulungu sadzamulandira ndipo nsembeyo idzakhala yonyansa pamaso pa Mulungu, yosamupindulira kanthu woperekayo.
19 The flesh also that toucheth any vncleane thing, shall not be eaten, but burnt with fire: but of this flesh all that be cleane shall eate thereof.
“‘Nyama imene yakhudza chilichonse chodetsedwa, munthu asayidye, koma itenthedwe pa moto. Aliyense amene ali woyeretsedwa angathe kudya nyama inayo.
20 But if any eate of the flesh of the peace offerings that pertaineth to the Lord, hauing his vncleannesse vpon him, euen the same person shalbe cut off from his people.
Koma ngati munthu wina amene ndi wosayeretsedwa adya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, ameneyo achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.
21 Moreouer, whe any toucheth any vncleane thing, as the vncleannesse of man, or of an vncleane beast, or of any filthie abomination, and eate of the flesh of the peace offrings, which pertaineth vnto the Lord, euen that person shalbe cut off from his people.
Ndipo ngati munthu wina akhudza chinthu chodetsedwa, kaya chonyansa cha munthu kapena cha nyama, kapenanso chonyansa china chilichonse, ndipo kenaka nʼkudya nyama ya nsembe yachiyanjano imene ndi ya Yehova, munthu ameneyo achotsedwe pakati anthu a mtundu wake.’”
22 Againe ye Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
23 Speake vnto the children of Israel, and say, Ye shall eate no fat of beeues, nor of sheepe, nor of goates:
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Musadye mafuta a ngʼombe, nkhosa kapenanso mbuzi.
24 Yet the fat of the dead beast, and the fat of that, which is torne with beastes, shalbe occupied to any vse, but ye shall not eate of it.
Mafuta a nyama yofa yokha, kapena mafuta a nyama yophedwa ndi zirombo akhoza kuwagwiritsa ntchito iliyonse, koma inu musadye mafuta amenewo.
25 For whosoeuer eateth the fat of the beast, of the which he shall offer an offering made by fire to the Lord, euen the person that eateth, shalbe cut off from his people.
Pakuti munthu wakudya mafuta a nyama yoperekedwa kwa Yehova ngati nsembe yotentha pa moto, ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
26 Neither shall ye eate any blood, either of foule, or of beast in all your dwellings.
Ndipo kulikonse kumene mukakhale musakadye magazi a mbalame iliyonse kapena magazi a nyama iliyonse.
27 Euery person that eateth any blood, euen the same person shall be cut off from his people.
Ngati munthu aliyense adya magazi achotsedwe pakati pa anthu a mtundu wake.’”
28 And the Lord talked with Moses, saying,
Yehova anayankhula ndi Mose kuti,
29 Speake vnto the children of Israel, and say, Hee that offereth his peace offerings vnto the Lord, shall bring his gifte vnto the Lord of his peace offerings:
“Awuze Aisraeli kuti, Aliyense amene apereka nsembe yachiyanjano kwa Yehova, abwere ndi gawo la nsembeyo kwa Yehova.
30 His handes shall bring the offerings of the Lord made by fire: euen the fatte with the breast shall he bring, that the breast may be shaken to and from before the Lord.
Atenge ndi manja ake zigawo za chopereka zoyenera kuzitentha pa moto ngati chopereka kwa Yehova. Abweretse mafuta, pamodzi ndi chidale chomwe, ndipo chidalecho achiweyule kuti chikhale chopereka choweyula kwa Yehova.
31 Then the Priest shall burne the fatte vpon the Altar, and the breast shall be Aarons and his sonnes.
Wansembe atenthe mafutawo pa guwa koma chidalecho chikhale cha Aaroni ndi ana ake.
32 And the right shoulder shall ye giue vnto the Priest for an heaue offering, of your peace offrings.
Mumupatse wansembe ntchafu ya kumanja ya nsembe yanu yachiyanjano kuti ikhale chopereka chanu kwa iye.
33 The same that offreth the blood of ye peace offrings, and the fatte, among the sonnes of Aaron, shall haue the right shoulder for his parte.
Mwana wa Aaroni amene amapereka magazi ndi mafuta a nsembe yachiyanjano, adzitenga ntchafu ya kumanja kukhala gawo lake.
34 For the breast shaken to and from, and the shoulder lifted vp, haue I taken of the children of Israel, euen of their peace offrings, and haue giuen them vnto Aaron the Priest and vnto his sonnes by a statute for euer from among the children of Israel.
Choncho pa zopereka zachiyanjano za Aisraeli, Ine ndatengapo chidale chomwe amaweyula ndi ntchafu zimene amapereka nsembe ndipo ndazipereka kwa wansembe Aaroni ndi ana ake. Izi ndizo gawo lawo nthawi zonse pa zopereka za Aisraeli.”
35 This is the anointing of Aaron, and the anointing of his sonnes, concerning the offerings of the Lord made by fire, in the day when he presented them to serue in the Priestes office vnto the Lord.
Zimenezi ndi chigawo cha Aaroni ndi ana ake chotapidwa pa zopereka kwa Yehova zoti zitenthedwe pa moto zimene zinaperekedwa pa tsiku limene anapatulidwa kuti akhale ansembe otumikira Yehova.
36 The which portions the Lord commanded to giue them in the day that he anointed them from among the children of Israel, by a statute for euer in their generations.
Yehova ndiye analamulira kuti pa zopereka za Aisraeli azitapapo zimenezi ndi kuwapatsa ansembe ngati gawo lawo. Yehovayo analamula zimenezi pa tsiku limene ansembewo anapatulidwa ndipo anachikhazikitsa ngati lamulo la nthawi zonse.
37 This is also the lawe of the burnt offring of the meate offring, and of the sinne offring, and of the trespasse offring, and of the consecrations, and of the peace offrings,
Awa ndi malamulo a nsembe izi: nsembe yopsereza, nsembe yachakudya, nsembe yopepesera machimo, nsembe yopepesera kupalamula, nsembe ya mwambo wodzoza ndi nsembe yachiyanjano.
38 Which the Lord commanded Moses in the mount Sinai, when he commanded the children of Israel to offer their giftes vnto the Lord in the wildernesse of Sinai.
Malamulo amenewa Yehova anapereka kwa Mose pa Phiri la Sinai pa tsiku limene Yehova analamulira Aisraeli kuti abwere ndi zopereka za kwa Yehova, ku chipululu cha Sinai kuja.