< Leviticus 27 >
1 Moreouer the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speake vnto the children of Israel, and say vnto them, If any man shall make a vowe of a person vnto the Lord, by thy estimation,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati munthu anachita lumbiro lapadera loti adzapereka munthu mnzake kwa Yehova ndipo akufuna kuti amuwombole,
3 Then thy estimation shall bee thus: a male from twentie yeere olde vnto sixty yeere olde shalbe by thy estimation euen fifty shekels of siluer, after the shekel of the Sanctuarie.
mtengo wake ukhale masekeli a siliva makumi asanu, molingana ndi kawerengedwe ka ku Nyumba ya Mulungu, ngati munthuyo ndi wamwamuna wa zaka zapakati pa 20 ndi 60.
4 But if it be a female, then thy valuation shall be thirtie shekels.
Ndipo ngati ndi wamkazi, mtengo wake ukhale masekeli makumi atatu.
5 And from fiue yere old to twentie yere olde thy valuation shall be for the male twentie shekels, and for the female ten shekels.
Mtengo wa munthu wamwamuna wa zaka zapakati pa zisanu ndi makumi awiri ukhale masekeli makumi awiri ndipo munthu wamkazi ukhale masekeli khumi.
6 But from a moneth old vnto fiue yere old, thy price of the male shall bee fiue shekels of siluer, and thy price of the female, three shekels of siluer.
Ngati ndi munthu wamwamuna wa pakati pa mwezi umodzi ndi zaka zisanu, mtengo wa munthu wamwamuna ukhale masekeli asanu a siliva ndipo ngati ndi wamkazi, ukhale masekeli atatu a siliva.
7 And from sixty yeere olde and aboue, if he be a male, then thy price shalbe fifteene shekels, and for the female ten shekels.
Ngati ndi munthu wa zaka makumi asanu ndi limodzi kapena kuposerapo, mtengo wa wamwamuna ukhale masekeli khumi ndi asanu, ndipo wamkazi ukhale masekeli khumi.
8 But if he be poorer then thou hast esteemed him, then shall hee present himselfe before the Priest, and the Priest shall value him, according to the abilitie of him that vowed, so shall the Priest value him.
Ngati munthu amene anachita lumbiro ndi wosauka kwambiri kuti sangathe kulipira ndalama zimenezo, abwere ndi munthu woperekedwa uja kwa wansembe, ndipo wansembeyo ayike mtengo woti munthu wolumbirayo angathe kulipira.
9 And if it be a beast, whereof men bring an offering vnto the Lord, all that one giueth of such vnto the Lord, shalbe holy.
“‘Ngati chimene anachitira lumbiro kuti apereke ndi nyama imene amapereka kukhala nsembe kwa Yehova, zonse zimene amapereka kwa Yehova nʼzopatulika.
10 He shall not alter it nor change it, a good for a badde, nor a badde for a good: and if hee change beast for beast, then both this and that, which was changed for it, shall be holy.
Munthu asasinthanitse ndi ina kapena kupereka ina yabwino mʼmalo mwa yoyipa, kapena yoyipa mʼmalo mwa yabwino. Ngati asinthitsa nyama ina mʼmalo mwa ina, nyamayo pamodzi ndi inzake wasinthitsayo zikhala zopatulika.
11 And if it be any vncleane beast, of which men do not offer a sacrifice vnto the Lord, hee shall then present the beast before the Priest.
Ngati chimene anachitira lumbiro ndi nyama yodetsedwa, nyama imene siloledwa kuyipereka kukhala nsembe kwa Yehova, nyamayo abwere nayo kwa wansembe,
12 And the Priest shall value it, whether it be good or bad: and as thou valuest it, which art the Priest, so shall it bee.
ndipo wansembeyo atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
13 But if he will bye it againe, then hee shall giue the fift part of it more, aboue thy valuation.
Ngati mwini wakeyo akufuna kuwombola nyamayo, awonjezere pa mtengo wake wa nyamayo chimodzi mwa zigawo zisanu zamtengowo.
14 Also whe a man shall dedicate his house to be holy vnto the Lord, then the Priest shall value it, whether it be good or bad, and as ye Priest shall prise it, so shall the value be.
“‘Ngati munthu apereka nyumba yake kuti ikhale yopatulika kwa Yehova, wansembe atchule mtengo wake poona ngati ndi yabwino kapena ndi yoyipa. Mtengo umene wansembe atchule ndiwo udzakhale mtengo wake.
15 But if he that sanctified it, will redeeme his house, then hee shall giue thereto the fift part of money more then thy estimation, and it shalbe his.
Ngati munthu amene wapereka nyumbayo afuna kuyiwombola nyumbayo, awonjezere pamtengo wake wa nyumbayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ndipo nyumbayo idzakhalanso yake.
16 If also a man dedicate to the Lord any grounde of his inheritance, then shalt thou esteeme it according to the seede therof: an Homer of barlie seede shalbe at fiftie shekels of siluer.
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova mbali ina ya malo a makolo ake, mtengo umene awuyike ukhale wolingana ndi mtengo wa mbewu zimene zimadzabzalidwamo. Zikhale mbewu za barele za makilogalamu makumi awiri ndipo mtengo wake ukhale masekeli makumi asanu.
17 If he dedicate his field immediatly from the yeere of Iubile, it shall bee worth as thou doest esteeme it.
Ngati munthu apereka munda wake kuyambira chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mtengo wake ukhale umene unakhazikitsidwa.
18 But if hee dedicate his fielde after the Iubile, then the Priest shall recken him the money according to ye yeeres that remaine vnto the yere of Iubile, and it shalbe abated by thy estimation.
Koma ngati apereka mundawo chaka chokondwerera zaka makumi asanu chitapita, wansembe adzatchula mtengo molingana ndi zaka zomwe zatsala kuti chifike chaka china chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo mtengo wake udzakhala wotsikirapo.
19 And if he that dedicateth it, will redeeme the fielde, then he shall put the fift parte of the price, that thou esteemedst it at, thereunto, and it shall remaine his.
Ngati munthu amene wapereka munda afuna kuwuwombola, ayenera kuwonjezera pa mtengo wake wa mundawo, limodzi mwa magawo asanu a mtengowo. Ndipo mundawo udzakhalanso wake.
20 And if he will not redeeme the fielde, but the Priest sell the fielde to another man, it shalbe redeemed no more.
Koma ngati sawuwombola mundawo, kapena ngati waugulitsa kwa munthu wina, mundawo sudzawomboledwanso.
21 But the field shalbe holy to the Lord, whe it goeth out in the Iubile, as a fielde separate from common vses: the possession thereof shall be the Priests.
Mwini mundawo akawusiya mʼchaka chokondwerera zaka makumi asanu ndiye kuti mundawo udzakhala wopatulika monga woperekedwa kwa Yehova: udzakhala munda wa ansembe.
22 If a man also dedicate vnto ye Lord a fielde which he hath bought, which is not of the groud of his inheritance,
“‘Ngati munthu apereka kwa Yehova munda umene anagula, umene si malo a makolo ake,
23 Then the Priest shall set the price to him, as thou esteemest it, vnto the yeere of Iubile, and he shall giue thy price the same day, as a thing holy vnto the Lord.
wansembe atchule mtengo wake kufikira pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, ndipo munthuyo apereke ndalama zokwanira mtengo wake pa tsikulo monga ndalama zopatulika kwa Yehova.
24 But in the yeere of Iubile, the fielde shall returne vnto him, of whome it was bought: to him, I say, whose inheritance the land was.
Pa chaka chokondwerera zaka makumi asanu, mundawo udzabwezedwa kwa munthu amene anawugulitsayo, amene malowo anali ake.
25 And all thy valuation shall bee according to the shekel of the Sanctuarie: a shekel conteyneth twenty gerahs.
Potchula mtengo uliwonse wansembe awerengere molingana ndi mtengo wa sekeli wa ku Nyumba ya Mulungu: magera makumi awiri pa sekeli imodzi.
26 Notwithstanding the first borne of the beastes, because it is the Lordes first borne, none shall dedicate such, be it bullocke, or sheepe; for it is the Lords.
“‘Koma pasapezeke munthu wopereka mwana woyamba kubadwa wa nyama, popeza mwana woyamba kubadwa ali kale wa Yehova, kaya ndi ngʼombe kapena nkhosa, zimenezi ndi za Yehova.
27 But if it be an vncleane beast, then he shall redeeme it by thy valuation, and giue the fift part more thereto: and if it be not redeemed, then it shalbe solde, according to thy estimation.
Ngati ili nyama yodetsedwa, ayiwombole pa mtengo umene wansembe wawuyika, ndi kuwonjezeranso pa mtengo wake wa nyamayo, limodzi mwa magawo asanu amtengowo. Ngati sayiwombola, igulitsidwe pa mtengo umene wansembe awuyike.
28 Notwithstanding, nothing separate from the common vse that a man doeth separate vnto the Lord of all that he hath (whether it bee man or beast, or lande of his inheritance) may be solde nor redeemed: for euery thing separate from the common vse is most holy vnto the Lord.
“‘Koma chinthu chilichonse choperekedwa kwa Yehova, kaya ndi munthu, nyama, kaya ndi malo a makolo, chimenechi chisagulitsidwe kapena kuwomboledwa. Choperekedwa kwa Yehova motere nʼchopatulika kwambiri.
29 Nothing separate from the common vse, which shall be separate from man, shalbe redeemed, but dye the death.
“‘Munthu amene waperekedwa kotheratu sangawomboledwe. Munthuyo ayenera kuphedwa.
30 Also all the tithe of the lande both of the seede of the ground, and of the fruite of the trees is the Lords: it is holy to the Lord.
“‘Chakhumi chilichonse chochokera mʼdziko, kaya ndi tirigu wochokera mʼnthaka kapena chipatso cha mʼmitengo ndi za Yehova. Chimenecho ndi chopatulika kwa Yehova.
31 But if a man will redeeme any of his tithe, he shall adde the fift part thereto.
Ngati munthu afuna kuwombola chakhumi chilichonse, awonjezere pamtengo wake chimodzi mwa zigawo zisanu za mtengowo.
32 And euery tithe of bullock, and of sheepe, and of all that goeth vnder the rod, the tenth shalbe holy vnto the Lord.
Chakhumi cha ngʼombe ndi nkhosa, kapena kuti nyama iliyonse ya khumi imene mʼbusa wayiwerenga idzakhala yopatulikira kwa Yehova.
33 He shall not looke if it be good or bad, neither shall he change it: els if he change it, both it, and that it was changed withall, shalbe holy, and it shall not be redeemed.
Palibe amene adzaloledwa kusankha nyama yomwe ili yabwino kapena kusinthitsa. Ngati asinthitsa, nyamayo pamodzi ndi inzakeyo zidzakhala zopatulika ndipo sangaziwombole.’”
34 These are the commandements which the Lord commanded by Moses vnto the children of Israel in mount Sinai.
Amenewa ndi malamulo amene Yehova anamupatsa Mose pa Phiri la Sinai kuti awuze Aisraeli.