< Leviticus 23 >
1 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speake vnto the children of Israel, and say vnto them, The feastes of ye Lord which yee shall call ye holie assemblies, euen these are my feasts.
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Awa ndi masiku anga osankhika a chikondwerero, masiku osankhika olemekeza Yehova amene uyenera kulengeza kuti akhale masiku opatulika a misonkhano.
3 Six daies shall worke be done, but in the seuenth day shalbe the Sabbath of rest, an holie conuocation: ye shall do no worke therein, it is the Sabbath of the Lord, in all your dwellings.
“‘Pa masiku asanu ndi limodzi muzigwira ntchito, koma tsiku lachisanu ndi chiwiri ndi Sabata lopuma, tsiku la msonkhano wopatulika. Kulikonse kumene inu mukukhala musamagwire ntchito iliyonse tsiku limeneli popeza ndi tsiku la Sabata la Yehova.
4 These are the feastes of the Lord, and holie conuocations, which yee shall proclaime in their seasons.
“‘Awa ndiwo masiku osankhidwa a zikondwerero za Yehova, masiku woyera a misonkhano amene muti mudzalengeze pa nthawi yake:
5 In the first moneth, and in the fourteenth day of the moneth at euening shalbe ye Passeouer of the Lord.
Chikondwerero cha Paska chiziyamba madzulo a tsiku la 14 la mwezi woyamba.
6 And on the fifteenth day of this moneth shalbe the feast of vnleauened bread vnto the Lord: seuen dayes ye shall eate vnleauened bread.
Tsiku la 15 la mwezi womwewo ndi tsiku lolemekeza Yehova ndipo muziyamba Chikondwerero cha Buledi Wopanda Yisiti. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
7 In the first day yee shall haue an holy conuocation: ye shall do no seruile worke therein.
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika. Musamagwire ntchito iliyonse.
8 Also ye shall offer sacrifice made by fire vnto the Lord seuen daies, and in the seuenth day shalbe an holie conuocation: ye shall do no seruile worke therein.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito yolemetsa.’”
9 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
10 Speake vnto the children of Israel, and say vnto them, When ye be come into ye land which I giue vnto you, and reape the haruest thereof, then ye shall bring a sheafe of the first fruites of your haruest vnto the Priest,
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Mukakalowa mʼdziko limene ndikukupatsanilo ndi kukolola za mʼminda mwanu, mudzabwere kwa wansembe ndi mtolo wa tirigu woyambirira kucha wa mʼminda mwanu.
11 And hee shall shake the sheafe before the Lord, that it may be acceptable for you: the morowe after the Sabbath, the Priest shall shake it.
Wansembeyo auweyule mtolowo pamaso pa Yehova kotero mtolowo udzalandiridwa mʼmalo mwanu. Wansembe auweyule tsiku lotsatana ndi la Sabata.
12 And that day when yee shake the sheafe, shall yee prepare a lambe without blemish of a yeere olde, for a burnt offring vnto the Lord:
Pa tsiku limene muweyula mtolowo, muperekenso mwana wankhosa wa mwamuna wa chaka chimodzi, wopanda chilema kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
13 And the meate offring thereof shalbe two tenth deales of fine floure mingled with oyle, for a sacrifice made by fire vnto ye Lord of sweete sauour. and the drinke offring thereof the fourth part of an Hin of wine.
Chopereka chachakudya chake chikhale cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta kuti chikhale nsembe yopsereza yopereka kwa Yehova, ya fungo lokoma. Ndipo chopereka cha chakumwa chake chikhale vinyo wa malita anayi ndi theka.
14 And ye shall eat neither bread nor parched corne, nor greene eares vntill the selfe same day that ye haue brought an offring vnto your God: this shalbe a lawe for euer in your generations and in all your dwellings.
Musadye buledi aliyense kapena tirigu wokazinga, kapena wamuwisi mpaka tsiku limene mwabwera ndi chopereka ichi kwa Mulungu wanu. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
15 Ye shall count also to you from the morowe after the Sabbath, euen from the day that yee shall bring the sheafe of the shake offring, seuen Sabbaths, they shalbe complete.
“‘Kuyambira tsiku lotsatana ndi la Sabata lija, tsiku limene munabwera ndi mtolo wa nsembe yoweyula, muziwerenga masabata asanu ndi awiri athunthu.
16 Vnto ye morow after the seuenth Sabbath shall ye nomber fiftie dayes: then yee shall bring a newe meate offring vnto the Lord.
Ndiye kuti muwerenge masiku makumi asanu kuchokera pa tsiku lotsatana ndi Sabata la chisanu ndi chiwiri, ndipo kenaka mupereke nsembe ya tirigu watsopano kwa Yehova.
17 Ye shall bring out of your habitations bread for the shake offring: they shalbe two loaues of two tenth deales of fine floure, which shalbe baken with leauen for first fruites vnto the Lord.
Kuchokera kulikonse kumene mukukhala, mubwere pamaso pa Yehova ndi buledi muwiri wa ufa wosalala wa makilogalamu awiri, ophikidwa ndi yisiti kuti akhale nsembe yoweyula ya zakudya zoyamba kucha.
18 Also yee shall offer with the bread seuen lambes without blemish of one yeere olde, and a yong bullocke and two rams: they shalbe for a burnt offring vnto the Lord, with their meate offrings and their drinke offrings, for a sacrifice made by fire of a sweete sauour vnto the Lord.
Pamodzi ndi bulediyu muperekenso ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri, aliyense akhale wa chaka chimodzi ndi wopanda chilema. Pakhalenso ngʼombe yayingʼono yayimuna ndi nkhosa zazimuna ziwiri. Zimenezi zidzakhala nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova pamodzi ndi nsembe za zakudya ndi nsembe za zakumwa. Zonsezi zikhale nsembe zopsereza za fungo lokomera Yehova.
19 Then ye shall prepare an hee goate for a sinne offring, and two lambes of one yeere olde for peace offrings.
Kenaka mupereke mbuzi imodzi yayimuna kuti ikhale nsembe yopepesera machimo ndiponso ana ankhosa awiri, aliyense wa chaka chimodzi kuti akhale nsembe yachiyanjano.
20 And the Priest shall shake them to and from with the bread of the first fruits before the Lord, and with the two lambes: they shalbe holy to the Lord, for the Priest.
Wansembe aweyule ana ankhosa awiriwo pamaso pa Yehova monga nsembe yoweyula, pamodzi ndi buledi wa tirigu woyambirira kucha. Zimenezi ndi zopereka zopatulika za Yehova zopatsidwa kwa ansembe.
21 So ye shall proclayme the same day, that it may be an holie conuocation vnto you: ye shall doe no seruile worke therein: it shalbe an ordinance for euer in al your dwellinges, throughout your generations.
Pa tsiku lomwelo mulengeze za msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
22 And when you reape the haruest of your land, thou shalt not rid cleane the corners of thy field when thou reapest, neither shalt thou make any aftergathering of thy haruest, but shalt leaue them vnto the poore and to the stranger: I am the Lord your God.
“‘Pamene mukukolola zinthu mʼmunda mwanu, musakolole munda wanu mpaka mʼmalire mwenimweni, ndipo musatole khunkha lake. Zimenezo musiyire anthu osauka ndi alendo. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
23 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
24 Speake vnto the children of Israel, and say, In the seuenth moneth, and in the first day of the moneth shall ye haue a Sabbath, for the remembrance of blowing the trumpets, an holy conuocation.
“Uza Aisraeli kuti, ‘Tsiku loyamba la mwezi wachisanu ndi chiwiri, likhale tsiku lopumula, la msonkhano wopatulika, mulilengeze poyimba lipenga.
25 Ye shall do no seruile worke therein, but offer sacrifice made by fire vnto the Lord.
Musagwire ntchito zolemetsa koma mupereke nsembe yopsereza kwa Yehova.’”
26 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
27 The tenth also of this seuenth moneth shalbe a day of reconciliation: it shalbe an holie conuocation vnto you, and yee shall humble your soules, and offer sacrifice made by fire vnto the Lord.
“Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu ndi chiwiri ndi tsiku lochita Mwambo Wopepesera Machimo. Muzichita msonkhano wopatulika. Muzidzichepetsa pamaso pa Yehova ndi kupereka nsembe zopsereza kwa Yehova.
28 And ye shall doe no worke that same day: for it is a day of reconciliation, to make an atonement for you before the Lord your God.
Tsiku limeneli musamagwire ntchito chifukwa ndi tsiku la Mwambo Wopepesera Machimo, kupepesera machimo anu pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
29 For euery person that humbleth not himselfe that same day, shall euen be cut off from his people.
Munthu aliyense amene sasala zakudya pa tsiku limeneli ayenera kuchotsedwa pakati pa anthu a mtundu wake.
30 And euery person that shall doe any work that same day, the same person also will I destroy from among his people.
Aliyense wogwira ntchito tsiku limeneli ndidzamuwononga pakati pa anthu a mtundu wake.
31 Ye shall do no maner worke therefore: this shalbe a law for euer in your generations, throughout all your dwellings.
Inu musadzagwire ntchito iliyonse. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse, kulikonse kumene mukakhale.
32 This shalbe vnto you a Sabbath of rest, and ye shall humble your soules: in the ninth day of the moneth at euen, from euen to euen shall ye celebrate your Sabbath.
Limeneli kwa inu ndi tsiku la Sabata lopumula, ndipo muyenera kusala zakudya. Kuyambira madzulo a tsiku lachisanu ndi chinayi la mwezi mpaka madzulo ena otsatirawo muzisunga tsikulo ngati Sabata lanu.”
33 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
34 Speake vnto the children of Israel, and say, In the fifteenth day of this seueth moneth shalbe for seuen dayes the feast of Tabernacles vnto the Lord.
“Uwawuze Aisraeli kuti pa masiku asanu ndi awiri kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri pazikhala Chikondwerero cha Misasa cholemekeza Yehova.
35 In the first day shalbe an holie conuocation: ye shall do no seruile worke therein.
Tsiku loyamba ndi la msonkhano wopatulika, musagwire ntchito zolemetsa.
36 Seuen daies ye shall offer sacrifice made by fire vnto the Lord, and in the eight day shalbe an holy conuocation vnto you, and ye shall offer sacrifices made by fire vnto the Lord: it is the solemne assemblie, yee shall doe no seruile worke therein.
Pa masiku asanu ndi awiri muzipereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Ndipo pa tsiku lachisanu ndi chitatu muzikhala ndi msonkhano wopatulika ndipo muzipereka nsembe yopsereza kwa Yehova. Kumeneku ndi kutsekera kwa msonkhano waukulu. Musagwire ntchito zolemetsa.
37 These are the feastes of the Lord (which ye shall call holie conuocations) to offer sacrifice made by fire vnto the Lord, as burnt offring, and meate offring, sacrifice, and drinke offrings, euery one vpon his day,
(“‘Amenewa ndi masiku osankhika a chikondwerero cha Yehova, amene muziwalengeza kuti ndi nthawi ya msonkhano wopatulika. Masiku amenewa muzipereka nsembe zopsereza, nsembe za chakudya, nsembe zanyama ndi zopereka zachakumwa za tsiku ndi tsiku.
38 Beside the Sabbaths of the Lord, and beside your giftes, and beside al your vowes, and beside all your free offrings, which ye shall giue vnto the Lord.
Zopereka zimenezi ndi zowonjezera pa zopereka za Yehova za pa Sabata, zopereka zanu zolumbira ndiponso mphatso zanu zaufulu zopereka kwa Yehova.)
39 But in the fifteenth day of the seueth moneth, when ye haue gathered in the fruite of the land, ye shall keepe an holie feast vnto the Lord seuen daies: in the first day shalbe a Sabbath: likewise in the eight day shalbe a Sabbath.
“‘Choncho kuyambira pa tsiku la 15 la mwezi wachisanu ndi chiwiri, mutakolola zinthu mʼmunda mwanu, muchite chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Tsiku loyamba ndi tsiku lopumula, ndipo tsiku lachisanu ndi chitatu ndi lopumulanso.
40 And yee shall take you in the first day the fruite of goodly trees, branches of palme trees, and the boughes of thicke trees, and willowes of the brooke, and shall reioyce before the Lord your God seuen daies.
Pa tsiku loyamba muzitenga zipatso zabwino kwambiri zothyola mʼmitengo, nthambi za kanjedza, nthambi zazikulu za mitengo ya masamba ambiri, ndi za misondozi yakumtsinje, ndipo muzikondwera pamaso pa Yehova Mulungu wanu kwa masiku asanu ndi awiri.
41 So ye shall keepe this feast vnto the Lord seuen daies in the yere, by a perpetuall ordinance through your generations: in the seuenth moneth shall you keepe it.
Chaka chilichonse muzichita chikondwerero cha Yehova kwa masiku asanu ndi awiri. Limeneli ndi lamulo lamuyaya pa mibado yanu yonse. Muzichita chikondwerero chimenechi mwezi wachisanu ndi chiwiri.
42 Ye shall dwell in boothes seuen daies: all that are Israelites borne, shall dwel in boothes,
Muzikhala mʼmisasa masiku asanu ndi awiri. Onse amene ali mbadwa mʼdziko la Israeli azikhala mʼmisasa
43 That your posterity may know that I haue made the children of Israel to dwell in boothes, when I brought them out of the lande of Egypt: I am the Lord your God.
kuti zidzukulu zanu zidzadziwe kuti ndine amene ndinakhazika Aisraeli mʼmisasa nditawatulutsa ku Igupto. Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’”
44 So Moses declared vnto the children of Israel the feastes of the Lord.
Choncho Mose analengeza kwa Aisraeli masiku osankhika a zikondwerero za Yehova.