< Leviticus 22 >

1 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speake vnto Aaron, and to his sonnes, that they be separated from the holy thinges of the children of Israel, and that they pollute not mine holy name in those things, which they hallowe vnto me: I am the Lord.
“Uza Aaroni ndi ana ake kuti azilemekeza zinthu zopatulika zimene Aisraeli azipereka kwa Ine, kuti asayipitse dzina langa loyera. Ine ndine Yehova.
3 Say vnto them, Whosoeuer he be of all your seede among your generations after you, that toucheth the holy things which the children of Israel hallowe vnto the Lord, hauing his vncleannesse vpon him, euen that person shall be cut off from my sight: I am the Lord.
“Uwawuze kuti ngati wina aliyense mwa zidzukulu zawo mʼmibado yonse imene ikubwera adzayandikira zinthu zopatulika zimene ana a Israeli apereka kwa Yehova, ali wodetsedwa, ameneyo achotsedwe pamaso pa Yehova. Ine ndine Yehova.
4 Whosoeuer also of the seede of Aaron is a leper, or hath a running issue, he shall not eate of the holy things vntill he be cleane: and who so toucheth any that is vncleane, by reason of the dead, or a man whose issue of seede runneth from him,
“Munthu aliyense mwa zidzukulu za Aaroni amene ali ndi khate kapena amatulutsa zoyipa mʼthupi mwake, asadye zinthu zopatulika mpaka atayeretsedwa. Wansembe angakhale wodetsedwa atakhudzana ndi chinthu chimene chadetsedwa ndi chinthu chakufa kapena kukhudza munthu amene wataya umuna,
5 Or the man that toucheth any creeping thing, whereby he may be made vncleane, or a man, by whom he may take vncleannesse, whatsoeuer vncleannesse he hath,
kapena kukhudza chilichonse chokwawa chomwe chimadetsa munthu, kapena kukhudza munthu amene angamudetse, kapenanso kukhudza kanthu kena kalikonse kodetsedwa.
6 The person that hath touched such, shall therefore be vncleane vntill the euen, and shall not eat of ye holy things, except he haue washed his flesh with water.
Tsono ngati wansembe angakhudze chilichonse mwa zimenezi ndiye kuti adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Asadye chopereka chilichonse chopatulika mpaka atasamba thupi lake lonse.
7 But when the Sunne is downe, hee shalbe cleane, and shall afterward eate of the holy things: for it is his foode.
Munthuyo adzakhala woyeretsedwa pamene dzuwa lalowa, ndipo angathe kudya chopereka chopatulikacho popeza ndi chakudya chake.
8 Of a beast that dyeth, or is rent with beasts, whereby he may be defiled, hee shall not eate: I am the Lord.
Wansembe sayenera kudya chinthu chofa chokha kapena chojiwa ndi chirombo kuopa kuti angadzidetse ndi chakudyacho. Ine ndine Yehova.
9 Let them keepe therefore mine ordinance, least they beare their sinne for it, and die for it, if they defile it: I the Lord sanctifie them.
“‘Choncho ansembe azisunga malamulo angawa kuti asapezeke wolakwa ndi kufa chifukwa chopeputsa malamulowa. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.
10 There shall no stranger also eate of the holie thing, neither the ghest of the Priest, neither shall an hired seruant eat of the holie thing:
“‘Aliyense amene si wabanja la wansembe, kaya ndi mlendo wa wansembe, kapena wantchito wake, asadye chopereka chopatulika.
11 But if the Priest bye any with money, he shall eate of it, also he that is borne in his house: they shall eate of his meate.
Koma kapolo amene wagulidwa ndi ndalama kapena kubadwira mʼbanja la wansembe angathe kudya chakudya cha wansembeyo.
12 If the Priests daughter also be maried vnto a stranger, she may not eate of the holy offrings.
Mwana wamkazi wa wansembe amene wakwatiwa ndi munthu amene si wansembe, asadyeko nsembe zopatulikazo.
13 Notwithstanding if the Priests daughter be a widowe or diuorced, and haue no childe, but is returned vnto her fathers house shee shall eate of her fathers bread, as she did in her youth but there shall no stranger eate thereof.
Koma mwana wamkazi wa wansembe amene ali wamasiye kapena wosudzulidwa, ndipo alibe mwana, komanso anabwerera ku nyumba ya abambo ake monga pa nthawi ya utsikana wake, angathe kudya chakudya cha abambo ake. Mlendo asadye chakudya chopatulika.
14 If a man eate of the holie thing vnwittingly, he shall put the fift part thereunto, and giue it vnto the Priest with the halowed thing.
“‘Ngati munthu wina aliyense adya chopereka chopatulika mosadziwa, munthuyo amubwezere wansembe chinthu chopatulikacho ndipo awonjezerepo limodzi la magawo asanu a chinthucho.
15 So they shall not defile the holy things of the children of Israel, which they offer vnto the Lord,
Choncho ansembe asayipitse zopereka zopatulika za Aisraeli zimene apereka kwa Yehova
16 Neither cause the people to beare the iniquitie of their trespas, while they eate their holy thing: for I the Lord do halowe them.
ndipo asachimwitse ndi kupalamulitsa Aisraeli powalola kudya zakudya zawo zopatulika. Ine ndine Yehova amene ndimawayeretsa.’”
17 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
18 Speake vnto Aaron, and to his sonnes, and to all the children of Israel, and say vnto them, Whosoeuer he be of the house of Israel, or of the strangers in Israel, that will offer his sacrifice for all their vowes, and for all their free offrings, which they vse to offer vnto the Lord for a burnt offring,
“Yankhula ndi Aaroni, ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse, ndipo uwawuze kuti, ‘Ngati wina aliyense wa inu, Mwisraeli kapena mlendo amene akukhala mu Israeli abwera ndi mphatso ya nsembe yopsereza kwa Yehova, kupereka chimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu,
19 Yee shall offer of your free minde a male without blemish of the beeues, of the sheepe, or of the goates.
ndiye kuti abwere ndi ngʼombe yayimuna, nkhosa yayimuna kapena mbuzi yayimuna. Izi zikhale zopanda chilema kuti zilandiridwe.
20 Ye shall not offer any thing that hath a blemish: for that shall not be acceptable for you.
Musapereke nyama iliyonse yokhala ndi chilema chifukwa sidzalandiridwa mʼmalo mwanu.
21 And whosoeuer bringeth a peace offring vnto ye Lord to accomplish his vowe, or for a free offring, of the beeues, or of the sheepe, his free offring shall bee perfect, no blemish shalbe in it.
Pamene wina aliyense abweretsa ngʼombe kapena nkhosa kuti ikhale nsembe yachiyanjano kwa Yehova, kukwaniritsa zimene analumbira kapena kuti ikhale nsembe yaufulu, nyamayo iyenera kukhala yangwiro ndi yopanda chilema kuti ilandiridwe.
22 Blinde, or broken, or maimed, or hauing a wenne, or skiruie, or skabbed: these shall yee not offer vnto the Lord nor make an offring by fire of these vpon the altar of the Lord.
Musapereke kwa Yehova nyama zakhungu, zovulala kapena zolumala, kapena nyama zimene zikutulutsa mafinya mʼthupi mwake, kapena zimene zili ndi nthenda yonyerenyetsa, kapena zimene zili ndi mphere. Nyama zotere musaziyike pa guwa kuti zikhale nsembe yopsereza kwa Yehova.
23 Yet a bullocke, or a sheepe that hath any member superfluous, or lacking, such mayest thou present for a free offring, but for a vowe it shall not be accepted.
Koma mungathe kupereka ngʼombe yayimuna kapena nkhosa imene ili ndi chiwalo chachitali kapena chachifupi kukhala nsembe yaufulu. Koma simungayipereke ngati nsembe yoperekera zimene munalumbirira chifukwa sidzalandiridwa.
24 Ye shall not offer vnto ye Lord that which is bruised or crusshed, or broken, or cut away, neither shall ye make an offring thereof in your land,
Nyama iliyonse imene mavalo ake ndi onyuka kapena ophwanyika, ongʼambika kapena oduka, musamayipereke kwa Yehova mʼdziko lanu.
25 Neither of ye hand of a strager shall ye offer ye bread of your God of any of these, because their corruption is in them, there is a blemish in them: therefore shall they not be accepted for you.
Ndipo musalandire nyama zotere kuchokera kwa mlendo ndi kuzipereka kukhala zakudya za Mulungu wanu. Zimenezi sizidzalandiridwa mʼmalo mwanu chifukwa zili ndi chilema ndipo ndi zolumala.’”
26 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
27 When a bullocke, or a sheepe, or a goate shall be brought foorth, it shalbe euen seuen daies vnder his damme: and from the eight day forth, it shalbe accepted for a sacrifice made by fire vnto the Lord.
“Pamene mwana wangʼombe, mwana wankhosa kapena mwana wambuzi wabadwa, akhale ndi make kwa masiku asanu ndi awiri. Kuyambira tsiku lachisanu ndi chitatu mpaka mʼtsogolo mwake, angathe kulandiridwa kuti akhale nsembe yopsereza ya kwa Yehova.
28 As for the cowe or the ewe, yee shall not kill her, and her yong both in one day.
Musaphe ngʼombe kapena nkhosa pamodzi ndi mwana wake tsiku limodzi. Muyidye pa tsiku lomwelo; musasiyeko ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
29 So when ye will offer a thanke offring vnto the Lord, ye shall offer willingly.
“Pamene mupereka nsembe yoyamika kwa Yehova, muyipereke mwakufuna kwanu mu njira yoti ilandiridwe mʼmalo mwanu.
30 The same day it shalbe eaten, yee shall leaue none of it vntill the morowe: I am the Lord.
Muyidye pa tsiku lomwelo, wosasiyako ina mpaka mmawa. Ine ndine Yehova.
31 Therefore shall ye keepe my commandements and do them: for I am the Lord.
“Choncho sungani malamulo anga ndi kuwatsatira. Ine ndine Yehova.
32 Neither shall ye pollute mine holy Name, but I will be halowed among the children of Israel. I the Lord sanctifie you,
Musanyoze dzina langa loyera. Koma lilemekezedwe pakati pa Aisraeli. Ine ndine Yehova amene ndimakuyeretsani
33 Which haue brought you out of the land of Egypt, to be your God: I am the Lord.
ndipo ndine amene ndinakutulutsani mu Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Ine ndine Yehova.”

< Leviticus 22 >