< Leviticus 21 >
1 And the Lord said vnto Moses, Speake vnto the Priestes the sonnes of Aaron, and say vnto them, Let none be defiled by the dead among his people,
Yehova anawuza Mose kuti, “Yankhula ndi ansembe, ana a Aaroni, ndipo uwawuze kuti, ‘Wansembe asadzidetse pokhudza munthu wakufa pakati pa abale ake.
2 But by his kinseman that is neere vnto him: to wit, by his mother, or by his father, or by his sonne, or by his daughter, or by his brother,
Koma akhoza kukhudza thupi lakufa la amayi ake, abambo ake, mwana wake wamwamuna, mwana wake wamkazi, mchimwene wake,
3 Or by his sister a maid, that is neere vnto him, which hath not had a husband: for her he may lament.
kapena mlongo wake wosakwatiwa amene amadalira iye chifukwa sanakwatiwe. Iye akhoza kudzidetsa pokhudza thupi lakufa la mchemwali wake wosakwatiwa yekha.
4 He shall not lament for the Prince among his people, to pollute him selfe.
Koma wansembe asadzidetse chifukwa cha anthu amene ali nawo pa ubale obwera chifukwa cha ukwati.
5 They shall not make balde partes vpon their head, nor shaue off the locks of their beard, nor make any cuttings in their flesh.
“‘Ansembe asamete tsitsi kumutu kwawo kapena mʼmphepete mwa ndevu zawo, kapenanso kudzichekacheka pa thupi lawo.
6 They shalbe holy vnto their God, and not pollute the name of their God: for the sacrifices of the Lord made by fire, and the bread of their God they doe offer: therefore they shalbe holie.
Ayenera kukhala oyera pamaso pa Mulungu wawo ndipo asachititse manyazi dzina la Mulungu wawo. Popeza amapereka nsembe zotentha pa moto kwa Yehova, chakudya cha Mulungu wawo, iwo azikhala woyera.
7 They shall not take to wife an whore, or one polluted, neither shall they marrie a woman diuorced from her husband: for such one is holy vnto his God.
“‘Asakwatire akazi amene adzidetsa ndi chiwerewere kapena akazi amene amuna awo awasudzula, chifukwa ansembe ndi oyera pamaso pa Mulungu wawo.
8 Thou shalt sanctifie him therefore, for he offereth the bread of thy God: he shall be holy vnto thee: for I the Lord, which sanctifie you, am holy.
Iwo akhale oyera chifukwa amapereka nsembe kwa Mulungu wanu. Muziwaona kuti ndi oyera, popeza Ine Yehova amene ndimawayeretsa ndine woyera, nawonso akhale oyera.
9 If a Priestes daughter fall to play the whore, she polluteth her father: therefore shall she be burnt with fire.
“‘Ngati mwana wamkazi wa wansembe adziyipitsa pochita zachiwerewere, ndiye kuti iye akuchititsa manyazi abambo ake; mwanayo atenthedwe pa moto.
10 Also ye hie Priest among his brethren, (vpon whose head the anointing oyle was powred, and hath consecrated his hand to put on the garments) shall not vncouer his head, nor rent his clothes,
“‘Munthu amene ali mkulu wa ansembe pakati pa abale ake, amene anamudzoza pomutsanulira mafuta pamutu pake, ndiponso amene anapatulidwa pomuveka zovala zaunsembe, asalekerere tsitsi lake kapena kungʼamba zovala zake kusonyeza kuti ali pa chisoni.
11 Neither shall he goe to any dead bodie, nor make him selfe vncleane by his father or by his mother,
Asalowe mʼnyumba mmene muli munthu wakufa ngakhale womwalirayo ndi amayi ake kapena abambo ake.
12 Neither shall he goe out of the Sanctuarie, nor pollute the holy place of his God: for the crowne of the anoynting oyle of his God is vpon him: I am the Lord.
Asadzidetse potulukira kunja kwa malo opatulika popeza mafuta womupatula kukhala wansembe ali pamutu pake. Ine ndine Yehova.
13 Also he shall take a maide vnto his wife:
“‘Iye akwatire namwali wosadziwa mwamuna.
14 But a widowe, or a diuorced woman, or a polluted, or an harlot, these shall he not marrie, but shall take a maide of his owne people to wife:
Asakwatire mkazi wamasiye, mkazi wosudzulidwa, kapena mkazi wachiwerewere, koma akwatire namwali wosadziwa mwamuna pakati pa anthu a mtundu wake,
15 Neyther shall he defile his seede among his people: for I am the Lord which sanctifie him.
kuti mtundu wake usakhale wodetsedwa pakati pa abale popeza ndine Yehova, amene ndimamuyeretsa.’”
16 And the Lord spake vnto Moses, saying,
Yehova anawuza Mose kuti,
17 Speake vnto Aaron, and say, Whosoeuer of thy seede in their generations hath any blemishes, shall not prease to offer the bread of his God:
“Muwuze Aaroni kuti, ‘Munthu aliyense mwa zidzukulu zake ku mibado yawo yonse ikubwera akakhala ndi chilema asabwere kudzapereka nsembe kwa Mulungu wake.
18 For whosoeuer hath any blemish, shall not come neere: as a man blinde or lame, or that hath a flat nose, or that hath any misshapen member,
Munthu aliyense wachilema motere: munthu wakhungu kapena wolumala miyendo, munthu wolumala nkhope kapena waziwalo zambiri,
19 Or a man that hath a broken foote, or a broken hande,
munthu wa phazi lolumala kapena dzanja lolumala,
20 Or is crooke backt, or bleare eyed, or hath a blemish in his eye, or be skiruie, or skabbed, or haue his stones broken.
kapena munthu wokhota msana kapena wamfupi kwambiri, kapena wolumala maso, munthu wa nthenda yonyerenyetsa, kapena wamphere, kapenanso wophwanyika mavalo, sayenera kusendera pafupi.
21 None of the seede of Aaron the Priest that hath a blemish, shall come neere to offer the sacrifices of the Lord made by fire, hauing a blemish: he shall not prease to offer the bread of his God.
Mdzukulu aliyense wa Aaroni wansembe, amene ali ndi chilema asadzayandikire kukapereka nsembe zopsereza kwa Yehova. Popeza kuti ali ndi chilema, asayandikire kudzapereka nsembe ya chakudya kwa Mulungu wake.
22 The bread of his God, euen of the most holie, and of the holy shall he eate:
Koma iye angathe kudya chakudya chopatulika kwambiri chija, ngakhalenso chakudya chotsala pa nsembe zopatulika.
23 But he shall not goe in vnto the vaile, nor come neere the altar, because hee hath a blemish, least he pollute my Sanctuaries: for I am the Lord that sanctifie them.
Koma chifukwa cha kulumala kwake, sayenera kuyandikira katani kapena kufika pa guwa kuti angadetse malo anga wopatulika. Ine ndine Yehova, amene ndimawayeretsa.’”
24 Thus spake Moses vnto Aaron, and to his sonnes, and to all the children of Israel.
Choncho Mose anawuza Aaroni ndi ana ake pamodzi ndi Aisraeli onse zimenezi.