< Leviticus 11 >

1 After, the Lord spake vnto Moses and to Aaron, saying vnto them,
Yehova anayankhula ndi Mose ndi Aaroni kuti,
2 Speake vnto the children of Israel, and say, These are the beastes which yee shall eate, among all the beasts that are on the earth.
“Awuze Aisraeli kuti, ‘Nyama zomwe mukhoza kudya mwa nyama zonse za dziko lapansi ndi izi:
3 Whatsoeuer parteth the hoofe, and is clouen footed, and cheweth the cudde, among the beastes, that shall ye eate.
Nyama iliyonse imene ili ndi chipondero chogawikana pakati ndi yobzikula mukhoza kudya.
4 But of them that chewe the cud, or deuide the hoofe onely, of them yee shall not eate: as the camel, because he cheweth the cud, and deuideth not ye hoofe, he shall be vncleane vnto you.
“‘Koma pali nyama zina zimene zimabzikula kokha kapena ndi zogawikana zipondero zimene simukuyenera kudya. Nyama zimenezi ndi ngamira, ngakhale imabzikula ilibe zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
5 Likewise the conie, because he cheweth the cud and deuideth not the hoofe, he shall bee vncleane to you.
Ina ndi mbira, ngakhale imabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
6 Also the hare, because he cheweth the cud, and deuideth not the hoofe, he shalbe vncleane to you.
Inanso ndi kalulu, ngakhale amabzikula, zipondero zake nʼzosagawikana. Choncho ndi wodetsedwa, musadye.
7 And the swine, because he parteth ye hoofe and is clouen footed, but cheweth not the cud, he shalbe vncleane to you.
Nkhumba simabzikula ngakhale ili ndi zipondero zogawikana. Choncho ndi yodetsedwa, musadye.
8 Of their flesh shall yee not eate, and their carkeise shall yee not touch: for they shall bee vncleane to you.
Musamadye nyama yake kapena kukhudza imene yafa chifukwa ndi yodetsedwa.
9 These shall ye eate, of all that are in the waters: whatsoeuer hath finnes and skales in ye waters, in the seas, or in the riuers, them shall ye eate.
“‘Mwa zamoyo zonse zimene zimakhala mʼmadzi a mʼnyanja ndi a mʼmitsinje mukhoza kudya chilichonse chimene chili ndi minga ya pa msana ndi mamba.
10 But all that haue not finnes nor skales in the seas, or in the riuers, of all that moueth in the waters, and of al liuing things that are in the waters, they shalbe an abomination vnto you.
Koma zamoyo zonse za mʼnyanja kapena za mʼmitsinje zimene zilibe minga ya pa msana ndi mamba, kaya ndi tizirombo tonse ta mʼmadzi ndi zamoyo zonse zopezeka mʼmenemo ndi zodetsedwa kwa inu.
11 They, I say, shalbe an abomination to you: ye shall not eate of their flesh, but shall abhorre their carkeis.
Pakuti zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu, nyama yake musadye, ndipo zikafa zikhalebe zodetsedwa kwa inu.
12 Whatsoeuer hath not fins nor skales in the waters, that shalbe abomination vnto you.
Chamoyo chilichonse cha mʼmadzi chimene chilibe minga ya pa msana kapena mamba ndi chodetsedwa kwa inu.
13 These shall ye haue also in abomination among the foules, they shall not be eaten: for they are an abomination, the eagle, and the goshauke, and the osprey:
“‘Mbalame zimene simukuyenera kudya chifukwa ndi zodetsedwa ndi izi: mphungu, nkhwazi, mwimba,
14 Also the vultur, and the kite after his kinde,
nankapakapa, akamtema a mitundu yonse,
15 And all rauens after their kinde:
akhungubwi a mitundu yonse,
16 The ostrich also, and the night crowe, and the seameaw, and the hauke after his kinde:
kadzidzi wamphondo, kadzidzi wodzuma, chipudo ndi mtundu uliwonse wa akabawi
17 The litle owle also, and the connorant, and the great owle.
kadzidzi wamngʼono, chiswankhono ndi mantchichi,
18 Also the redshanke and the pelicane, and the swanne:
tsekwe, vuwo, dembo,
19 The storke also, the heron after his kinde, and the lapwing, and the backe:
indwa, zimeza za mitundu yonse, nsadzu ndi mleme.
20 Also euery foule that creepeth and goeth vpon all foure, such shalbe an abomination vnto you.
“‘Zowuluka zonse za miyendo inayi ndi zodetsedwa.
21 Yet these shall ye eate: of euery foule that creepeth, and goeth vpon all foure which haue their feete and legs all of one to leape withal vpon the earth,
Komabe mwa zowuluka zokhala ndi miyendo inayi zimene mukhoza kudya ndi zokhazo zimene zili ndi miyendo yolumphira.
22 Of them ye shall eate these, the grashopper after his kinde, and the solean after his kinde, the hargol after his kinde, and the hagab after his kind.
Pa zimenezo mungathe kudya izi: dzombe la mitundu yonse, atsokonombwe a mitundu yonse, nkhululu za mitundu yonse, ndi ziwala za mitundu yonse.
23 But al other foules that creepe and haue foure feete, they shalbe abomination vnto you.
Koma za mapiko zina zonse zokhala ndi miyendo inayi muzitenge kukhala zodetsedwa kwa inu.
24 For by such ye shalbe polluted: whosoeuer toucheth their carkeis, shalbe vncleane vnto the euening.
“‘Zimenezi zidzakudetsani. Aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
25 Whosoeuer also beareth of their carkeis, shall wash his clothes, and be vncleane vntil euen.
Aliyense wonyamula chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
26 Euery beast that hath clawes deuided, and is not clouen footed, nor cheweth the cud, such shalbe vncleane vnto you: euery one that toucheth them, shalbe vncleane.
“‘Nyama iliyonse imene ili ndi ziboda zogawikana koma mapazi ake wosagawikana, kapena imene sibzikula muyiyese yodetsedwa kwa inu ndipo munthu aliyense akakhudza nyama yakufayo, adzakhala wodetsedwa.
27 And whatsoeuer goeth vpon his pawes among all maner beastes that goeth on all foure, such shalbe vncleane vnto you: who so doth touch their carkeis shalbe vncleane vntil the euen.
Mwa nyama zonse zoyenda ndi miyendo inayi, nyama zonse zokhala ndi zikhadabo kuphazi muzitenge kukhala zodetsedwa ndipo aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
28 And he that beareth their carkeis, shall wash his clothes, and be vncleane vntill the euen: for such shalbe vncleane vnto you.
Aliyense wonyamula nyamazi zitafa ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu.
29 Also these shalbe vncleane to you amog the things that creepe and moue vpon the earth, the weasell, and the mouse, and the frog, after his kinde:
“‘Mwa nyama zokwawa, zimene zili zodetsedwa kwa inu ndi izi: likongwe, mbewa, msambulu za mitundu yonse,
30 Also the rat, and the lizard, and the chameleon, and the stellio, and the molle.
gondwa, mngʼazi, buluzi, dududu ndi nanzikambe.
31 These shall be vncleane to you among all that creepe: whosoeuer doeth touch them when they be dead, shalbe vncleane vntil the euen.
Mwa nyama zonse zoyenda pansi, zimenezi ndi zodetsedwa kwa inu. Munthu aliyense wozikhudza zitafa adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
32 Also whatsoeuer any of the dead carkeises of them doth fall vpon, shalbe vncleane, whether it be vessel of wood, or rayment, or skinne, or sacke: whatsoeuer vessel it be that is occupied, it shalbe put in the water as vncleane vntil the euen, and so be purified.
Iliyonse mwa nyama zimenezi ikafa ndi kugwera pa chiwiya chilichonse, kaya chimagwira ntchito yotani, kaya ndi chopangidwa ndi mtengo, kaya ndi cha nsalu, kaya ndi cha chikopa kapena chiguduli chiwiyacho chidzakhala chodetsedwa. Muchiviyike mʼmadzi chiwiyacho komabe chidzakhala chodetsedwa mpaka madzulo, ndipo kenaka chidzakhala choyeretsedwa.
33 But euery earthen vessel, whereinto any of them falleth, whatsoeuer is within it shalbe vncleane, and ye shall breake it.
Tsono nyama ina iliyonse mwa zimenezi ikagwera mʼmbiya ya dothi, ndiye kuti chilichonse cha mʼmbiyamo chidzakhala chodetsedwa, ndipo muyenera kuswa mbiyayo.
34 Al meate also that shalbe eaten, if any such water come vpon it, shalbe vncleane: and all drinke that shalbe drunke in al such vessels shalbe vncleane.
Chakudya chilichonse chimene mungadye chikakhala kuti chathiridwa mʼmbiyamo, ndiye kuti chakudyacho chidzakhala chodetsedwa, ndipo madzi akumwa wochokera mʼmbiya zotere ndi wodetsedwa.
35 And euery thing that their carkeis fall vpon, shalbe vncleane: the fornais or the pot shalbe broken: for they are vncleane, and shalbe vncleane vnto you.
Chiwalo chilichonse cha nyama yakufa chikagwera pa chinthu chilichonse kaya pa uvuni, kapena pa mʼphika, ndiye kuti zinthuzo zidzakhala zodetsedwa, ndipo ziphwanyidwe popeza ndi zodetsedwa.
36 Yet the fountaines and welles where there is plentie of water shalbe cleane: but that which toucheth their carkeises shalbe vncleane.
Koma kasupe kapena chitsime chamadzi chidzakhala choyeretsedwa ngakhale kuti chilichonse chokhudza nyama yakufayo chidzakhala chodetsedwa. Zimenezi muzitenge kukhala zodetsedwa.
37 And if there fal of their dead carkeis vpon any seede, which vseth to be sowe, it shalbe cleane.
Chiwalo chilichonse cha nyama yakufayo chikagwera pa mbewu zimene akuti adzale, mbewu zimenezo zidzakhalabe zabwino.
38 But if any water be powred vpon ye seede, and there fal of their dead carkeis thereon, it shall be vncleane vnto you.
Koma mbewuzo zikakhala zonyowa ndi madzi, ndipo chiwalo chilichonse cha nyama zakufazo chikagwera pa mbewuzo, mbewuzo zikhale zodetsedwa kwa inu.
39 If also any beast, whereof ye may eate, die, he that toucheth the carkeis thereof shall be vncleane vntil the euen.
“‘Ngati nyama imene mumaloledwa kudya yafa yokha, ndiye kuti aliyense wokhudza nyama yakufayo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
40 And he that eateth of the carkeis of it, shall wash his clothes and be vncleane vntil the euen: he also that beareth the carkeis of it, shall wash his clothes, and be vncleane vntil the euen.
Aliyense amene adyako nyama yakufayo achape zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo. Aliyense amene wanyamula nyama yakufayo ayenera kuchapa zovala zake, ndipo adzakhala wodetsedwa mpaka madzulo.
41 Euery creeping thing therefore that creepeth vpon the earth shalbe an abomination, and not be eaten.
“‘Chinthu chilichonse chokwawa pansi ndi chonyansa, simuyenera kudya.
42 Whatsoeuer goeth vpon the breast, and whatsoeuer goeth vpon al foure, or that hath many feete among all creeping thinges that creepe vpon the earth, ye shall not eate of them, for they shalbe abomination.
Musadye chilichonse chokwawa pansi, choyenda chamimba kapena choyenda ndi miyendo inayi kapenanso yambiri popeza ndi chodetsedwa.
43 Ye shall not pollute your selues with any thing that creepeth, neither make your selues vncleane with them, neither defile your selues thereby: ye shall not, I say, be defiled by them,
Musadzisandutse nokha odetsedwa ndi chokwawa chilichonse. Musadziyipitse nazo, kuti mukhale odetsedwa.
44 For I am the Lord your God: be sanctified therefore, and be holy, for I am holy, and defile not your selues with any creeping thing, that creepeth vpon the earth.
Ine ndine Yehova Mulungu wanu, choncho dziyeretseni kuti mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera. Musadzisandutse odetsedwa ndi chokwawa chilichonse.
45 For I am the Lord that brought you out of the lande of Egypt, to be your God, and that you should be holy, for I am holy.
Ine ndine Yehova amene ndinakutulutsani ku Igupto kuti ndikhale Mulungu wanu. Tsono mukhale woyera, chifukwa Ine ndine woyera.
46 This is the law of beasts, and of foules, and of euery liuing thing that moueth in the waters, and of euery thing that creepeth vpon the earth:
“‘Amenewa ndi malamulo onena za nyama, mbalame, chamoyo chilichonse choyenda mʼmadzi ndiponso chamoyo chilichonse chokwawa.
47 That there may be a difference betweene the vncleane and cleane, and betweene the beast that may be eaten, and the beast that ought not to be eaten.
Muzisiyanitsa pakati pa chodetsedwa ndi choyeretsedwa, komanso pakati pa zomwe mutha kudya ndi zomwe simuyenera kudya.’”

< Leviticus 11 >