< Judges 8 >

1 Then the men of Ephraim sayde vnto him, Why hast thou serued vs thus that thou calledst vs not, when thou wentest to fight with the Midianites? and they chode with him sharply.
Aefereimu anafunsa Gideoni kuti, “Nʼchifukwa chiyani watichita zimenezi? Bwanji sunatiyitane pamene umakamenyana ndi Amidiyani?” Iwo anamudzudzula kwambiri.
2 To whom he said, What haue I now done in comparison of you? is not the gleaning of grapes of Ephraim better, then the vintage of Abiezer?
Koma iye anawayankha kuti, “Nʼchiyani ndachita kuyerekeza ndi zimene mwachita inu? Kodi zimene mwachita inu Aefereimu si zazikulu kuposa zimene fuko langa la Abiezeri lachita?
3 God hath deliuered into your handes the princes of Midian, Oreb and Zeeb: and what was I able to do in comparison of you? and when he had thus spoken, then their spirits abated toward him.
Mulungu wapereka mafumu a Midiyani, Orebu ndi Zeebu mʼmanja mwanu. Ndachita chiyani kuyerekeza ndi zimene mwachita inu?” Atanena izi, anthuwo mitima yawo inatsika.
4 And Gideon came to Iorden to passe ouer, hee, and the three hundreth men that were with him, weary, yet pursuing them.
Gideoni anafika ndi kuwoloka mtsinje wa Yorodani pamodzi ndi anthu 300 amene anali naye. Ngakhale kuti anali otopa anapirikitsabe adani awo.
5 And he said vnto the men of Succoth, Giue, I pray you, morsels of bread vnto the people that follow me (for they be wearie) that I may follow after Zebah, and Zalmunna Kings of Midian.
Atafika ku Sukoti anapempha anthu a kumeneko kuti, “Chonde apatseniko buledi ankhondo angawa pakuti atopa. Koma ine ndikupirikitsa Zeba ndi Zalimuna, mafumu a Midiyani.”
6 And the princes of Succoth sayde, Are the handes of Zebah and Zalmunna nowe in thine hads, that we should giue bread vnto thine army?
Koma atsogoleri a Sukoti anayankha kuti, “Kodi Zeba ndi Zalimuna mwawagonjetsa kale kuti tipatse buledi ankhondo akowa?”
7 Gideon then sayde, Therefore when the Lord hath deliuered Zebah and Zalmunna into mine hand, I will teare your flesh with thornes of the wildernes and with breers.
Gideoni anayankha kuti, “Mwatero! Yehova akapereka Zeba ndi Zalimuna mʼdzanja langa, ndidzakukwapulani ndi matsatsa a minga ya mʼchipululu.”
8 And he went vp thence to Penuel, and spake vnto them likewise, and the men of Penuel answered him, as the men of Succoth answered.
Atachoka pamenepo anapita ku Penueli ndipo anapemphanso buledi kwa anthu a kumeneko, koma iwo anamuyankha monga anayankhira anthu a ku Sukoti aja.
9 And he sayd also vnto the men of Penuel, When I come againe in peace, I will breake downe this towre.
Gideoni anawawuzanso kuti, “Ndikamadzabwerera nditawagonjetsa, ndidzagwetsa nsanja iyi.”
10 Now Zebah and Zalmunna were in Karkor, and their hostes with them, about fifteene thousande, all that were left of all the hostes of them of the East: for there was slaine an hundreth and twentie thousand men, that drew swordes.
Nthawi iyi nʼkuti Zeba ndi Zalimuna ali ku Karikori ndi ankhondo pafupifupi 15,000. Amenewa ndiwo anatsalako mwa ankhondo a anthu akummawa; pakuti anafa ankhondo 120,000.
11 And Gideon went through them that dwelt in Tabernacles on the East side of Nobah and Iogbehah, and smote the hoste: for the hoste was carelesse.
Gideoni anadzera njira ya anthu a matenti kummawa kwa Noba ndi Yogibeha ndipo anawathira nkhondo popeza ankhondo awo anali osakonzekera.
12 And when Zebah and Zalmunna fled, hee followed after them, and tooke the two kings of Midian, Zebah and Zalmunna, and discomfited all the hoste.
Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri a Amidiyani anathawa koma Gideoni anawathamangitsa mpaka kuwagwira. Koma ankhondo awo onse anathawa ndi mantha.
13 So Gideon the sonne of Ioash returned from battel, the sunne being yet hie,
Ndipo Gideoni mwana wa Yowasi, pobwera kuchokera ku nkhondo anadzera njira ya ku chikweza cha Heresi.
14 And tooke a seruant of the me of Succoth, and inquired of him: and he wrote to him the princes of Succoth and the Elders thereof, euen seuentie and seuen men.
Kumeneko iye anagwira mnyamata wa ku Sukoti ndipo atamufunsa, mnyamatayo anamulembera mayina a akuluakulu ndi atsogoleri 77 a ku Sukoti.
15 And he came vnto the men of Succoth, and sayd, Behold Zebah and Zalmunna, by whome ye vpbrayded me, saying, Are the hands of Zebah and Zalmunna already in thine hands, that we should giue bread vnto thy weary men?
Kenaka Gideoni anabwera kwa anthu a ku Sukoti ndi kunena kuti, “Awa ndi Zeba ndi Zalimuna, mafumu awiri munkandinena nawo aja kuti, ‘Kodi Zeba ndi Zalimuna wawagonjetsa kale mmene ukuti tiwapatse buledi anthu ako otopawa?’”
16 Then he tooke the Elders of the citie, and thornes of the wildernes and breers, and did teare the men of Succoth with them.
Tsono Gideoni anatenga akuluakulu a mu mzindawo ndipo anagwira matsatsa a minga za mʼchipululu ndi kuwakwapula nawo.
17 Also he brake downe the towre of Penuel, and slew the men of the citie.
Anagwetsa nsanja ya ku Penueli ndi kupha amuna onse a mu mzindawo.
18 Then saide he vnto Zebah and Zalmunna, What maner of men were they, whom ye slew at Tabor? and they answered, As thou art, so were they: euery one was like the children of a King.
Kenaka anafunsa Zeba ndi Zalimuna kuti, “Kodi anthu a ku Tabori amene munawapha aja anali a maonekedwe otani?” Iwo anayankha kuti, “Anali anthu a maonekedwe ngati inu. Aliyense ankaoneka ngati mwana wa mfumu?” Iwo anayankha kuti, “Anthu ngati inu, aliyense wooneka ngati mwana wa mfumu.”
19 And he said, They were my brethren, euen my mothers children: as the Lord liueth, if ye had saued their liues, I would not slay you.
Ndipo Gideoni anayankha kuti, “Ndikulumbira pa Mulungu, mukanapanda kuwapha nanenso sindikanakuphani. Ndi abale anga amenewo, ana a amayi anga enieni.”
20 Then he sayde vnto Iether his first borne sonne, Vp, and slay them: but the boy drew not his sword: for he feared, because he was yet yong.
Tsono anawuza Yetero, mwana wake wachisamba kuti, “Tiye, ipha anthu amenewa!” Koma chifukwa Yeteri anali wamngʼono sanasolole lupanga lake, popeza anachita mantha.
21 Then Zebah and Zalmunna sayd, Rise thou, and fall vpon vs: for as the man is, so is his strength. And Gideon arose and slew Zebah and Zalmunna, and tooke away the ornamentes, that were on their camels neckes.
Tsono Zeba ndi Zalimuna anawuza Gideoni kuti, “Bwera utiphe ndiwe chifukwa uli ndi mphamvu za munthu wamkulu.” Choncho Gideoni anapita nawapha natenganso zokongoletsera zimene zinali pa makosi a ngamira zawo.
22 Then the men of Israel sayd vnto Gideon, Reigne thou ouer vs, both thou, and thy sonne, and thy sonnes sonne: for thou hast deliuered vs out of the hand of Midian.
Aisraeli anati kwa Gideoni, “Inu muzitilamulira, mwana wanu ndi zidzukulu zanu, chifukwa mwatipulumutsa mʼmanja mwa Amidiyani.”
23 And Gideon sayde vnto them, I will not reigne ouer you, neither shall my childe reigne ouer you, but the Lord shall reigne ouer you.
Koma Gideoni anawawuza kuti, “Sindidzakulamulirani, mwana wanganso sadzakulamulirani. Koma Yehova ndiye adzakulamulirani.”
24 Againe Gideon sayd vnto them, I would desire a request of you, that you would giue mee euery man the earings of his pray (for they had golden earings because they were Ismaelites)
Gideoni anatinso, “Ine ndikupemphani chinthu chimodzi. Aliyense wa inu andipatse ndolo zomwe anafunkha ku nkhondo.” (Adani aja anali ndi ndolo zagolide popeza anali Aismaeli).
25 And they answered, Wee will giue them. And they spred a garment, and did cast therein euery man the earings of his pray.
Iwo anayankha kuti, “Ife tikupatsani ndithu ndolozi.” Choncho anayala chinsalu, ndipo aliyense anaponyapo ndolo zimene anafunkha.
26 And the weight of the golden earings that he required, was a thousande and seuen hundreth shekels of golde, beside collers and iewels, and purple rayment that was on the kings of Midian, and beside the cheynes that were about their camels neckes.
Tsono kulemera kwa ndolo zagolide zimene anapereka kunali makilogalamu makumi awiri, osawerengera kulemera kwa mphande, mkanda wamʼkhosi, zovala zapepo za mafumu a Midiyani ndiponso malamba azitsulo za mʼmakosi a ngamira zawo.
27 And Gideon made an Ephod thereof, and put it in Ophrah his citie: and all Israel went a whoring there after it, which was the destruction of Gideon and his house.
Gideoni anagwiritsa ntchito golide uja kupanga efodi, ndipo anakamuyika ku mzinda wake ku Ofura. Tsono Aisraeli onse anasiya kupembedza Yehova nayamba kupembedza efodiyo kumeneko. Ichi chinasanduka msampha kwa Gideoni ndi banja lake lonse.
28 Thus was Midian brought lowe before the children of Israel, so that they lift vp their heads no more: and the countrey was in quietnes fourtie yeeres in the dayes of Gideon.
Choncho Amidiyani anagonjetsedwa ndi Aisraeli ndipo sanayeserenso kuwawukira. Ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 40 pamene Gideoni anali ndi moyo.
29 Then Ierubbaal the sonne of Ioash went, and dwelt in his owne house.
Yeru-Baala mwana wa Yowasi anapita kukakhala kwawo.
30 And Gideon had seuentie sonnes begotten of his body: for he had many wiues.
Ana a Gideoni anali 70 popeza anali ndi akazi ambiri.
31 And his concubine that was in Shechem, bare him a sonne also, whose name he called Abimelech.
Mdzakazi wake amene anali ku Sekemu, anabereka naye mwana wamwamuna, amene anamutcha Abimeleki.
32 So Gideon the sonne of Ioash dyed in a good age, and was buried in the sepulchre of Ioash his father in Ophrah, of the father of ye Ezrites.
Gideoni mwana wa Yowasi anamwalira atakalamba ndipo anayikidwa mʼmanda a abambo ake, Yowasi ku Ofura mzinda wa Mwabiezeri.
33 But when Gideon was dead, the children of Israel turned away and went a whoring after Baalim, and made Baal-berith their God.
Atangomwalira Gideoni, Aisraeli anayambanso kupembedza Abaala. Iwo anasandutsa Baala-Beriti kukhala mulungu wawo.
34 And the children of Israel remembred not the Lord their God, which had deliuered the out of the hands of all their enemies on euery side.
Aisraeli sanakumbukirenso Yehova Mulungu wawo amene anawapulumutsa mʼmanja mwa adani awo mbali zonse.
35 Neither shewed they mercy on the house of Ierubbaal, or Gideon, according to al the goodnesse which he had shewed vnto Israel.
Ndiponso sanachite zinthu zokomera banja la Yeru-Baala (ndiye kuti Gideoni) chifukwa cha zabwino zonse zimene iye anawachitira.

< Judges 8 >