< Judges 3 >

1 These nowe are the nations which the Lord left, that he might proue Israel by them (euen as many of Israel as had not knowen all the warres of Canaan,
Iyi ndi mitundu ya anthu yomwe Yehova anayisiya kuti ayese nayo Aisraeli amene sanadziwe kumenya nkhondo mu Kanaani
2 Only to make the generations of the children of Israel to know, and to teach them warre, which doutles their predecessors knew not)
(Yehova anachita izi kuti Aisraeli onse aphunzire kumenya nkhondo; makamaka amene nʼkale lonse sanadziwe kumenya nkhondo.
3 Fiue princes of the Philistims, and all the Canaanites, and the Sidonians, and the Hiuites that dwelt in mount Lebanon, from mount Baal-hermon vntill one come to Hamath.
Mitundu ya anthuyo ndi: Mafumu asanu a Afilisti, Akanaani onse, Asidoni, ndi Ahivi amene ankakhala ku mapiri a Lebanoni kuyambira ku phiri la Baala-Herimoni mpaka ku Lebo Hamati.
4 And these remayned to proue Israel by them, to wit, whether they would obey the commandements of the Lord, which he commanded their fathers by the hand of Moses.
Iwowa Yehova anawasiya kuti aziyesa nawo Aisraeli kuti aone ngati angamvere malamulo a Yehova, amene anapatsa makolo awo kudzera mwa Mose.
5 And the children of Israel dwelt among the Canaanites, the Hittites, and the Amorites, and the Perizzites, and the Hiuites, and the Iebusites,
Choncho Aisraeli anakhala pakati pa Akanaani, Ahiti, Aamori, Aperezi, Ahivi ndi Ayebusi.
6 And they tooke their daughters to bee their wiues, and gaue their daughters to their sonnes, and serued their gods.
Tsono Aisraeli aja amalola ana awo aamuna ndi aakazi kuti azikwatira ndi kukwatiwa ndi anthu amitundu ina. Kenaka anayamba kupembedza milungu yawo.
7 So the children of Israel did wickedly in the sight of the Lord, and forgate the Lord their God, and serued Baalim, and Asheroth.
Aisraeli anachita zinthu zoyipira Yehova. Iwowa anayiwala Yehova Mulungu wawo ndi kumatumikira Abaala ndi Asera.
8 Therefore the wrath of the Lord was kindled against Israel, and he solde them into the hand of Chushan rishathaim King of Aram-naharaim, and the children of Israel serued Chushan rishathaim eyght yeeres.
Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeliwo ndipo anawagulitsa kwa Kusani-Risataimu mfumu ya ku Mesopotamiya. Choncho Aisraeli anakhala pansi pa ulamuliro wake zaka zisanu ndi zitatu.
9 And when the children of Israel cryed vnto the Lord, the Lord stirred vp a sauiour to ye children of Israel, and he saued them, euen Othniel the sonne of Kenaz, Calebs yonger brother.
Koma pamene Aisraeliwo analirira kwa Yehova, Iye anawawutsira mpulumutsi, Otanieli mwana wamwamuna wa Kenazi, mngʼono wake wa Kalebe. Iyeyu ndiye anawapulumutsa.
10 And the spirite of the Lord came vpon him, and he iudged Israel, and went out to warre: and the Lord deliuered Chushan rishathaim king of Aram into his hand, and his hand preuailed against Chushan rishathaim.
Mzimu wa Yehova unatsika pa iye, choncho anasanduka mtsogoleri wa Israeli. Iye anapita kukamenya nkhondo, ndipo Yehova anapereka Kusani-Risataimu mfumu ya Aaramu mʼmanja mwake. Choncho anayigonjetsa.
11 So the lande had rest fourtie yeeres, and Othniel the sonne of Kenaz dyed.
Ndipo mʼdzikomo munakhala mtendere zaka makumi anayi. Kenaka Otanieli mwana wa Kenazi anamwalira.
12 Then the children of Israel againe committed wickednesse in the sight of the Lord: and the Lord strengthened Eglon King of Moab against Israel, because they had committed wickednesse before the Lord.
Aisraeli anachitanso zinthu zoyipira Yehova. Tsono Yehova anapatsa mphamvu Egiloni, mfumu ya Mowabu kuti alimbane ndi Aisraeli aja popeza anachita zinthu zoyipira Yehova.
13 And he gathered vnto him the children of Ammon, and Amalek, and went and smote Israel, and they possessed the citie of palme trees.
Egiloniyo anamemeza Aamori ndi Aamaleki kupita kukamenyana ndi Israeli, ndipo analanda Yeriko, mzinda wa migwalangwa.
14 So the children of Israel serued Eglon king of Moab eighteene yeeres.
Aisraeli anatumikira ngati akapolo Egiloni mfumu ya Mowabu kwa zaka 18.
15 But when the children of Israel cried vnto the Lord, the Lord stirred them vp a sauiour, Ehud the sonne of Gera the sonne of Iemini, a man lame of his right hande: and the children of Israel sent a present by him vnto Eglon King of Moab.
Aisraeli analiranso kwa Yehova, ndipo Iye anawawutsira mpulumutsi, Ehudi. Iyeyu anali mwana wa Gera, munthu wamanzere, wa fuko la Benjamini. Aisraeli ankatumiza msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, kudzera kwa Ehudi.
16 And Ehud made him a dagger with two edges of a cubite length, and he did gird it vnder his rayment vpon his right thigh,
Ndipo Ehudi anapanga lupanga lakuthwa kuwiri lotalika masentimita makumi asanu, ndipo anamangirira lupangalo pa ntchafu yake ya kumanja mʼkati mwa zovala zake.
17 And he presented ye gift vnto Eglon King of Moab (and Eglon was a very fat man)
Iye anakapereka msonkho kwa Egiloni, mfumu ya Mowabu, amene anali munthu wonenepa kwambiri.
18 And when he had now presented the present, he sent away the people that bare ye present,
Ehudi atapereka msonkhowo, anawuza anthu amene ananyamula msonkhowo kuti azipita.
19 But he turned againe from the quarris, that were by Gilgal, and said, I haue a secret errand vnto thee, O King. Who said, Keepe silence: and all that stoode about him, went out from him.
Iye mwini anabwerera pamalo a miyala yozokotedwa ku Giligala ndipo anati, “Zikomo mfumu, ine ndili ndi mawu achinsinsi kuti ndikuwuzeni.” Mfumuyo inawuza onse amene amayitumikira kuti akhale chete, ndipo kenaka anawatulutsa.
20 Then Ehud came vnto him. (and he sate alone in a sommer parler, which he had) and Ehud said, I haue a message vnto thee from God. Then he arose out of his throne,
Kenaka Ehudi anayandikira pafupi ndi mfumuyo, ndipo iyo inakhala yokha mʼchipinda chapamwamba, mozizira bwino. Tsono Ehudi anati, “Ndili ndi mawu ochokera kwa Mulungu woti ndikuwuzeni.” Mfumuyo itadzuka pa mpando wake waufumu,
21 And Ehud put forth his left hand, and tooke the dagger from his right thigh, and thrust it into his bellie,
Ehudi ndi dzanja lake lamanzere, anasolola lupanga pa ntchafu yake ya kumanja ndi kubaya nalo mfumuyo pa mimba.
22 So that the hafte went in after the blade, and the fatte closed about the blade, so that he could not drawe the dagger out of his bellie, but the dirt came out.
Lupanga linalowa mʼmimba pamodzi ndi chogwirira chake. Mafuta anaphimba lupangalo popeza silinatulutsidwe mʼmimbamo. Ndiponso matumbo anatuluka.
23 Then Ehud gate him out into the porch, and shut the doores of the parler vpon him, and locked them.
Kenaka Ehudi anatuluka panja pa khonde, atatseka ndi kukhoma zitseko za chipinda chapamwambacho.
24 And when he was gone out, his seruantes came: who seeing that the doores of the parler were locked, they sayd, Surely he doeth his easement in his sommer chamber.
Ehudi atachoka, atumiki a mfumu aja anabwera, ndipo ataona kuti zitseko za chipinda chapamwamba zinali zokhoma anaganiza kuti mwina mfumu ikudzithandiza mʼkatimo.
25 And they taryed till they were ashamed: and seeing he opened not the doores of the parler, they tooke the key, and opened them, and behold, their lord was fallen dead on the earth.
Iwo anadikira nthawi yayitali koma popanda chochitika. Koma ataona kuti mfumuyo sikutsekulabe zitseko za chipindacho, iwo anatenga makiyi ndi kutsekula zitsekozo, ndipo anangoona mbuye wawo atagwera pansi, ali wakufa.
26 So Ehud escaped (while they taried) and was passed the quarris, and escaped vnto Seirah.
Ehudi anathawa pamene iwo ankadikira. Iye anadzera ku malo a miyala yozokotedwa kuja ndi kuthawa kupita ku Seiri.
27 And when he came home, he blew a trumpet in mount Ephraim, and the children of Israel went downe with him from the mountaine, and he went before them.
Atafika kumeneko, anayimba lipenga ku dziko la ku mapiri la Efereimu. Iye akutsogolera, Aisraeli onse anatsika naye pamodzi kuchoka ku mapiriko.
28 Then said he vnto them, Follow me: for the Lord hath deliuered your enemies, euen Moab into your hand. So they went downe after him, and tooke the passages of Iorden towarde Moab, and suffred not a man to passe ouer.
Iye anawawuza kuti, “Nditsatireni, chifukwa Yehova wapereka Amowabu, adani anu mʼmanja mwanu.” Choncho anthuwo anamutsatira, nalanda madooko a Yorodani opita ku Mowabu. Iwo sanalole kuti wina aliyense awoloke.
29 And they slewe of the Moabites the same time about ten thousand men, all fed men, and all were warriours, and there escaped not a man.
Nthawi imeneyo anapha Amowabu pafupifupi 10,000. Ophedwawo anali anthu amphamvu komanso odziwa kumenya nkhondo, ndipo panalibe ndi mmodzi yemwe anathawa.
30 So Moab was subdued that daye, vnder the hand of Israel: and the land had rest fourescore yeeres.
Tsiku limenelo Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Israeli, ndipo dzikolo linakhala pa mtendere kwa zaka 80.
31 And after him was Shamgar the sonne of Anath, which slewe of the Philistims sixe hundreth men with an oxe goade, and he also deliuered Israel.
Ehudi atamwalira, panabwera Samugara mwana wa Anati. Iye anapha Afilisti 600 ndi ndodo yomenyera ngʼombe. Nayenso anapulumutsa Israeli.

< Judges 3 >