< Judges 2 >

1 And an Angel of the Lord came vp from Gilgal to Bochim, and sayd, I made you to go vp out of Egypt, and haue brought you vnto the land which I had sworne vnto your fathers, and sayd, I wil neuer breake my couenant with you.
Mngelo wa Yehova anapita ku Bokimu kuchokera ku Giligala ndipo anati kwa Aisraeli, “Ndinakutulutsani mʼdziko la Igupto ndikukulowetsani mʼdziko limene ndinalumbira kwa makolo anu. Ndinati ‘Sindidzaswa pangano langa ndi inu,
2 Ye also shall make no couenant with the inhabitants of this land, but shall breake downe their altars: but ye haue not obeyed my voyce. Why haue ye done this?
ndipo inu musadzachite pangano ndi anthu a dziko lino, koma mudzaphwanye maguwa awo ansembe.’ Koma inu simunamvere lamulo langa. Chifukwa chiyani mwachita zimenezi?
3 Wherefore, I sayd also, I wil not cast them out before you, but they shalbe as thornes vnto your sides, and their gods shalbe your destruction.
Ndikukuwuzani tsopano kuti sindithamangitsa nzikazo pamene inu mukufika. Ndidzawasandutsa kukhala adani anu ndipo milungu yawo idzakhala ngati msampha kwa inu.”
4 And when the Angel of the Lord spake these wordes vnto all the children of Israel, the people lift vp their voyce, and wept.
Mngelo wa Mulungu atayankhula izi kwa Aisraeli, onse analira mokweza,
5 Therefore they called the name of that place, Bochim, and offered sacrifices there vnto the Lord.
ndipo anatcha malowo kuti Bokimu (kutanthauza kuti Olira). Pamenepo anapereka nsembe kwa Yehova.
6 Now when Ioshua had sent the people away, the children of Israel went euery man into his inheritance, to possesse the land.
Yoswa atawuza Aisraeli kuti achoke, iwo anapita kukatenga dzikolo, aliyense dera lake.
7 And the people had serued the Lord al the dayes of Ioshua, and all the dayes of the Elders that outliued Ioshua, which had seene all the great works of the Lord that he did for Israel.
Anthuwo anatumikira Yehova masiku onse a moyo wa Yoswa. Atamwalira Yoswa, Aisraeli anatumikirabe Yehova nthawi yonse ya moyo wa akuluakulu amene anaona zazikulu zimene Yehova anawachitira.
8 But Ioshua the sonne of Nun the seruant of the Lord dyed, when he was an hundreth and ten yeeres olde:
Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110.
9 And they buryed him in the coastes of his inheritance, in Timnath-heres in mount Ephraim, on the Northside of mount Gaash.
Ndipo anamuyika mʼmanda a mʼdziko lake, ku Timnati-Heresi mʼdziko la mapiri la Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
10 And so all that generation was gathered vnto their fathers, and another generation arose after them, which neither knewe the Lord, nor yet the works, which he had done for Israel.
Mʼbado onse utapita kukakhala ndi anthu a mtundu awo, kenaka panauka mʼbado wina umene sunadziwe Yehova ngakhale ntchito zazikulu zimene Yehova anachitira Aisraeli.
11 Then the children of Israel did wickedly in the sight of the Lord, and serued Baalim,
Choncho Aisraeli anayamba kuchita zinthu zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anatumikira Abaala.
12 And forsooke ye Lord God of their fathers, which brought them out of the lande of Egypt, and followed other gods, euen the gods of the people that were round about them, and bowed vnto them, and prouoked the Lord to anger.
Iwo anasiya Yehova Mulungu wa makolo awo, amene anawatulutsa ku Igupto. Ndipo anatsatira ndi kupembedza milungu yosiyanasiyana ya anthu amene anawazungulira. Motero Aisraeli anakwiyitsa Yehova.
13 So they forsooke the Lord, and serued Baal, and Ashtaroth.
Iwo anasiya Yehova ndi kumatumikira Baala ndi Asiteroti.
14 And the wrath of the Lord was hote against Israel, and he deliuered them into the hands of spoylers, that spoyled them, and he sold them into the handes of their enemies rounde about them, so that they could no longer stande before their enemies.
Yehova anapsera mtima Aisraeli ndipo anawapereka mʼmanja mwa anthu ofunkha amene ankasakaza zinthu zawo. Ndipo analola kuti adani awo owazungulira amene sanathenso kulimbana nawo, awagonjetse.
15 Whithersoeuer they went out, the hand of the Lord was sore against them, as ye Lord had sayd, and as the Lord had sworne vnto them: so he punished them sore.
Nthawi zonse Aisraeli ankati akapita ku nkhondo, Yehova amalimbana nawo kuti agonjetsedwe, monga ananenera molumbira kuti zidzaterodi. Choncho iwo anali pa mavuto aakulu.
16 Notwithstanding, the Lord raysed vp Iudges, which deliuered them out of the hands of their oppressours.
Choncho Yehova anawawutsira atsogoleri amene ankawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amene ankasakaza zinthu zawo.
17 But yet they would not obey their Iudges: for they went a whoring after other gods, and worshipped them, and turned quickly out of the way, wherein their fathers walked, obeying the commandements of the Lord: they did not so.
Komabe iwo sanawamvere atsogoleri awowo popeza ankapembedza milungu ina ndi kumayigwadira. Iwo anapatuka msangamsanga mu njira imene ankayendamo makolo awo. Iwo aja ankamvera malamulo a Yehova, koma mʼbado uwu ayi.
18 And when the Lord had raysed them vp Iudges, the Lord was with the Iudge, and deliuered them out of the hande of their enemies all the dayes of the Iudge (for the Lord had compassion on their gronings, because of them that oppressed them and tormented them)
Nthawi zonse Yehova akawautsira mtsogoleri, Iye amakhala naye, ndipo mtsogoleriyo ankawapulumutsa Aisraeliwo mʼmanja mwa adani awo mʼnthawi imene anali moyo. Yehova ankawamvera chisoni Aisraeli pamene ankabuwula chifukwa cha anthu owazunza ndi kuwasautsa.
19 Yet when the Iudge was dead, they returned, and did worse then their fathers, in following other gods to serue them and worshippe them: they ceased not from their owne inuentions, nor from their rebellious way.
Koma nthawi zonse mtsogoleri akamwalira, Aisraeli ankabwerera mʼmbuyo. Iwo amadzisandutsa oyipa kupambana makolo awo popeza ankatsata milungu ina, kuyitumikira ndi kumayigwadira. Anakana kusiya makhalidwe awo oyipa ndi njira zawo zamakani.
20 Wherfore the wrath of the Lord was kindled against Israel, and he sayd, Because this people hath transgressed my couenant, which I commaded their fathers, and hath not obeyed my voyce,
Choncho Yehova anawapsera mtima Aisraeli ndipo anati, “Chifukwa mtundu uwu waswa pangano limene ndinakhazikitsa ndi makolo awo ndipo sanandimvere,
21 Therefore will I no more cast out before them any of the nations, which Ioshua left when he dyed,
Inenso sindidzapirikitsanso mtundu uli wonse wa anthu amene Yoswa anawasiya pomwalira.
22 That through them I may proue Israel, whether they wil keepe the way of the Lord, to walke therein, as their fathers kept it, or not.
Ndidzatero kuti ndiwayese Aisraeli ndi kuona ngati adzasamala kuyenda mʼnjira ya Ine Yehova monga momwe ankachitira makolo awo.”
23 So the Lord left those nations, and droue them not out immediatly, neither deliuered them into the hand of Ioshua.
Choncho Yehova anayileka mitundu imeneyi ndipo sanayithamangitse kapena kuyipereka mʼmanja mwa Yoswa.

< Judges 2 >