< Judges 15 >

1 But within a while after, in the time of wheate haruest, Samson visited his wife with a kid, saying, I wil go in to my wife into the chamber: but her father would not suffer him to goe in.
Patapita nthawi, mu nyengo yodula tirigu, Samsoni anatenga kamwana kambuzi ndipo anapita kukacheza kwa mkazi wake. Iye anati, “Ndikufuna kukalowa ku chipinda cha mkazi wanga.” Koma abambo a mkaziyo anamuletsa kutero.
2 And her father sayde, I thought that thou hadst hated her: therefore gaue I her to thy companion. Is not her yonger sister fayrer then shee? take her, I pray thee, in stead of the other.
Abambo a mkaziyo anati, “Ine ndimaganiza kuti umamuda kwambiri nʼchifukwa chake ndinamupereka kwa mnzako. Kodi mngʼono wake uja sindiye wokongola kupambana iye? Ingotengani ameneyo mʼmalo mwake.”
3 Then Samson saide vnto them, Nowe am I more blamelesse then the Philistims: therefore will I doe them displeasure.
Samsoni anawawuza kuti, “Pano sindikhala wochimwa ndikawachita choyipa chachikulu Afilistiwa.”
4 And Samson went out, and tooke three hundreth foxes, and tooke firebrands, and turned them taile to taile, and put a firebrand in ye middes betweene two tailes.
Choncho Samsoni anapita nakagwira nkhandwe 300 nazimangirira michira ziwiriziwiri ndipo pa fundo iliyonse ya michirayo anamangirira nsakali.
5 And when he had set the brandes on fire, he sent them out into the standing corne of the Philistims, and burnt vp both the rickes and the standing corne with the vineyardes and oliues.
Anayatsa nsakalizo kenaka ndi kuzitayira nkhandwe zija mʼminda ya tirigu ya Afilisti, ndipo zinatentha milu ya tirigu, ndi wosadula yemwe pamodzi ndi mitengo ya mpesa ndi ya olivi.
6 Then the Philistims sayde, Who hath done this? And they answered, Samson the sonne in law of the Timnite, because hee had taken his wife, and giuen her to his companion. Then the Philistims came vp and burnt her and her father with fire.
Tsono Afilisti anayamba kufunsana kuti, “Ndani wachita izi?” Ena anati, “Ndi Samsoni mkamwini wa munthu wa ku Timna uja chifukwa Mtimunayo anatenga mkazi wake ndi kumupereka kwa mnzake.” Choncho Afilisti anapita kukatentha mtsikanayo pamodzi ndi abambo ake.
7 And Samson saide vnto them, Though yee haue done this, yet wil I be auenged of you, and then I wil cease.
Samsoni anawawuza kuti, “Ngati mumachita zangati zimenezi, ndiye ine sindileka mpaka nditakulipsirani.”
8 So hee smote them hippe and thigh with a mightie plague: then hee went and dwelt in the top of the rocke Etam.
Choncho Samsoni anamenyana nawo koopsa ndipo anapha ambiri a iwo. Kenaka anakalowa mʼphanga la Etamu, nakhala momwemo.
9 Then the Philistims came vp, and pitched in Iudah, and were spred abroad in Lehi.
Pambuyo pake Afilisti anakamanga misasa ya nkhondo mʼdziko la Yuda, ndi kuthira nkhondo mʼdera la Lehi.
10 And the men of Iudah sayde, Why are yee come vp vnto vs? And they answered, To binde Samson are we come vp, and to do to him as hee hath done to vs.
Anthu a fuko la Yuda anafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani mwabwera kudzamenyana nafe?” Iwo anayankha kuti, “Tabwera kudzamanga Samsoni ndi kuti timuchite zofanana ndi zimene anatichita.”
11 Then three thousande men of Iudah went to the top of the rocke Etam, and sayde to Samson, Knowest thou not that the Philistims are rulers ouer vs? Wherefore then hast thou done thus vnto vs? And he answered them, As they did vnto me, so haue I done vnto them.
Ndipo anthu 3,000 a ku Yuda anapita ku phanga la Etamu, ndi kukamufunsa Samsoni kuti, “Kodi iwe sudziwa kuti ife amatilamulira ndi Afilisti? Tsono ndi chiyani chimene watichitachi?” Iye anayankha kuti, “Ine ndinachita zomwe iwo anandichita.”
12 Againe they sayd vnto him, Wee are come to binde thee, and to deliuer thee into the hande of the Philistims. And Samson sayde vnto them, Sweare vnto me, that yee will not fall vpon me your selues.
Iwo anati kwa iye, “Ife tabwera kuti tikumange ndi kukupereka kwa Afilisti.” Ndipo Samsoni anati, “Lonjezani mwa lumbiro kuti simundipha ndinu.”
13 And they answered him, saying, No, but we will bynde thee and deliuer thee vnto their hande, but we will not kill thee. And they bound him with two newe cordes, and brought him from the rocke.
Iwo anamuyankha kuti, “Ayi, ife sitikupha. Koma tingokumanga ndi kukupereka mʼmanja mwa Afilisti.” Choncho anamumanga ndi zingwe ziwiri zatsopano namutulutsa mʼphanga muja.
14 When hee came to Lehi, the Philistims shouted against him, and the Spirite of the Lord came vpon him, and the cordes that were vpon his armes, became as flaxe that was burnt with fire: for the bandes loosed from his handes.
Samsoni anafika ku Lehi, ndipo Afilisti anamuchingamira akufuwula. Nthawi yomweyo Mzimu wa Yehova unatsika pa iye mwamphamvu ndipo zingwe zimene anamumanga nazo zinasanduka ngati thonje lopsa mʼmoto, zinachita ngati zasungunuka nʼkuchoka mʼmanja mwake.
15 And he found a new iawebone of an asse, and put forth his hand, and caught it, and slewe a thousand men therewith.
Anapeza chibwano cha bulu amene anali atangofa kumene. Anachitola ndi kuphera nacho anthu 1,000.
16 Then Samson sayd, With the iaw of an asse are heapes vpon heapes: with the iawe of an asse haue I slaine a thousand men.
Ndipo Samsoni anati, “Ndi chibwano cha bulu, milu ndi milu ya anthu. Ndi chibwano cha bulu, ndapha anthu 1,000.”
17 And when he had left speaking, hee cast away the iawebone out of his hande, and called that place, Ramath-Lehi.
Atatsiriza kuyankhula, anataya chibwanocho, ndipo malowo anawatcha Ramati-Lehi.
18 And he was sore a thirst, and called on the Lord, and sayde, Thou hast giuen this great deliuerance into the hand of thy seruaunt: and nowe shall I dye for thirst, and fall into the handes of the vncircumcised?
Pambuyo pake anamva ludzu kwambiri ndipo anayitana Yehova mopempha kuti, “Inu mwapatsa mtumiki wanu chipulumutso chachikulu chotere. Kodi tsopano ndife ndi ludzu ndi kugwidwa ndi anthu osachita mdulidwewa?”
19 Then God brake the cheeke tooth, that was in the iawe, and water came thereout: and when he had drunke, his Spirit came againe, and he was reuiued: wherefore the name therof is called, Enhakkore, which is in Lehi vnto this day.
Pamenepo Mulungu anangʼamba nthaka ku Lehi, ndipo madzi anatuluka mʼdzenjemo. Samsoni anamwa madziwo, ndipo mphamvu zake zinabwerera nakhalanso monga analili. Choncho chitsimecho chinatchedwa Eni-Hakore, ndipo chilipobe ku Lehiko mpaka lero.
20 And hee iudged Israel in the dayes of the Philistims twentie yeeres.
Samsoni anatsogolera Israeli pa nthawi ya Afilisti kwa zaka makumi awiri.

< Judges 15 >