< Joshua 1 >

1 Nowe after the death of Moses the seruant of the Lord, the Lord spake vnto Ioshua the sonne of Nun, Moses minister, saying,
Atamwalira Mose mtumiki wa Mulungu, Yehova anati kwa Yoswa mwana wa Nuni mthandizi wa Mose:
2 Moses my seruant is dead: nowe therefore arise, go ouer this Iorden, thou, and all this people, vnto the lande which I giue them, that is, to ye children of Israel.
“Mose mtumiki wanga wamwalira. Ndipo iwe ndi anthu onsewa, tsopano konzekani kuwoloka mtsinje wa Yorodani kupita ku dziko limene ndiwapatse Aisraeli onse.
3 Euery place that the sole of your foote shall treade vpon, haue I giuen you, as I said vnto Moses.
Paliponse pamene phazi lanu liponde, ndikupatsani monga momwe ndinalonjezera Mose.
4 From the wildernesse and this Lebanon euen vnto the great riuer, the riuer Perath: all the land of the Hittites, euen vnto the great Sea towarde the going downe of the sunne, shalbe your coast.
Dziko lanu lidzayambira ku chipululu kummwera mpaka ku mapiri a Lebanoni kumpoto, kuchokeranso ku mtsinje waukulu wa Yufurate kummawa, mpaka dziko lonse la Ahiti, kukafika ku Nyanja Yayikulu ya kumadzulo.
5 There shall not a man be able to withstande thee all the dayes of thy life: as I was with Moses, so will I be with thee: I will not leaue thee, nor forsake thee.
Palibe munthu amene adzatha kukugonjetsa masiku onse a moyo wako. Monga Ine ndinakhalira ndi Mose, chomwechonso ndidzakhala nawe. Sindidzakusiya kapena kukataya.
6 Be strong and of a good courage: for vnto this people shalt thou deuide the lande for an inheritance, which I sware vnto their fathers to giue them.
“Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima, chifukwa iwe udzatsogolera anthu awa kukalandira dziko limene Ine ndinalonjeza makolo awo kuti ndidzawapatsa.
7 Onely be thou strong, and of a most valiant courage, that thou mayest obserue and doe according to all the Lawe which Moses my seruant hath commanded thee: thou shalt not turne away from it to the right hande, nor to the left, that thou mayest prosper whithersoeuer thou goest.
Ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima kwambiri. Usamale ndithu kuti umvere malamulo onse amene mtumiki wanga Mose anakupatsa. Usachoke pa malamulo anga ndipo kulikonse kumene udzapite udzapambana.
8 Let not this booke of the Law depart out of thy mouth, but meditate therin day and night, that thou mayest obserue and doe according to all that is written therein: for then shalt thou make thy way prosperous, and then shalt thou haue good successe.
Uziwerenga Buku la Malamuloli, uzilingalira zolembedwa mʼmenemo usana ndi usiku, kuti uchite zonse zimene zinalembedwamo. Ukamatero udzapeza bwino ndi kupambana.
9 Haue not I commanded thee, saying, Be strong and of a good courage, feare not, nor be discouraged? for I the Lord thy God will be with thee, whithersoeuer thou goest.
Paja ndinakulamula kuti ukhale wamphamvu ndi wolimba mtima. Choncho usamachite mantha kapena kutaya mtima popeza Ine Yehova Mulungu wako ndidzakhala nawe kulikonse kumene udzapite.”
10 Then Ioshua commanded the officers of the people, saying,
Tsono Yoswa analamula atsogoleri a Aisraeli nawawuza kuti,
11 Passe through the hoste, and commande the people, saying, Prepare you vitailes: for after three dayes ye shall passe ouer this Iorden, to goe in to possesse the lande, which the Lord your God giueth you to possesse it.
“Pitani ku misasa yonse ndipo muwuze anthu kuti, ‘Konzekani, mangani katundu wanu, popeza pakapita masiku atatu kuyambira lero mudzawoloka Yorodani kupita kukatenga dziko limene Yehova Mulungu wanu akukupatsani.’”
12 And vnto the Reubenites, and to the Gadites, and to halfe the tribe of Manasseh spake Ioshua, saying,
Koma Yoswa anawuza fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase kuti,
13 Remember the worde, which Moses the seruant of the Lord commanded you, saying, The Lord your God hath giuen you rest, and hath giuen you this land.
“Kumbukirani zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani kuti, ‘Yehova Mulungu wanu akukupatsani mpumulo, ndi dziko ili kuti likhale lanu.’
14 Your wiues, your children, and your cattell shall remaine in the land which Moses gaue you on this side Iorden: but ye shall goe ouer before your brethren armed, all that be men of warre, and shall helpe them,
Tsono akazi anu, ana anu ndi ziweto zanu zitsale mʼdziko lino limene Mose anakupatsani kummawa kwa Yorodani. Koma ankhondo anu okha ndiwo awoloke atatenga zida zawo ndi kupita patsogolo pa abale anu kukawathandiza.
15 Vntill the Lord haue giuen your brethren rest, as well as to you, and vntill they also shall possesse the land, which the Lord your God giueth them: then shall ye returne vnto the lande of your possession and shall possesse it, which land Moses the Lordes seruant gaue you on this side Iorden toward the sunne rising.
Abale anuwo akadzalandira dziko limene Yehova Mulungu wanu akuwapatsa monga inu mwachitira, inu mudzabwerera kudzakhazikika mʼdziko lanu limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani tsidya la kummawa kwa Yorodani.”
16 Then they answered Ioshua, saying, Al that thou hast commanded vs, we will doe, and whithersoeuer thou sendest vs, we will goe.
Kenaka iwo anayankha Yoswa kuti, “Ife tidzachita chilichonse chimene mwatilamula, ndipo kulikonse kumene mudzatitume tidzapita.
17 As we obeyed Moses in all things, so will we obey thee: onely the Lord thy God be with thee, as he was with Moses.
Monga momwe tinamvera Mose kwathunthu, chomwechonso tidzakumvera iwe. Yehova Mulungu wanu akhale nanu monga momwe anachitira ndi Mose.
18 Whosoeuer shall rebell against thy commandement, and will not obey thy wordes in all that thou commaundest him, let him bee put to death: onely be strong and of good courage.
Aliyense wotsutsana ndi inu kapena wosamvera zimene mutilamula adzaphedwa. Inu mukhale wamphamvu ndi wolimba mtima!”

< Joshua 1 >