< Joshua 6 >

1 Now Iericho was shut vp, and closed, because of the children of Israel: none might go out nor enter in.
Tsono mzinda wa Yeriko unali utatsekedwa kuti Aisraeli asalowe. Palibe amene amatuluka kapena kulowa.
2 And the Lord saide vnto Ioshua, Behold, I haue giuen into thine hand Iericho and the King thereof, and the strong men of warre.
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa, “Taona ndapereka Yeriko, pamodzi ndi mfumu yake ndi ankhondo ake mʼmanja mwako.
3 All ye therefore that be men of warre, shall compasse the citie, in going round about the citie once: thus shall you doe sixe dayes:
Tsono iwe pamodzi ndi ankhondo ako onse muzizungulira mzindawu masiku asanu ndi limodzi, kamodzi pa tsiku.
4 And seuen Priests shall beare seuen trumpets of rams hornes before the Arke: and the seuenth day ye shall compasse the citie seuen times, and the Priests shall blow with the trumpets.
Ansembe asanu ndi awiri, atanyamula malipenga a nyanga za nkhosa zazimuna, akhale patsogolo pa Bokosi la Chipangano. Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri mudzazungulire mzindawu kasanu ndi kawiri ansembe akuliza malipenga.
5 And when they make a long blast with the rams horne, and ye heare the sound of the trumpet, al the people shall shoute with a great shoute: then shall the wall of the citie fall downe flat, and the people shall ascend vp, euery man streight before him.
Ansembe adzalize malipenga kosalekeza. Tsono anthu onse akadzamva kuliza kumeneku adzafuwule kwambiri, ndipo makoma a mzindawo adzagwa. Zikadzatero ankhondo adzalowe mu mzindawo.”
6 Then, Ioshua the sonne of Nun called the Priests and said vnto them, Take vp the Arke of the couenant, and let seuen Priests beare seuen trumpets of rams hornes before the Arke of the Lord.
Ndipo Yoswa mwana wa Nuni anayitana ansembe ndipo anawawuza kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano cha Yehova ndipo ansembe asanu ndi awiri anyamule malipenga. Iwowa akhale patsogolo pake.”
7 But he said vnto the people, Goe and compasse the citie: and let him that is armed, go forth before the Arke of the Lord.
Ndipo analamulira anthu kuti, “Yambani kuyenda! Yendani mozungulira mzinda ndipo ankhondo akhale patsogolo pa Bokosi la Yehova.”
8 And when Ioshua had spoken vnto the people, the seuen Priestes bare the seuen trumpets of rams hornes, and went foorth before the Arke of the Lord, and blew with the trumpets, and the Arke of the couenant of ye Lord followed them.
Mofanana ndi mmene Yoswa anayankhulira kwa anthu aja, ansembe asanu ndi awiri anapita patsogolo pa Bokosi la Chipangano la Yehova akuliza malipenga a nyanga za nkhosa zija, ndipo Bokosi la Chipangano cha Yehova limabwera pambuyo pawo.
9 And the men of armes went before the Priestes, that blewe the trumpets: then the gathering hoste came after the Arke, as they went and blewe the trumpets.
Ankhondo amayenda patsogolo pa ansembe amene amayimba malipenga, ndiponso gulu lina pambuyo pa Bokosilo. Nthawi yonseyi nʼkuti malipenga akulira.
10 (Nowe Ioshua had commanded the people, saying, Ye shall nor shout, neither make any noyse with your voyce, neither shall a worde proceede out of your mouth, vntill the day that I say vnto you, Shout, then shall ye shoute)
Koma Yoswa nʼkuti atalamulira anthu kuti, “Musafuwule, musakweze mawu anu kapena kuyankhula mpaka tsiku limene ndidzakuwuzani kuti mufuwule. Pamenepo mudzafuwule!”
11 So the Arke of the Lord compassed the citie, and went about it once: then they returned into the hoaste, and lodged in the campe.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anazungulira mzindawo kamodzi. Kenaka anthu anabwerera ku msasa wawo kukagona.
12 And Ioshua rose early in the morning, and the Priestes bare the Arke of the Lord:
Yoswa anadzuka mmawa tsiku linalo ndipo ansembe ananyamula Bokosi la Yehova.
13 Also seuen Priests bare seuen trumpets of rams hornes, and went before the Arke of the Lord, and going blewe with the trumpets: and the men of armes went before them, but the gathering hoste came after the Arke of the Lord, as they went and blewe the trumpets.
Ansembe asanu ndi awiri onyamula malipenga asanu ndi awiri anakhala patsogolo pa Bokosi la Yehova akuyimba malipenga. Ankhondo anali patsogolo pawo ndipo gulu lina linatsatira Bokosi la Yehova. Apa nʼkuti malipenga akulira.
14 And the second day they compassed the citie once, and returned into the host: thus they did sixe dayes.
Tsiku lachiwiri anazunguliranso mzinda kamodzi ndi kubwerera ku misasa. Iwo anachita izi kwa masiku asanu ndi limodzi.
15 And when the seuenth day came, they rose early, euen with the dawning of the day, and compassed the citie after ye same maner seuen times: only that day they compassed the citie seuen times.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri, anadzuka mʼbandakucha ndipo anazungulira mzindawo kasanu ndi kawiri. Ndi pa tsiku lokhali limene anazungulira mzindawu kasanu ndi kawiri.
16 And when the Priests had blowen ye trumpets the seuenth time, Ioshua said vnto ye people, Shoute: for the Lord hath giuen you the citie.
Pomwe amazungulira kachisanu ndi chiwiri, ansembe akuliza malipenga mokweza, Yoswa analamulira anthu kuti “Fuwulani pakuti Yehova wakupatsani mzindawu!
17 And the citie shalbe an execrable thing, both it, and all that are therein, vnto the Lord: onely Rahab the harlot shall liue, shee, and all that are with her in the house: for shee hid the messengers that we sent.
Mzindawu ndi zonse zimene zili mʼmenemo muziwononge. Rahabe yekha, mayi wadama, ndi aliyense amene ali pamodzi naye mʼnyumba mwake asaphedwe, chifukwa anabisa anthu odzazonda, amene ife tinawatuma
18 Notwithstanding, be ye ware of the execrable thing, lest ye make your selues execrable, and in taking of the execrable thing, make also the hoste of Israel execrable, and trouble it.
Koma musatenge kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa. Mukadzangotenga kanthu kalikonse koyenera kuwonongedwa, mudzaputa mavuto, misasa ya Israeli idzawonongedwa.
19 But all siluer, and gold, and vessels of brasse, and yron shalbe consecrate vnto the Lord, and shall come into the Lordes treasury.
Zonse za siliva ndi golide, ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo, ndi zake za Yehova ndipo ziyenera kukasungidwa mosungiramo chuma chake.”
20 So the people shouted, whe they had blowen trumpets: for when the people had heard the sound of the trumpet, they shouted with a great shoute: and the wall fel downe flat: so the people went vp into the citie, euery man streight before him: and they tooke the citie.
Ansembe analiza malipenga. Anthu atamva kulira kwa malipenga, anafuwula kwambiri ndipo makoma a Yeriko anagwa. Choncho ankhondo anabwera ku mzinda uja nawulanda.
21 And they vtterly destroyed all that was in the citie, both man and woman, yong, and olde, and oxe, and sheepe, and asse, with the edge of the sword.
Iwo analowa mu mzindawo nawononga ndi lupanga chilichonse chamoyo kuyambira amuna, akazi, ana ndi akulu, ngʼombe, nkhosa ndi abulu.
22 But Ioshua had said vnto the two men that had spied out the countrey, Go into the harlots house, and bring out thence the woman, and all that she hath, as ye sware to her.
Yoswa anawuza anthu awiri amene anakazonda dziko aja kuti, “Pitani ku nyumba ya mkazi wadama uja ndipo mukamutulutse iye pamodzi ndi onse amene ali naye ndipo mukabwere nawo kuno, munamulumbirira.”
23 So the yong men that were spies, went in, and brought out Rahab, and her father, and her mother, and her brethren, and all that shee had: also they brought out all her familie, and put them without the host of Israel.
Choncho iwo anapita nakatenga Rahabe, abambo ake ndi amayi ake, abale ake ndi onse amene anali naye. Iwo anatulutsa banja lake lonse ndipo analiyika kuseri kwa msasa wa Aisraeli.
24 After they burnt the citie with fire, and all that was therein: onely the siluer and the gold, and the vessels of brasse and yron, they put vnto the treasure of the house of the Lord.
Kenaka iwo anawotcha mzinda wonse ndi chilichonse chimene chinali mʼmenemo, kupatulapo zasiliva ndi zagolide pamodzi ndi ziwiya zamkuwa ndi zachitsulo zimene anakaziyika mʼnyumba yosungiramo chuma cha Yehova.
25 So Ioshua saued Rahab the harlot, and her fathers houshold, and all that shee had; and shee dwelt in Israel euen vnto this day, because shee had hid the messengers, which Ioshua sent to spie out Iericho.
Koma Yoswa sanaphe Rahabe, mkazi wadamayo pamodzi ndi banja lake ndi onse amene anali naye, chifukwa anabisa anthu amene iye anawatuma kukazonda Yeriko. Zidzukulu zake za Rahabeyo zikukhala pakati pa Aisraeli mpaka lero.
26 And Ioshua sware at that time, saying, Cursed be the man before ye Lord, that riseth vp, and buildeth this citie Iericho: hee shall lay the foundation thereof in his eldest sonne, and in his yongest sonne shall hee set vp the gates of it.
Pa nthawi imeneyo Yoswa anapereka chenjezo motemberera kuti, “Akhale wotembereredwa pamaso pa Yehova munthu amene adzamangenso mzinda uwu wa Yeriko: “Aliyense amene adzayike maziko ake, mwana wake wamwamuna wachisamba adzafa, aliyense womanga zipata zake mwana wake wamngʼono adzafa.”
27 So the Lord was with Ioshua, and he was famous through all the world.
Motero Yehova anali ndi Yoswa, ndipo mbiri yake inafalikira dziko lonse.

< Joshua 6 >