< Joshua 4 >
1 And when all the people were wholy gone ouer Iorden, (after the Lord had spoken vnto Ioshua, saying,
Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
2 Take you twelue me out of the people, out of euery tribe a man,
“Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
3 And command you them, saying, Take you hence out of the middes of Iorden, out of the place where the Priestes stoode in a readinesse, twelue stones, which ye shall take away with you, and leaue them in the lodging where you shall lodge this night)
Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
4 Then Ioshua called the twelue men, whome he had prepared of the children of Israel, out of euery tribe a man,
Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
5 And Ioshua said vnto them, Go ouer before the Arke of the Lord your God, euen through the middes of Iorden, and take vp euery man of you a stone vpon his shoulder according vnto the nomber of the tribes of the children of Israel,
ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
6 That this may bee a signe among you, that whe your children shall aske their fathers in time to come, saying, What meane you by these stones?
kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
7 Then ye may answere them, That the waters of Iorden were cut off before the Arke of the couenant of the Lord: for when it passed through Iorden, the waters of Iorden were cut off: therefore these stones are a memoriall vnto the children of Israel for euer.
Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
8 Then ye children of Israel did euen so as Ioshua had commanded, and tooke vp twelue stones out of the mids of Iorden as ye Lord had said vnto Ioshua, according to the nomber of the tribes of the children of Israel, and caried them away with them vnto the lodging, and layd them down there.
Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
9 And Ioshua set vp twelue stones in the middes of Iorden, in the place where the feete of the Priests, which bare the Arke of the couenant stood, and there haue they continued vnto this day.
Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
10 So the Priests, which bare ye Arke, stoode in the middes of Iorden, vntill euery thing was finished that ye Lord had comanded Ioshua to say vnto the people, according to all that Moses charged Ioshua: then the people hasted and went ouer.
Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
11 When all the people were cleane passed ouer, the Arke of the Lord went ouer also, and the Priests before the people.
Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
12 And the sonnes of Reuben, and the sonnes of Gad, and halfe the tribe of Manasseh went ouer before the children of Israel armed, as Moses had charged them.
Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
13 Euen fourty thousand prepared for warre, went before the Lord vnto battel, into ye plaine of Iericho.
Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
14 That day the Lord magnified Ioshua in the sight of all Israel, and they feared him, as they feared Moses all dayes of his life.
Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
15 And the Lord spake vnto Ioshua, saying,
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
16 Commande the Priests that beare ye Arke of the testimonie, to come vp out of Iorden.
“Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
17 Ioshua therefore commanded the Priests, saying, Come ye vp out of Iorden.
Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
18 And when the Priests that bare the Arke of the couenant of ye Lord were come vp out of the middes of Iorden, and assoone as the soles of the Priests feete were set on the dry land, the waters of Iorde returned vnto their place, and flowed ouer all the bankes thereof, as they did before.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
19 So the people came vp out of Iorden the tenth day of the first moneth, and pitched in Gilgal, in the Eastside of Iericho.
Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
20 Also the twelue stones, which they tooke out of Iorden, did Ioshua pitch in Gilgal.
Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
21 And he spake vnto ye childre of Israel, saying, When your children shall aske their fathers in time to come, and say, What meane these stones?
Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
22 Then ye shall shew your children, and say, Israel came ouer this Iorden on dry land:
Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
23 For the Lord your God dryed vp ye waters of Iorden before you, vntill ye were gone ouer, as the Lord your God did the red Sea, which hee dryed vp before vs, till we were gone ouer,
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
24 That all the people of the worlde may know that the hand of the Lord is mightie, that ye might feare the Lord your God continually.
Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”