< Joshua 3 >
1 Then Ioshua rose very earely, and they remoued from Shittim, and came to Iorden, he, and all the children of Israel, and lodged there, before they went ouer.
Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
2 And after three dayes the officers went throughout the hoste,
Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
3 And commanded the people, saying, When ye see the Arke of the couenat of the Lord your God, and the Priestes of the Leuites bearing it, ye shall depart from your place, and goe after it.
kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
4 Yet there shalbe a space betweene you and it, about two thousande cubites by measure: ye shall not come neere vnto it, that ye may knowe the way, by the which ye shall goe: for ye haue not gone this way in times past.
Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
5 (Nowe Ioshua had saide vnto the people, Sanctifie your selues: for to morowe the Lord will doe wonders among you)
Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
6 Also Ioshua spake vnto the Priestes, saying, Take vp the Arke of the couenant, and goe ouer before the people: so they tooke vp the Arke of the couenant, and went before the people.
Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
7 Then the Lord saide vnto Ioshua, This day will I begin to magnifie thee in the sight of all Israel, which shall knowe, that as I was with Moses, so will I be with thee.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
8 Thou shalt therefore command the Priests that beare the Arke of the Couenant, saying, When ye are come to the brinke of the waters of Iorden, ye shall stande still in Iorden.
Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
9 Then Ioshua said vnto the children of Israel, Come hither, and heare the wordes of the Lord your God.
Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
10 And Ioshua said, Hereby ye shall know that the liuing God is among you, and that he will certainely cast out before you the Canaanites, and the Hittites, and the Hiuites, and the Perizzites, and the Girgashites, and the Amorites, and the Iebusites.
Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
11 Beholde, the Arke of the couenant of the Lord of all the worlde passeth before you into Iorden.
Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
12 Nowe therefore take from among you twelue men out of the tribes of Israel, out of euery tribe a man.
Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
13 And assoone as the soles of the feete of the Priestes (that beare the Arke of the Lord God the Lord of all the worlde) shall stay in the waters of Iorden, the waters of Iorden shall be cut off: for the waters that come from aboue, shall stande still vpon an heape.
Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
14 Then when the people were departed from their tentes to goe ouer Iorden, the Priestes bearing the Arke of the Couenant, went before people.
Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
15 And as they that bare the Arke came vnto Iorden, and the feete of the Priestes that bare the Arke were dipped in the brinke of the water, (for Iorden vseth to fill all his bankes all the time of haruest)
Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
16 Then the waters that came downe from aboue, stayed and rose vpon an heape and departed farre from the citie of Adam, that was beside Zaretan: but the waters that came downe towarde the Sea of the wildernes, euen the salt Sea, failed, and were cut off: so the people went right ouer against Iericho.
madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
17 But the Priestes that bare the Arke of the couenant of the Lord, stoode drie within Iorden readie prepared, and all the Israelites went ouer dry, vntill all the people were gone cleane ouer through Iorden.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.