< Joshua 24 >
1 And Ioshua assembled againe all the tribes of Israel to Shechem, and called the Elders of Israel, and their heades, and their iudges, and their officers, and they presented themselues before God.
Tsono Yoswa anasonkhanitsa mafuko onse a Israeli ku Sekemu. Iye anayitanitsa akuluakulu, atsogoleri, oweruza, ndi akuluakulu a boma la Israeli, ndipo iwo anafika pamaso pa Mulungu.
2 Then Ioshua said vnto all the people, Thus saith the Lord God of Israel, Your fathers dwelt beyond the flood in olde time, euen Terah the father of Abraham, and the father of Nachor, and serued other gods.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Yehova Mulungu wa Israeli akuti, ‘Kalekale makolo anu, kuphatikiza Tera, abambo a Abrahamu ndi Nahori ankakhala kutsidya kwa Mtsinje ndipo ankapembedza milungu ina.
3 And I tooke your father Abraham from beyond the flood, and brought him through all the land of Canaan, and multiplied his seede, and gaue him Izhak.
Koma ine ndinatenga kholo lanu Abrahamu kumuchotsa ku dziko la kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndipo ndinamutsogolera kupita ku dziko la Kanaani. Ndinamupatsa zidzukulu zambiri. Ndinamupatsa Isake,
4 And I gaue vnto Izhak, Iaakob and Esau: and I gaue vnto Esau mount Seir, to possesse it: but Iaakob and his children went downe into Egypt.
ndipo Isake ndinamupatsa Yakobo ndi Esau. Ndinapereka dziko la mapiri la Seiri kwa Esau, koma Yakobo ndi ana ake anapita ku Igupto.
5 I sent Moses also and Aaron, and I plagued Egypt: and when I had so done among them, I brought you out.
“‘Kenaka ndinatuma Mose ndi Aaroni, ndipo ine ndinazunza Aigupto. Pambuyo pake ndinakutulutsani.
6 So I brought your fathers out of Egypt, and ye came vnto the Sea, and the Egyptians pursued after your fathers with charets and horsemen vnto the red sea.
Nditatulutsa makolo anu ku Igupto ndinafika nawo ku Nyanja Yofiira. Aigupto anawathamangira ndi magaleta ndi okwera pa akavalo mpaka ku Nyanja Yofiira.
7 Then they cryed vnto the Lord, and he put a darkenesse betweene you and the Egyptians, and brought the sea vpon them, and couered them: so your eyes haue seene what I haue done in Egypt also ye dwelt in the wildernesse a long season.
Tsono makolo anuwo anapemphera kwa Ine kuti ndiwathandize, ndipo ndinayika mtambo wakuda pakati pawo ndi Aiguptowo, ndipo Nyanja inamiza Aigupto aja. Inu munaona ndi maso anu zimene ndinachita kwa Aiguptowo ndipo inu munakhala mʼchipululu nthawi yayitali.
8 After, I brought you into the land of the Amorites, which dwelt beyond Iorden, and they fought with you: but I gaue them into your hand, and ye possessed their countrey, and I destroyed them out of your sight.
“‘Pambuyo pake Ine ndinabwera nanu ku dziko la Aamori amene amakhala kummawa kwa Yorodani. Iwo anamenyana nanu koma ndinawapereka mʼdzanja lanu. Ndinawawononga pamaso panu, ndipo inu munalanda dziko lawo.
9 Also Balak the sonne of Zippor King of Moab arose and warred against Israel, and sent to call Balaam the sonne of Beor for to curse you,
Balaki mwana wa Zipori, mfumu ya Mowabu, analimbana ndi Israeli. Iye anayitanitsa Balaamu mwana wa Beori kuti akutemberereni.
10 But I would not heare Balaam: therefore he blessed you, and I deliuered you out of his hand.
Koma ine sindinamvere Balaamu, kotero iye anakudalitsani mowirikiza ndipo ndinakulanditsani mʼdzanja lake.
11 And ye went ouer Iorden, and came vnto Iericho, and the men of Iericho fought against you, the Amorites, and the Perizzites, and the Canaanites, and the Hittites, and the Girgashites, the Hiuites and the Iebusites, and I deliuered them into your hand.
“‘Ndipo inu munawoloka Yorodani ndi kufika ku Yeriko. Anthu a ku Yeriko analimbana nanu pamodzi ndi Aamori, Aperezi, Akanaani, Ahiti, Agirigasi, Ahivi ndi Ayebusi. Koma Ine ndinawapereka mʼdzanja lanu.
12 And I sent hornets before you, which cast them out before you, euen the two kings of the Amorites, and not with thy sword, nor with thy bow.
Ine ndinatumiza mavu amene anapirikitsa mafumu awiri Aamori aja pamaso panu. Inu simunachite izi ndi lupanga ndi uta wanu.
13 And I haue giuen you a land, wherein ye did not labour, and cities which ye built not, and yee dwell in them, and eate of the vineyards and oliue trees, which yee planted not.
Motero ndinakupatsani dziko limene simunalivutikire ndiponso mizinda imene simunamange. Inu mukukhala mʼmenemo ndi kumadya zipatso za mʼmunda wamphesa ndi kuthyola zipatso mʼmitengo ya olivi zimene simunadzale.’
14 Nowe therefore feare the Lord, and serue him in vprightnesse and in trueth, and put away the gods, which your fathers serued beyonde the flood and in Egypt, and serue the Lord.
“Ndipo tsopano wopani Yehova ndi kumutumikira Iye mokhulupirika ndi moona. Chotsani milungu imene makolo anu ankapembedza kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate ndi ku Igupto ndipo tumikirani Yehova.
15 And if it seeme euill vnto you to serue the Lord, choose you this day whome yee will serue, whether the gods which your fathers serued (that were beyond the flood) or the gods of the Amorites, in whose land ye dwel: but I and mine house will serue the Lord.
Koma ngati kutumikira Yehova kukuyipirani, sankhani lero amene mudzamutumikire, kapena milungu imene makolo anu ankayitumikira kutsidya kwa mtsinje wa Yufurate, kapena milungu ya Aamori, amene mukukhala mʼdziko lawo. Koma ine ndi banja langa, tidzatumikira Yehova.”
16 Then the people answered and saide, God forbid, that we shoulde forsake the Lord, to serue other gods.
Ndipo anthu anayankha, “Sizingatheke kuti timusiye Yehova ndi kutumikira milungu ina!
17 For the Lord our God, he brought vs and our fathers out of the lande of Egypt, from the house of bondage, and he did those great miracles in our sight, and preserued vs in all the way that we went, and among all the people through whome we came.
Yehova Mulungu wathu ndiye amene anatitulutsa ife ndi makolo athu mu ukapolo, mʼdziko la Igupto. Tinaona ndi maso athu zizindikiro zozizwitsa zimene anachita. Iye anatiteteza pa ulendo wathu wonse ndi pakati pa mitundu yonse imene tinkakumana nayo.
18 And the Lord did cast out before vs all the people, euen the Amorites which dwelt in the lande: therefore will we also serue the Lord, for he is our God.
Ife tikufika Iye anapirikitsa anthu onse pamodzi ndi Aamori amene ankakhala mʼdzikoli. Ifenso tidzatumikira Yehova chifukwa Iye ndiye Mulungu.”
19 And Ioshua saide vnto the people, Ye can not serue the Lord: for he is an holie God: he is a ielous God: hee will not pardon your iniquitie nor your sinnes.
Koma Yoswa anati kwa anthuwo, “Inutu simungathe kutumikira Yehova. Iye ndi Mulungu woyera, salola kupikisana naye. Sadzakukhululukirani ngati mumuwukira ndi kumuchimwira.
20 If yee forsake the Lord and serue strange gods, then he will returne and bring euill vpon you, and consume you, after that hee hath done you good.
Ngati inu musiya Yehova ndi kutumikira milungu yachilendo, adzakufulatirani. Iye adzakulangani ndi kukuwonongani ngakhale kuti poyamba anakuchitirani zabwino.”
21 And the people saide vnto Ioshua, Nay, but we will serue the Lord.
Koma anthuwo anati kwa Yoswa, “Ayi! Ife tidzatumikira Yehova.”
22 And Ioshua saide vnto the people, Yee are witnesses against your selues, that yee haue chosen you the Lord, to serue him: and they sayd, We are witnesses.
Kenaka Yoswa anati, “Inu mukudzichitira nokha umboni kuti mwasankha kutumikira Yehova.” Iwo anayankha kuti, “Inde ife ndife mboni.”
23 Then put away nowe, saide he, the strange gods which are among you, and bowe your hearts vnto the Lord God of Israel.
Yoswa anati, “Tsono chotsani milungu yachilendo imene ili pakati panu ndipo perekani mitima yanu kwa Yehova Mulungu wa Israeli.”
24 And ye people saide vnto Ioshua, The Lord our God wil we serue, and his voyce wil we obey.
Ndipo anthuwo anati kwa Yoswa, “Ife tidzatumikira Yehova Mulungu wathu ndi kumvera Iye.”
25 So Ioshua made a couenant with the people the same day, and gaue them an ordinance and lawe in Shechem.
Choncho pa tsiku limenelo Yoswa anachita pangano mʼmalo mwa anthuwo, ndipo pa Sekemu pomwepo iye anapereka malamulo ndi malangizo kwa anthu aja.
26 And Ioshua wrote these woordes in the booke of the Lawe of God, and tooke a great stone, and pitched it there vnder an oke that was in the Sanctuarie of the Lord.
Ndipo Yoswa analemba zinthu izi mʼbuku la malamulo a Mulungu. Kenaka iye anatenga mwala waukulu nawuyimika pansi pa mtengo wa thundu pa malo wopatulika a Yehova.
27 And Ioshua saide vnto all the people, Beholde, this stone shall be a witnesse vnto vs: for it hath heard all the wordes of the Lord which he spake with vs: it shall be therefore a witnesse against you, lest yee denie your God.
Yoswa anati kwa anthu onse, “Tamvani! Mwala uwu udzakhala mboni yotitsutsa. Mwalawu wamva mawu onse amene Yehova wayankhula kwa ife. Udzakhala mboni yotitsutsa ngati mukhala osakhulupirika kwa Mulungu wanu.”
28 Then Ioshua let the people depart, euery man vnto his inheritance.
Kenaka Yoswa analola anthu kuti apite, aliyense ku dera lake.
29 And after these things Ioshua the sonne of Nun, the seruaunt of the Lord died, being an hundreth and ten yeeres olde.
Zitatha zinthu izi, Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Yehova, anamwalira ali ndi zaka 110,
30 And they buried him in ye border of his inheritance in Timnath-serah, which is in mount Ephraim, on the Northside of mount Gaash.
ndipo anamuyika mʼmanda mʼdziko lake, ku Timnati-Sera dziko lamapiri la ku Efereimu, kumpoto kwa phiri la Gaasi.
31 And Israel serued the Lord all the daies of Ioshua, and all the daies of the Elders that ouerliued Ioshua, and which had knowen all the workes of the Lord that he had done for Israel.
Israeli anatumikira Yehova pa nthawi yonse imene Yoswa anali ndi moyo ndiponso pa nthawi ya akuluakulu amene anali moyo Yoswa atamwalira, anthu amene ankadziwa zonse zimene Yehova anachitira Israeli.
32 And the bones of Ioseph, which the children of Israel brought out of Egypt, buried they in Shechem in a parcell of ground which Iaakob bought of the sonnes of Hamor the father of Shechem, for an hundreth pieces of siluer, and the children of Ioseph had them in their inheritance.
Ndipo mafupa a Yosefe amene Aisraeli anawatulutsa ku Igupto anawayika mʼmanda a ku Sekemu pa malo amene Yakobo anagula ndi ndalama zasiliva 100 kwa ana a Hamori, abambo a Sekemu. Malo awa anakhala cholowa cha adzukulu a Yosefe.
33 Also Eleazar the sonne of Aaron died, whome they buried in the hill of Phinehas his sonne, which was giuen him in mount Ephraim.
Ndipo Eliezara mwana wa Aaroni anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda ku Gibeya, malo amene anapatsidwa kwa Finehasi mwana wake, mʼdziko lamapiri la Efereimu.