< Joshua 22 >

1 Then Ioshua called the Reubenites, and the Gadites, and the halfe tribe of Manasseh,
Pambuyo pake Yoswa anayitanitsa fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase,
2 And sayd vnto them, Ye haue kept all that Moses the seruaunt of the Lord commanded you, and haue obeied my voice in all that I commanded you:
ndipo anawawuza kuti, “Inu mwachita zonse zimene Mose mtumiki wa Yehova anakulamulani, ndipo mwamvera mu zonse zimene ndinakulamulirani.
3 You haue not forsaken your brethren this long season vnto this day, but haue diligently kept the commandement of the Lord your God.
Aisraeli anzanu simunawasiye nthawi yayitali yonseyi mpaka lero lino. Inu mwaonetsetsa kuti mwachita zonse zimene Yehova anakulamulani.
4 And nowe the Lord hath giuen rest vnto your brethren as he promised them: therefore nowe returne ye and goe to your tentes, to the land of your possession, which Moses the seruant of the Lord hath giuen you beyond Iorden.
Tsono pakuti Yehova Mulungu wanu wapereka mpumulo kwa abale anu monga anayankhulira nawo, bwererani ku nyumba zanu ku dziko limene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani, dziko limene lili pa tsidya la Yorodani kummawa.
5 But take diligent heede, to doe the commandement and Lawe, which Moses the seruant of the Lord commanded you: that is, that ye loue the Lord your God, and walke in all his wayes, and keepe his commandements, and cleaue vnto him, and serue him with all your heart and with all your soule.
Koma samalitsani kuti mumvere malamulo ndi malangizo amene Mose mtumiki wa Yehova anakupatsani: kukonda Yehova Mulungu wanu, kuchita zimene iye amafuna, kumvera malamulo ake, kukhala okhulupirika kwa Iye ndi kumutumikira ndi mtima wanu wonse ndi moyo wanu wonse.”
6 So Ioshua blessed them and sent them away, and they went vnto their tents.
Ndipo Yoswa anawadalitsa ndi kuwalola kuti apite ndipo anapitadi ku nyumba zawo.
7 Nowe vnto one halfe of the tribe of Manasseh Moses had giuen a possession in Bashan: and vnto the other halfe thereof gaue Ioshua among their brethren on this side Iorden Westwarde: therefore when Ioshua sent them away vnto their tents, and blessed them,
Apa nʼkuti Mose atapereka dziko la Basani ku theka lina la fuko la Manase. Koma theka lina la fuko la Manase Yoswa analipatsa dziko la kumadzulo kwa Yorodani pamodzi ndi abale awo onse. Pamene Yoswa ankawatumiza kwawo anthu amenewa, anawadalitsa,
8 Thus he spake vnto them, saying, Returne with much riches vnto your tents, and with a great multitude of cattell, with siluer and with golde, with brasse and with yron, and with great abundance of rayment: deuide the spoyle of your enemies with your brethren.
nawawuza kuti, “Mukubwerera kwanu ndi chuma chambiri. Muli ndi ngʼombe zambiri pamodzi ndi siliva, golide, mkuwa ndi chitsulo, ndiponso zovala zambiri. Izi zimene munafunkha kwa adani anu agawireni abale anu.”
9 So the children of Reuben, and the children of Gad, and halfe the tribe of Manasseh returned, and departed from the children of Israel from Shiloh (which is in the land of Canaan) to goe vnto the countrey of Gilead to the land of their possession, which they had obteyned, according to ye word of the Lord by the hand of Moses.
Choncho mafuko a Rubeni, Gadi, pamodzi ndi theka la fuko la Manase anabwerera kwawo. Aisraeli ena onse anawasiya ku Silo mʼdziko la Kanaani. Tsono anapita ku dziko la Giliyadi, dziko limene linali lawo popeza analilandira potsata malamulo a Yehova kudzera mwa Mose.
10 And when they came vnto the borders of Iorden (which are in the land of Canaan) then the children of Reuben, and the children of Gad, and the halfe tribe of Manasseh, built there an altar by Iorden, a great altar to see to.
Atafika ku Geliloti, malo amene ali mʼmbali mwa mtsinje wa Yorodani mʼdziko la Kanaani, fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase anamanga guwa lansembe lalikulu pamenepo.
11 When the children of Israel heard say, Beholde, the children of Reuben, and the children of Gad, and the halfe tribe of Manasseh haue built an altar in the forefront of the lande of Canaan vpon the borders of Iorden at the passage of the children of Israel:
Ndipo pamene Aisraeli ena onse anawuzidwa kuti anthu a fuko la Rubeni, fuko la Gadi ndi theka la fuko la Manase amanga guwa lansembe mʼmalire a Kanaani ku Geliloti, ku tsidya lathu lino la Yorodani,
12 When the children of Israel heard it, then the whole Congregation of the children of Israel gathered them together at Shiloh to goe vp to warre against them.
gulu lonse la Aisraeli linasonkhana ku Silo kuti lipite kukachita nawo nkhondo.
13 Then the children of Israel sent vnto the children of Reuben, and to the children of Gad, and to ye halfe tribe of Manasseh into the land of Gilead, Phinehas the sonne of Eleazar the Priest,
Choncho Aisraeli anatumiza Finehasi mwana wa wansembe, Eliezara ku dziko la Giliyadi kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase.
14 And with him ten princes, of euery chiefe house a prince, according to all the tribes of Israel: for euery one was chiefe of their fathers housholde among the thousands of Israel.
Pamodzi ndi Finehasiyo anatumiza akuluakulu khumi ochokera ku fuko lililonse la Aisraeli. Aliyense mwa akuluakulu amenewa anali mtsogoleri wa banja limodzi la mafuko a Aisraeli.
15 So they went vnto the children of Reuben, and to the children of Gad, and to the halfe tribe of Manasseh, vnto the land of Gilead, and spake with them, saying,
Atafika ku Giliyadi anawuza fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lija la fuko la Manase kuti,
16 Thus saith the whole congregation of the Lord, What transgression is this that ye haue transgressed against the God of Israel, to turne away this day from the Lord, in that ye haue built you an altar for to rebell this day against the Lord?
“Gulu lonse likukufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mwachita chinthu chonyansa chotere potsutsana ndi Mulungu wa Israeli? Nʼchifukwa chiyani mwapatuka ndi kuleka kutsata Yehova podzimangira nokha guwa lansembe? Mwapandukiratu Yehova!
17 Haue we too litle for the wickednesse of Peor, whereof we are not clensed vnto this day, though a plague came vpon the Congregation of the Lord?
Kodi tchimo lija la ku Peori ndi lochepa kwa inu? Paja Yehova analanga gulu lonse ndi mliri chifukwa cha tchimolo, ndipo mpaka lero tchimo limene lija tikanazunzika nalobe.
18 Ye also are turned away this day from the Lord: and seeing ye rebell to day against ye Lord, euen to morowe he will be wroth with all the Congregation of Israel.
Kodi inu tsono mufuna kupatuka kuleka kumutsata Yehova? “‘Ngati lero mumupandukira Yehovayo, ndiye kuti mawamawali Iye adzakwiyira gulu lonse wa Israeli.
19 Notwithstanding if the land of your possession be vncleane, come ye ouer vnto the land of the possession of the Lord, wherein the Lordes Tabernacle dwelleth, and take possession among vs: but rebell not against the Lord, nor rebell not against vs in building you an altar, beside the altar of the Lord our God.
Ngati dziko limene inu mwatenga ndi loyipitsidwa, bwerani ku dziko la Yehova kumene kuli chihema chake kuja, ndipo mukhale nafe limodzi. Koma inu musawukire Yehova kapena kutisandutsa ife kukhala opanduka podzimangira guwa lansembe, kuwonjezera pa guwa lansembe la Yehova Mulungu wanu.
20 Did not Achan ye sonne of Zerah trespasse grieuously in the execrable thing, and wrath fell on all the Congregation of Israel? and this man alone perished not in his wickednesse.
Kumbukirani pamene Akani mwana wa Zera anakana kumvera lamulo la zinthu zoyenera kuwonongedwa, kodi suja mkwiyo wa Yehova unagwera gulu lonse la Israeli? Akaniyo sanafe yekha chifukwa cha tchimo lakelo.’”
21 Then the children of Reuben and the children of Gad, and halfe the tribe of Manasseh answered, and saide vnto the heads ouer the thousands of Israel,
Tsono mafuko a Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawayankha atsogoleri a mabanja a Israeli aja kuti,
22 The Lord God of gods, the Lord God of gods, he knoweth, and Israel himselfe shall know: if by rebellion, or by transgression against ye Lord we haue done it, saue thou vs not this day.
“Wamphamvu uja, Mulungu ndiye Yehova! Wamphamvu uja Mulungu ndiye Yehova. Iyeyu ndiye akudziwa chifukwa chiyani tinachita zimenezi. Tikufunanso kuti inu mudziwe. Ngati tinachita izi mopandukira ndiponso moonetsa kusakhulupirira Yehova, lero lomwe lino musatisiye ndi moyo.
23 If we haue built vs an altar to returne away from the Lord, either to offer thereon burnt offering, or meate offering, or to offer peace offerings thereon, let the Lord himselfe require it:
Ngati tinapandukira Yehova ndi kuleka kumutsata pamene tinadzimangira guwa loti tizipserezerapo nsembe kapena kupereka nsembe zaufa, kapena nsembe za mtendere, Yehova yekha ndiye atilange.
24 And if we haue not rather done it for feare of this thing, saying, In time to come your children might say vnto our children, What haue ye to doe with the Lord God of Israel?
“Ayi! Ife tinachita izi kuopa kuti tsiku lina zidzukulu zanu zingadzanene kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Kodi inu mukufuna chiyani kwa Yehova Mulungu wa Israeli?
25 For the Lord hath made Iorden a border betweene vs and you, ye children of Reuben, and of Gad: therefore ye haue no part in the Lord: so shall your children make our children cease from fearing the Lord.
Yehova anayika mtsinje wa Yorodani kukhala malire pakati pa ife ndi inu, anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi. Inuyo mulibe gawo mwa Yehova.’ Tsono mwina zidzukulu zanuzo nʼkudzaletsa zathu kupembedza Yehova.
26 Therefore we said, We will nowe go about to make vs an altar, not for burnt offering, nor for sacrifice,
“Nʼchifukwa chake tinaganiza kuti, ‘Tiyeni timange guwa lansembe, koma osati kuti tiziperekapo nsembe zopsereza kapena zopereka.’
27 But it shall be a witnesse betweene vs and you, and betweene our generations after vs, to execute the seruice of the Lord before him in our burnt offerings, and in our sacrifices, and in our peace offerings, and that your children should not say to our children in time to come, Ye haue no part in the Lord.
Koma mosiyana ndi zimenezi, guwali likhale umboni pakati pa ife ndi inu ndiponso mibado imene ikubwerayo, kuti ife timapembedzanso Yehova ndi nsembe zathu zopsereza, zopereka, ndiponso nsembe za mtendere. Motero mʼtsogolo muno zidzukulu zanu sizidzatha kunena kwa zidzukulu zathu kuti, ‘Inu mulibe gawo mwa Yehova!’
28 Therefore said we, If so be that they should so say to vs or to our generations in time to come, then will we answere, Beholde the facion of the altar of the Lord, which our fathers made, not for burnt offering nor for sacrifice, but it is a witnesse betweene vs and you.
“Ndipo ife tinati kuti, ‘Ngati iwo adzatiyankhulira kapena kuyankhulira zidzukulu zathu motero mʼtsogolo muno, ife tidzayankha kuti, onani guwa lansembe, lofanana ndi lomwe makolo athu anamanga osati loperekerapo nsembe zopsereza kapena nsembe zina koma ngati umboni pakati pa inu ndi ife.’
29 God forbid, that we should rebell against the Lord, and turne this day away from the Lord to builde an altar for burnt offering, or for meate offering, or for sacrifice, saue the altar of the Lord our God, that is before his Tabernacle.
“Sizingatheke konse kuti ife lero nʼkupandukira Yehova. Ife sitingapatuke kuleka kumutsata Yehova ndi kumanga guwa lina la nsembe zopsereza, nsembe za zakudya, ndi nsembe zina zopikisana ndi guwa la Yehova, Mulungu wathu limene lili patsogolo pa Hema ya Yehova mʼmene amakhalamo.”
30 And when Phinehas the Priest, and the princes of the Congregation and heads ouer the thousands of Israel which were with him, heard the wordes, that the children of Reuben, and children of Gad, and the children of Manasseh spake, they were well content.
Tsono Finehasi wansembe ndi atsogoleri a gululo amene anali naye atamva zimene anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka lakummawa la fuko la Manase ananena, anakondwera kwambiri.
31 And Phinehas the sonne of Eleazar the Priest said vnto the children of Reuben and to the children of Gad, and to the children of Manasseh, This day we perceiue, that the Lord is among vs, because ye haue not done this trespasse against the Lord: nowe ye haue deliuered the children of Israel out of the hand of the Lord.
Ndipo Finehasi wansembe, mwana wa Eliezara anati kwa mafuko a Rubeni, Gadi ndi Manase, “Lero tadziwa kuti Yehova ali nafe chifukwa zimene mwachitazi simunawukire nazo Yehova. Inu mwapulumutsa Aisraeli onse ku chilango cha Yehova.”
32 Then Phinehas the sonne of Eleazar the Priest with the princes returned from the children of Reuben, and from the children of Gad, out of the land of Gilead, vnto the land of Canaan, to the children of Israel, and brought them answere.
Ndipo Finehasi mwana wa wansembe Eliezara, pamodzi ndi atsogoleriwo anachoka ku Giliyadi nasiya anthu a fuko la Rubeni ndi Gadi nabwerera ku Kanaani kwa Aisraeli anzawo, ndipo anakafotokoza zonsezi.
33 And the saying pleased the children of Israel: and the children of Israel blessed God, and minded not to goe against them in battell, for to destroy the land, wherein the children of Reuben, and Gad dwelt.
Mawu amenewa anakondweretsa Aisraeli onse ndipo anayamika Mulungu. Choncho sanakambenso zopita ku nkhondo kukawononga dziko limene Arubeni ndi Agadi ankakhalamo.
34 Then the children of Reuben, and the children of Gad called the altar Ed: for it shall be a witnesse betweene vs, that the Lord is God.
Arubeni ndi Agadi anatcha guwalo kuti Mboni: Mboni pakati pathu kuti Yehova ndi Mulungu.

< Joshua 22 >