< Joshua 18 >

1 And the whole Congregation of the children of Israel, came together at Shiloh: for they set vp the Tabernacle of the Congregation there, after the land was subiect vnto them.
Atagonjetsa dziko lonse Aisraeli anasonkhana ku Silo ndipo anayimikako tenti ya msonkhano.
2 Nowe there remained among the children of Israel seuen tribes, to whom they had not deuided their inheritance.
Koma pa nthawiyo nʼkuti mafuko asanu ndi awiri a Aisraeli asanalandire cholowa chawo.
3 Therefore Ioshua said vnto the children of Israel, Howe long are ye so slacke to enter and possesse the land which the Lord God of your fathers hath giuen you?
Ndipo Yoswa anati kwa Aisraeli, “Kodi mudikira mpaka liti kuti mulowe ndi kulanda dziko limene Yehova Mulungu wa makolo anu wakupatsani?
4 Giue from among you for euery tribe three men, that I may sende them, and that they may rise, and walke through the land, and distribute it according to their inheritance, and returne to me.
Sankhani amuna atatu kuchokera ku fuko lililonse ndipo ine ndidzawatuma kuti akayendere dzikolo ndi kukalilembera bwino kuti ndiligawe kukhala lawo. Akatero, abwererenso kwa ine.
5 And that they may deuide it vnto them into seuen parts, (Iudah shall abide in his coast at the South, and the house of Ioseph shall stand in their coastes at the North)
Aligawe dzikolo mʼzigawo zisanu ndi ziwiri; fuko la Yuda lidzakhale ndi dziko lake la kummwera ndi nyumba ya Yosefe ikhalebe mʼdziko lawo la kumpoto.
6 Ye shall describe the land therefore into seuen partes, and shall bring them hither to me, and I will cast lottes for you here before the Lord our God.
Mudzalembe mawu ofotokoza za zigawo zisanu ndi ziwiri za dzikolo, ndi kubwera nawo kwa ine. Tsono ineyo ndidzakuchitirani maere pamaso pa Yehova Mulungu wanu.
7 But the Leuites shall haue no part among you: for the Priesthood of the Lord is their inheritance: also Gad and Reuben and halfe the tribe of Manasseh haue receiued their inheritance beyond Iorden Eastward, which Moses the seruant of the Lord gaue them.
Alevi asakhale ndi dziko pakati panu, chifukwa gawo lawo ndi kutumikira Yehova pa ntchito ya unsembe. Ndipo Gadi, Rubeni ndi theka la fuko la Manase analandira kale cholowa chawo kummawa kwa Yorodani. Mose mtumiki wa Yehova ndiye anawapatsa.”
8 Then the men arose, and went their way: and Ioshua charged them that went to describe the land, saying, Depart, and goe through the land, and describe it, and returne to me, that I may here cast lottes for you before the Lord in Shiloh.
Anthuwo akupita kukalembera dzikolo, Yoswa anawalangiza kuti, “Pitani mukayendere ndi kulembera dzikolo. Kenaka mukabwere kwa ine, ndidzakuchitirani maere kuno ku Silo pamaso pa Yehova.”
9 So the men departed, and passed through the lande, and described it by cities into seuen partes in a booke, and returned to Ioshua into the campe at Shiloh.
Ndipo anthu anachoka ndi kukayendera dziko lonse. Iwo analemba bwinobwino mʼbuku za dzikolo, mzinda ndi mzinda. Analigawa magawo asanu ndi awiri, ndipo anabwerera kwa Yoswa ku misasa ya ku Silo.
10 Then Ioshua cast lottes for them in Shiloh before the Lord, and there Ioshua deuided the land vnto the children of Israel, according to their portions:
Pambuyo pake Yoswa anawachitira maere ku Silo pamaso pa Yehova, ndipo fuko lililonse la Israeli analigawira dziko lake.
11 And the lot of the tribe of the children of Beniamin came foorth according to their families, and the cost of their lot lay betweene the children of Iudah, and the children of Ioseph.
Maere anagwera mabanja a fuko la Benjamini. Dziko limene anapatsidwa linali pakati pa fuko la Yuda ndi fuko la Yosefe:
12 And their coast on the Northside was from Iorden, and the border went vp to the side of Iericho on the Northpart, and went vp through the mountaines Westward, and the endes thereof are in the wildernesse of Beth-auen:
Mbali ya kumpoto malire awo anayambira ku Yorodani nalowera chakumpoto kwa matsitso a ku Yeriko kulowera cha kumadzulo kwa dziko la ku mapiri ndi kukafika ku chipululu cha Beti-Aveni.
13 And this border goeth along from thence to Luz, euen to the Southside of Luz (the same is Beth-el) and this border descendeth to Atroth-addar, neere the mount, that lyeth on the Southside of Beth-horon the nether.
Kuchokera kumeneko malirewo analoza ku Luzi nadutsa mʼmbali mwa mapiri kummwera kwa Luzi (ndiye Beteli) ndipo anatsika mpaka ku Ataroti Adari, ku mapiri a kummwera kwa Beti-Horoni wa Kumunsi.
14 So the border turneth, and compasseth the corner of the Sea Southward, from the mount that lyeth before Beth-horon Southward: and the endes thereof are at Kiriath-baal (which is Kiriath-iearim) a citie of the children of Iudah: this is the Westquarter.
Ndipo malirewo analowanso kwina, analunjika kummwera kuchokera kumadzulo kwake kwa phiri loyangʼanana ndi Beti-Horoni, mpaka ku mzinda wa Kiriyati Baala (ndiye Kiriati Yearimu), mzinda wa anthu a fuko la Yuda. Amenewa ndiye anali malire a mbali ya kumadzulo.
15 And the Southquarter is from the ende of Kiriath-iearim, and this border goeth out Westward, and commeth to the fountaine of waters of Nephtoah.
Malire a kummwera anayambira mʼmphepete mwenimweni mwa Kiriati Yearimu napita kumadzulo mpaka kukafika ku akasupe a Nefitowa.
16 And this border descendeth at the ende of the mountaine, that lyeth before the valley of Ben-hinnom, which is in the valley of the gyants Northward, and descendeth into the valley of Hinnom by the side of Iebusi Southwarde, and goeth downe to En-rogel,
Malire anatsikira mʼmphepete mwa phiri loyangʼanana ndi chigwa cha Beni Hinomu, kumpoto kwa chigwa cha Refaimu. Anapitirira kutsikira ku chigwa cha Hinomu kummwera kwa chitunda cha Ayebusi mpaka ku Eni Rogeli.
17 And compasseth from the North, and goeth foorth to En-shemesh, and stretcheth to Geliloth, which is toward the going vp vnto Adummim, and goeth downe to the stone of Bohan the sonne of Reuben.
Kenaka anakhotera kumpoto kupita ku Eni-Semesi, kupitirira mpaka ku Geliloti amene amayangʼanana ndi pokwera pa Adumimu. Kenaka malire anatsikira ku Mwala wa Bohani, mwana wa Rubeni.
18 So it goeth along to the side ouer against the plaine Northward, and goeth downe into the plaine.
Anabzola cha kumpoto kwa chitunda cha Beti Araba ndi kutsikabe mpaka ku chigwa cha Yorodani.
19 After, this border goeth along to the side of Beth-hoglah Northward: and the endes thereof, that is, of the border, reach to the point of the salt Sea Northward, and to the ende of Iorden Southward: this is the Southcoast.
Anabzolanso cha kumpoto kwa chitunda cha Beti-Hogila kukafika cha kumpoto ku gombe la Nyanja ya Mchere kumene mtsinje wa Yorodani umathirirako, cha kummwera kwenikweni. Awa anali malire a kummwera.
20 Also Iorden is the border of it on the Eastside: this is the inheritance of the children of Beniamin by the coastes thereof rounde about according to their families.
Yorodani ndiye anali malire a mbali ya kummawa. Awa anali malire a dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira.
21 Nowe the cities of the tribe of the children of Beniamin according to their families, are Iericho, and Beth-hoglah, and the valley of Keziz,
Mabanja a fuko la Benjamini anali ndi mizinda iyi; Yeriko, Beti-Hogila, Emeki Kezizi,
22 And Beth-arabah, and Zemaraim, and Beth-el,
Beti-Araba, Zemaraimu, Beteli
23 And Auim, and Parah, and Ophrah,
Avimu, Para, Ofiri,
24 And Chephar, Ammonai, and Ophni, and Gaba: twelue cities with their villages.
Kefari-Amoni, Ofini ndi Geba, mizinda khumi ndi awiri ndi midzi yake
25 Gibeon, and Ramah, and Beeroth,
Panalinso Gibiyoni, Rama, Beeroti,
26 And Mizpeh, and Chephirah, and Mozah,
Mizipa, Kefira, Moza
27 And Rekem, and Irpeel, and Taralah,
Rekemu, Iripeeli, Tarala,
28 And Zela, Eleph, and Iebusi, (which is Ierusalem) Gibeath, and Kiriath: fourteene cities with their villages: this is the inheritance of the children of Beniamin according to their families.
Zera Haelefu, mzinda wa Ayebusi (ndiye kuti Yerusalemu) Gibeya ndi Kiriati, mizinda 14 ndi midzi yake. Limeneli ndilo dziko limene mabanja a fuko la Benjamini analandira kuti likhale lawo.

< Joshua 18 >