< Jonah 1 >

1 The worde of the Lord came also vnto Ionah the sonne of Amittai, saying,
Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti,
2 Arise, and goe to Nineueh, that great citie, and crye against it: for their wickednesse is come vp before mee.
“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”
3 But Ionah rose vp to flee into Tarshish from the presence of the Lord, and went downe to Iapho: and he founde a ship going to Tarshish: so he payed the fare thereof, and went downe into it, that he might go with them vnto Tarshish, from the presence of the Lord.
Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.
4 But the Lord sent out a great winde into the sea, and there was a mightie tempest in the sea, so that the ship was like to be broken.
Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.
5 Then the mariners were afraide, and cryed euery man vnto his God, and cast the wares that were in the ship, into the sea to lighten it of the: but Ionah was gone downe into the sides of the ship, and he lay downe, and was fast a sleepe.
Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato.
6 So the shipmaster came to him, and saide vnto him, What meanest thou, O sleeper? Arise, call vpon thy God, if so be that God wil thinke vpon vs, that we perish not.
Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”
7 And they saide euery one to his fellowe, Come, and let vs cast lottes, that we may know, for whose cause this euill is vpon vs. So they cast lottes, and the lot fell vpon Ionah.
Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.
8 Then said they vnto him, Tell vs for whose cause this euill is vpon vs? what is thine occupation? and whence commest thou? which is thy countrey? and of what people art thou?
Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”
9 And he answered them, I am an Ebrewe, and I feare the Lord God of heauen, which hath made the sea, and the dry lande.
Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”
10 Then were the men exceedingly afrayde, and said vnto him, Why hast thou done this? (for the men knewe, that he fled from the presence of the Lord, because he had tolde them)
Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).
11 Then saide they vnto him, What shall we doe vnto thee, that the sea may be calme vnto vs? (for the sea wrought and was troublous)
Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”
12 And he said vnto them, Take me, and cast me into the sea: so shall the sea be calme vnto you: for I knowe that for my sake this great tempest is vpon you.
Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”
13 Neuerthelesse, the men rowed to bring it to the lande, but they coulde not: for the sea wrought, and was troublous against them.
Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja
14 Wherefore they cryed vnto the Lord, and said, We beseech thee, O Lord, we beseech thee, let vs not perish for this mans life, and lay not vpon vs innocent blood: for thou, O Lord, hast done, as it pleased thee.
Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.”
15 So they tooke vp Ionah, and cast him into the sea, and the sea ceased from her raging.
Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata.
16 Then the men feared the Lord exceedingly, and offered a sacrifice vnto the Lord, and made vowes.
Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.
17 Nowe the Lord had prepared a great fish to swallowe vp Ionah: and Ionah was in the belly of the fish three dayes, and three nightes.
Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.

< Jonah 1 >