< Jonah 4 >

1 Therefore it displeased Ionah exceedingly, and he was angry.
Koma Yona anakhumudwa kwambiri ndipo anakwiya.
2 And he prayed vnto the Lord, and saide, I pray thee, O Lord, was not this my saying, when I was yet in my countrey? therefore I preuented it to flee vnto Tarshish: for I knewe that thou art a gratious God, and merciful, slow to anger, and of great kindnes, and repentest thee of the euill.
Iye anapemphera kwa Yehova kuti, “Inu Yehova, kodi izi si zimene ndinanena ndikanali kwathu? Nʼchifukwa chaketu ine ndinafulumira kuthawa kupita ku Tarisisi. Ine ndinadziwa kuti ndinu Mulungu wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wa chikondi chopanda malire, Mulungu amene mumaleka kubweretsa tsoka.
3 Therefore nowe O Lord, take, I beseech thee, my life from me: for it is better for me to die then to liue.
Ndipo tsopano, Inu Yehova, ingondiphani basi, pakuti ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”
4 Then saide the Lord, Doest thou well to be angry?
Koma Yehova anayankha kuti, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye?”
5 So Ionah went out of the citie and sate on the East side of the citie, and there made him a boothe, and sate vnder it in the shadowe till he might see what should be done in the citie.
Yona anatuluka mu mzindamo nakakhala pansi cha kummawa kwa mzindawo. Kumeneko anadzimangira chithando nakhala mʼmenemo mu mthunzi, kudikira kuti aone zimene zichitikire mzindawo.
6 And the Lord God prepared a gourde, and made it to come vp ouer Ionah, that it might be a shadowe ouer his head and deliuer him from his griefe. So Ionah was exceeding glad of the gourde.
Tsono Yehova Mulungu anameretsa msatsi ndi kuyikulitsa kuti ipereke mthunzi kwa Yona kuchotsa mavuto ake; ndipo Yona anasangalala kwambiri chifukwa cha msatsiyo.
7 But God prepared a worme when the morning rose the next day, and it smote the gourd, that it withered.
Koma tsiku linalo mmawa, Mulungu anabweretsa mbozi imene inadya msatsiyo ndipo inafota.
8 And when the sunne did arise, God prepared also a feruent East winde: and the sunne beat vpon the head of Ionah, that he fainted, and wished in his heart to die, and said, It is better for me to dye, then to liue.
Dzuwa litatuluka, Yehova anabweretsa mphepo yotentha yochokera kummawa, ndipo dzuwa linatentha pamutu pa Yona kotero analenguka nalo. Iye anangofuna atafa, ndipo anati, “Ndi bwino kuti ndife kupambana nʼkukhala ndi moyo.”
9 And God said vnto Ionah, Doest thou well to be angrie for the gourde? And he said, I doe well to be angrie vnto the death.
Koma Mulungu anati kwa Yona, “Kodi nʼkoyenera kuti iwe ukwiye chifukwa cha msatsi?” Iye anayankha kuti, “Inde nʼkoyenera. Kukwiya kwanga nʼkofuna kufa nako.”
10 Then said the Lord, Thou hast had pitie on the gourde for the which thou hast not laboured, neither madest it growe, which came vp in a night, and perished in a night,
Koma Yehova anati, “Iwe ukumvera chisoni msatsiwo, ngakhale kuti sunawugwirire ntchito kapena kuwukulitsa. Inamera pa usiku umodzi ndipo inafanso pa usiku umodzi.
11 And shoulde not I spare Nineueh that great citie, wherein are sixe score thousande persons, that cannot discerne betweene their right hand, and their left hand, and also much cattell?
Koma mu Ninive muli anthu opitirira 120,000 amene sadziwa kusiyanitsa kuti chabwino nʼchiti ndipo choyipa nʼchiti, mulinso ziweto zochuluka. Kodi sindiyenera kumvera chisoni mzinda waukulu ngati uwu?”

< Jonah 4 >