< John 16 >
1 These thinges haue I saide vnto you, that ye should not be offended.
“Ine ndakuwuzani zonsezi kuti musadzakhumudwe.
2 They shall excommunicate you: yea, the time shall come, that whosoeuer killeth you, will thinke that he doeth God seruice.
Iwo adzakuchotsani mʼsunagoge mwawo. Kunena zoona, nthawi ikubwera imene aliyense amene adzakuphani adzaganiza kuti akutumikira Mulungu.
3 And these things will they doe vnto you, because they haue not knowen ye Father, nor me.
Iwo adzachita zoterozo chifukwa sanadziwe Atate kapena Inenso.
4 But these things haue I tolde you, that when the houre shall come, ye might remember, that I tolde you them. And these things said I not vnto you from ye beginning, because I was with you.
Ine ndakuwuzani izi kuti nthawi ikadzafika mudzakumbukire kuti Ine ndinakuchenjezani kale. Ine sindinakuwuzeni izi poyamba paja chifukwa ndinali nanu.”
5 But now I go my way to him that sent me, and none of you asketh me, Whither goest thou?
“Tsopano Ine ndikupita kwa Iye amene anandituma koma palibe wina mwa inu akundifunsa kuti, ‘Kodi mukupita kuti?’
6 But because I haue saide these thinges vnto you, your hearts are full of sorowe.
Muli ndi chisoni kwambiri chifukwa ndakuwuzani zimene.
7 Yet I tell you the trueth, It is expedient for you that I goe away: for if I goe not away, that Comforter will not come vnto you: but if I depart, I will send him vnto you.
Komatu ndakuwuzani zoona. Ine ndikuti kuli bwino kwa inu kuti ndichoke. Ngati sindichoka, Nkhosweyo sidzabwera kwa inu, koma ngati Ine ndipita, ndidzamutumiza kwa inu.
8 And when he is come, he will reproue the worlde of sinne, and of righteousnesse, and of iudgement.
Iye akabwera, adzatsutsa dziko lapansi za uchimo, zachilungamo ndi zachiweruzo.
9 Of sinne, because they beleeued not in me:
Za uchimo, chifukwa anthu sakhulupirira Ine.
10 Of righteousnesse, because I goe to my Father, and ye shall see me no more:
Za chilungamo, chifukwa Ine ndi kupita kwa Atate, kumene simudzandionanso.
11 Of iudgement, because the prince of this world is iudged.
Za chiweruzo, chifukwa wolamulira dziko lino lapansi waweruzidwa tsopano.
12 I haue yet many things to say vnto you, but ye cannot beare them nowe.
“Ine ndili ndi zambiri zoti ndiyankhule nanu, koma simungathe kuzilandira tsopano.
13 Howbeit, when he is come which is the Spirit of trueth, he will leade you into all trueth: for he shall not speake of himselfe, but whatsoeuer he shall heare, shall he speake, and he will shew you the things to come.
Koma pamene Iye, Mzimu wachoonadi, abwera, adzakutsogolerani mʼchoonadi chonse. Iye sadzayankhula mwa Iye yekha, adzayankhula zokhazo zimene wamva ndipo Iye adzakuwuzani zimene zikubwera.
14 He shall glorifie me: for he shall receiue of mine, and shall shewe it vnto you.
Iye adzalemekeza Ine chifukwa adzatenga za Ine nadzakudziwitsani.
15 All thinges that the Father hath, are mine: therefore said I, that he shall take of mine, and shewe it vnto you.
Zonse za Atate ndi zanga. Ichi nʼchifukwa chake Ine ndanena kuti Mzimu Woyera adzatenga kwa Ine zanga kuti muzidziwe.”
16 A litle while, and ye shall not see me: and againe a litle while, and ye shall see me: for I goe to the Father.
Yesu anapitiriza kuyankhula kuti, “Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso, ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso.”
17 Then said some of his disciples among them selues, What is this that he saieth vnto vs, A litle while, and ye shall not see me, and againe, a litle while, and ye shall see me, and, For I goe to the Father.
Ena a ophunzira ake anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi Iye akutanthauza chiyani ponena kuti, ‘Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso,’ ndi ‘ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso,’ ndiponso ‘chifukwa ndikupita kwa Atate?’”
18 They said therefore, What is this that he saith, A litle while? we know not what he sayeth.
Iwo anapitiriza kufunsana kuti, “Kodi akutanthauza chiyani, ‘kanthawi kochepa?’ Ife sitikumvetsetsa chimene Iye akuyankhula.”
19 Now Iesus knew that they would aske him, and said vnto them, Doe ye enquire among your selues, of that I said, A litle while, and ye shall not see me: and againe, a litle while, and yee shall see me?
Yesu anadziwa kuti ankafuna kuti amufunse za zimenezi, choncho anawafunsa kuti, “Kodi mukufunsana wina ndi mnzake chimene Ine ndimatanthauza pamene ndinati, ‘Mwa kanthawi kochepa simudzandionanso,’ ndi ‘patatha nthawi pangʼono mudzandionanso?’
20 Verely, verely I say vnto you, that ye shall weepe and lament, and the worlde shall reioyce: and ye shall sorowe, but your sorowe shalbe turned to ioye.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti inu mudzalira ndi kubuma pomwe dziko lapansi lidzakhale likukondwera. Inu mudzamva chisoni, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.
21 A woman when she traueileth, hath sorowe, because her houre is come: but assoone as she is deliuered of the childe, she remembreth no more the anguish, for ioy that a man is borne into the world.
Mayi akamabereka mwana amamva ululu chifukwa nthawi yake yafika; koma mwana wake akabadwa amayiwala ululu wake chifukwa cha chimwemwe chake chakuti mwana wabadwa mʼdziko lapansi.
22 And ye nowe therefore are in sorowe: but I will see you againe, and your hearts shall reioyce, and your ioy shall no man take from you.
Chimodzimodzinso ndi inu. Tsopano ino ndi nthawi yanu yomva chisoni, koma Ine ndidzakuonaninso ndipo inu mudzasangalala, ndipo palibe amene adzachotsa chimwemwe chanu.
23 And in that day shall ye aske me nothing. Verely, verely I say vnto you, whatsoeuer ye shall aske the Father in my Name, he will giue it you.
Tsiku limenelo inu simudzandipemphanso kalikonse. Ine ndikukuwuzani zoona kuti Atate anga adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
24 Hitherto haue ye asked nothing in my Name: aske, and ye shall receiue, that your ioye may be full.
Mpaka tsopano simunapemphe kalikonse mʼdzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
25 These things haue I spoken vnto you in parables: but the time will come, when I shall no more speake to you in parables: but I shall shew you plainely of the Father.
“Ngakhale ndakhala ndikuyankhula mʼmafanizo, nthawi ikubwera imene Ine sindidzagwiritsanso ntchito mafanizo otere koma ndidzakuwuzani momveka za Atate anga.
26 At that day shall ye aske in my Name, and I say not vnto you, that I will pray vnto the Father for you:
Tsiku limenelo inu mudzapempha mʼdzina langa. Ine sindikunena kuti ndidzapempha Atate mʼmalo mwanu ayi.
27 For the Father himselfe loueth you, because ye haue loued me, and haue beleeued that I came out from God.
Atate mwini anakukondani chifukwa inu mwandikonda Ine ndipo mwakhulupirira kuti Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate.
28 I am come out from the Father, and came into the worlde: againe I leaue the worlde, and goe to the Father.
Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate ndi kulowa mʼdziko lapansi. Tsopano ndikulisiya dziko lapansi kubwerera kwa Atate.”
29 His disciples saide vnto him, Loe, nowe speakest thou plainely, and thou speakest no parable.
Kenaka ophunzira ake anati, “Tsopano mukuyankhula momveka bwino ndi mopanda mafanizo.
30 Nowe knowe wee that thou knowest all things, and needest not that any man should aske thee. By this we beleeue, that thou art come out from God.
Tsopano ife tikuona kuti Inu mumadziwa zinthu zonse ndi kuti sipafunika wina aliyense kukufunsani. Mwa ichi ife takhulupirira kuti Inu munachokera kwa Mulungu.”
31 Iesus answered them, Doe you beleeue nowe?
Yesu anawafunsa kuti, “Kodi tsopano mwakhulupirira?”
32 Beholde, the houre commeth, and is already come, that ye shalbe scattered euery man into his owne, and shall leaue me alone: but I am not alone: for the Father is with me.
Koma nthawi ikubwera ndipo yafika, pamene inu mudzabalalitsidwa, aliyense ku nyumba yake. Inu mudzandisiya ndekhandekha. Koma Ine sindili ndekha, pakuti Atate anga ali nane.
33 These thinges haue I spoken vnto you, that in me ye might haue peace: in the world ye shall haue affliction, but be of good comfort: I haue ouercome the world.
“Ine ndakuwuzani izi kuti mwa Ine mukhale nawo mtendere. Mʼdziko lapansi mudzakhala nawo mavuto. Koma limbikani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko lapansi.”