< Joel 3 >

1 For beholde, in those dayes and in that time, when I shall bring againe the captiuitie of Iudah and Ierusalem,
“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
2 I will also gather all nations, and wil bring them downe into the valley of Iehoshaphat, and will pleade with them there for my people, and for mine heritage Israel, whom they haue scattered among the nations, and parted my land.
ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
3 And they haue cast lottes for my people, and haue giuen the childe for the harlot, and sold the girle for wine, that they might drinke.
Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
4 Yea, and what haue you to do with me, O Tyrus and Zidon and all the costes of Palestina? will ye render me a recompence? and if ye recompence mee, swiftly and speedily will I render your recompence vpon your head:
“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
5 For ye haue taken my siluer and my golde, and haue caried into your temples my goodly and pleasant things.
Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
6 The children also of Iudah and the children of Ierusalem haue you solde vnto the Grecians, that ye might send them farre from their border.
Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
7 Beholde, I will rayse them out of the place where ye haue sold them, and will render your reward vpon your owne head,
“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
8 And I will send your sonnes and your daughters into the hande of the children of Iudah, and they shall sell them to the Sabeans, to a people farre off: for the Lord hath spoken it.
Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
9 Publish this among the Gentiles: prepare warre, wake vp the mightie men: let all the men of warre drawe neere and come vp.
Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
10 Breake your plowshares into swords, and your sithes into speares: let the weake say, I am strong.
Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
11 Assemble your selues, and come all yee heathen and gather your selues together round about: there shall the Lord cast downe the mightie men.
Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
12 Let the heathen be wakened, and come vp to the valley of Iehoshaphat: for there will I sit to iudge all the heathen round about.
“Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
13 Put in your sithes, for the haruest is ripe: come, get you downe, for the winepresse is full: yea, the winepresses runne ouer, for their wickednesse is great.
Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
14 O multitude, O multitude, come into the valley of threshing: for the day of the Lord is neere in the valley of threshing.
Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
15 The sunne and moone shalbe darkened, and the starres shall withdrawe their light.
Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
16 The Lord also shall roare out of Zion, and vtter his voyce from Ierusalem, and the heauens and the earth shall shake, but the Lord wil be the hope of his people, and the strength of the children of Israel.
Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
17 So shall ye know that I am the Lord your God dwelling in Zion, mine holy Mountaine: then shall Ierusalem bee holy, and there shall no strangers go thorowe her any more.
“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
18 And in that day shall the mountaines drop downe newe wine, and the hilles shall flowe with milke, and al the riuers of Iudah shall runne with waters, and a fountaine shall come forth of the House of the Lord, and shall water the valley of Shittim.
“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
19 Egypt shalbe waste, and Edom shall be a desolate wildernesse, for the iniuries of the childre of Iudah, because they haue shed innocent blood in their land.
Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
20 But Iudah shall dwell for euer, and Ierusalem from generation to generation.
Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
21 For I will clense their blood, that I haue not clensed, and the Lord will dwell in Zion.
Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”

< Joel 3 >