< Joel 1 >

1 The worde of the Lord that came to Ioel the sonne of Pethuel.
Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.
2 Heare ye this, O Elders, and hearken ye all inhabitantes of the land, whether such a thing hath bene in your dayes, or yet in the dayes of your fathers.
Inu akuluakulu, imvani izi; mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko. Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu, kapena mʼnthawi ya makolo anu?
3 Tell you your children of it, and let your children shew to their children, and their children to another generation.
Muwafotokozere ana anu, ndipo ana anuwo afotokozere ana awo, ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
4 That which is left of ye palmer worme, hath the grashopper eaten, and the residue of ye grashopper hath the canker worme eaten, and the residue of the canker worme hath the caterpiller eaten.
Chimene dzombe losamera mapiko lasiya dzombe lowuluka ladya; chimene dzombe lowuluka lasiya dzombe lalingʼono ladya; chimene dzombe lalingʼono lasiya chilimamine wadya.
5 Awake ye drunkards, and weepe, and howle all ye drinkers of wine, because of the newe wine: for it shalbe pulled from your mouth.
Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire! Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo; lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano, pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
6 Yea, a nation commeth vpon my lande, mightie, and without nomber, whose teeth are like the teeth of a lyon, and he hath the iawes of a great lyon.
Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa, wamphamvu ndi wosawerengeka; uli ndi mano a mkango, zibwano za mkango waukazi.
7 He maketh my vine waste, and pilleth off the barke of my figge tree: he maketh it bare, and casteth it downe: ye branches therof are made white.
Wawononga mphesa zanga ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu. Wakungunula makungwa ake ndi kuwataya, kusiya nthambi zake zili mbee.
8 Mourne like a virgine girded with sackcloth for the husband of her youth.
Lirani ngati namwali wovala chiguduli, chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
9 The meate offring, and the drinke offring is cut off from the House of the Lord: the Priests the Lords ministers mourne.
Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova. Ansembe akulira, amene amatumikira pamaso pa Yehova.
10 The fielde is wasted: the lande mourneth: for the corne is destroyed: the new wine is dried vp, and the oyle is decayed.
Minda yaguga, nthaka yauma; tirigu wawonongeka, vinyo watsopano watha, mitengo ya mafuta yauma.
11 Be ye ashamed, O husband men: howle, O ye vine dressers for the wheate, and for the barly, because the haruest of the fielde is perished.
Khalani ndi nkhawa, inu alimi, lirani mofuwula inu alimi a mphesa; imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele, pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
12 The vine is dried vp, and the figge tree is decayed: the pomegranate tree and the palme tree, and the apple tree, euen all the trees of the fielde are withered: surely the ioy is withered away from the sonnes of men.
Mpesa wauma ndipo mtengo wamkuyu wafota; makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi, mitengo yonse ya mʼmunda yauma. Ndithudi chimwemwe cha anthu chatheratu.
13 Girde your selues and lament, ye Priests: howle ye ministers of the altar: come, and lie all night in sackecloth, ye ministers of my God: for the meate offring, and the drinke offring is taken away from the house of your God.
Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani; lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe. Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse, inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga; pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
14 Sanctifie you a fast: call a solemne assemblie: gather the Elders, and all the inhabitants of the land into the House of the Lord your God, and cry vnto the Lord,
Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya, itanani msonkhano wopatulika. Sonkhanitsani akuluakulu ndi anthu onse okhala mʼdziko ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu ndipo alirire Yehova.
15 Alas: for the day, for the day of the Lord is at hand, and it commeth as a destruction from the Almightie.
Kalanga ine tsikulo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira; lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.
16 Is not the meate cut off before our eyes? and ioy, and gladnesse from the house of our God?
Kodi chakudya chathu sichachotsedwa ife tikuona? Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
17 The seede is rotten vnder their cloddes: the garners are destroyed: the barnes are broken downe, for the corne is withered.
Mbewu zikunyala poti pansi ndi powuma. Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka; nkhokwe zapasuka popeza tirigu wauma.
18 How did the beasts mourne! the herdes of cattel pine away, because they haue no pasture, and the flockes of sheepe are destroyed.
Taonani mmene zikulirira ziweto; ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku chifukwa zilibe msipu; ngakhalenso nkhosa zikusauka.
19 O Lord, to thee will I crie: for the fire hath deuoured the pastures of the wildernesse, and the flame hath burnt vp all the trees of the fielde.
Kwa Inu Yehova ndilirira, pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo, malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
20 The beasts of the fielde cry also vnto thee: for the riuers of waters are dried vp, and the fire hath deuoured the pastures of the wildernes.
Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu; timitsinje tonse taphwa ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

< Joel 1 >