< Job 42 >
1 Then Iob answered the Lord, and sayd,
Pamenepo Yobu anayankha Yehova kuti,
2 I knowe that thou canst doe all things, and that there is no thought hidde from thee.
“Ndikudziwa kuti Inu mungathe kuchita zinthu zonse; chimene mufuna kuchita wina sangaletse konse.
3 Who is hee that hideth counsell without knowledge? therefore haue I spoken that I vnderstood not, euen things too wonderfull for me, and which I knew not.
Munandifunsa kuti, ‘Kodi ndiwe yani amene ukufuna kusokoneza uphungu wanga ndi mawu opanda nzeru? Zoonadi ndinayankhula zimene sindinazimvetse, zinthu zodabwitsa kwambiri kwa ine zimene sindinazidziwe.
4 Heare, I beseech thee, and I will speake: I will demaunde of thee, and declare thou vnto me.
“Inu munandiwuza kuti, ‘Mvetsetsa tsopano ndipo ndidzayankhula; ndidzakufunsa ndipo iwe udzandiyankhe.’
5 I haue heard of thee by the hearing of the eare, but now mine eye seeth thee.
Ndinkangomva za Inu ndi makutu anga, koma tsopanonso ndakuonani ndi maso anga.
6 Therefore I abhorre my selfe, and repent in dust and ashes.
Nʼchifukwa chake ndi kuchita manyazi, ndikulapa podzithira fumbi ndi phulusa.”
7 Now after that the Lord had spoken these wordes vnto Iob, ye Lord also said vnto Eliphaz ye Temanite, My wrath is kindled against thee, and against thy two friends: for yee haue not spoken of me the thing that is right, like my seruant Iob.
Yehova atayankhula ndi Yobu mawu amenewa anawuza Elifazi wa ku Temani kuti, “Ine ndakukwiyira pamodzi ndi abwenzi ako awiri, chifukwa simunayankhule zabwino za Ine, monga mmene wayankhulira mtumiki wanga Yobu.
8 Therefore take vnto you nowe seuen bullockes, and seuen rammes, and go to my seruant Iob, and offer vp for your selues a burnt offring, and my seruant Iob shall pray for you: for I wil accept him, least I should put you to shame, because ye haue not spoken of me the thing, which is right, like my seruant Iob.
Kotero tsopano mutenge ngʼombe zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi nkhosa zazimuna zisanu ndi ziwiri ndi kupita nazo kwa mtumiki wanga Yobu kuti mukapereke nsembe zopsereza. Mtumiki wanga Yobu adzakupemphererani, ndipo Ine ndidzalandira pemphero lake. Sindidzakuchitirani kanthu molingana ndi uchitsiru wanu. Inu simunayankhule zabwino za Ine, monga anayankhulira Yobu mtumiki wanga.”
9 So Eliphaz the Temanite, and Bildad the Shuhite, and Zophar the Naamathite went, and did according as the Lord had saide vnto them, and the Lord accepted Iob.
Motero Elifazi wa ku Temani, Bilidadi wa ku Suki ndi Zofari wa ku Naama anachita zimene Yehova anawawuza ndipo Yehova anamvera pemphero la Yobu.
10 Then the Lord turned the captiuitie of Iob, when he prayed for his friends: also the Lord gaue Iob twise so much as he had before.
Yobu atawapempherera abwenzi ake aja, Yehova anamubwezera chuma chake ndipo anamupatsa mowirikiza kuposa zomwe anali nazo kale.
11 Then came vnto him all his brethren, and all his sisters, and all they that had bene of his acquaintance before, and did eate bread with him in his house, and had compassion of him, and comforted him for al the euil, that the Lord had brought vpon him, and euery man gaue him a piece of money, and euery one an earing of golde.
Abale ake ndi alongo ake onse, kuphatikizapo onse amene ankamudziwa kale, amabwera kwa iye nʼkudzadya naye chakudya mʼnyumba mwake. Iwo anamutonthoza ndi kumupepesa chifukwa cha mavuto onse amene Yehova analola kuti amugwere. Aliyense wa iwowa anamupatsa ndalama ndi mphete yagolide.
12 So the Lord blessed the last dayes of Iob more then the first: for he had foureteene thousand sheepe, and sixe thousand camels, and a thousand yoke of oxen, and a thousand shee asses.
Yehova anadalitsa Yobu pa masiku ake otsirizawa kupambana poyamba paja. Iye anali ndi nkhosa 14,000, ngamira 6,000, ngʼombe zantchito 2,000 ndi abulu aakazi 1,000.
13 He had also seue sonnes, and three daughters.
Anaberekanso ana aamuna asanu ndi awiri ndi ana aakazi atatu.
14 And he called the name of one Iemimah, and the name of the seconde Keziah, and the name of the third Keren-happuch.
Mwana wake wamkazi woyamba anamutcha Yemima, wachiwiri anamutcha Keziya, wachitatu anamutcha Kereni Hapuki.
15 In all the lande were no women found so faire as the daughters of Iob, and their father gaue them inheritaunce among their brethren.
Mʼdziko monsemo munalibe akazi okongola ngati ana a Yobu, ndipo abambo awo anawapatsa cholowa pamodzi ndi alongo awo.
16 And after this liued Iob an hundreth and fourtie yeres, and sawe his sonnes, and his sonnes sonnes, euen foure generations.
Zitachitika zimenezi, Yobu anakhala ndi moyo zaka 140. Iye anaona zidzukulu zake mpaka mʼbado wachinayi.
17 So Iob dyed, being old, and full of dayes.
Potsiriza, Yobu anamwalira ali nkhalamba ya zaka zochuluka kwambiri.