< Job 37 >

1 At this also mine heart is astonied, and is mooued out of his place.
“Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Heare the sound of his voyce, and the noyse that goeth out of his mouth.
Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake, kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 He directeth it vnder the whole heauen, and his light vnto the endes of the world.
Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 After it a noyse soundeth: hee thundereth with the voyce of his maiestie, and hee will not stay them when his voyce is heard.
Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka. Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero. Pamene wabangula, palibe chimene amalephera kuchita.
5 God thundereth marueilously with his voyce: he worketh great things, which we know not.
Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 For he sayth to the snowe, Be thou vpon the earth: likewise to the small rayne and to the great rayne of his power.
Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’ ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 With the force thereof he shutteth vp euery man, that all men may knowe his worke.
Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake. Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 Then the beastes go into the denne, and remaine in their places.
Zirombo zimakabisala ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 The whirlewind commeth out of the South, and the colde from the North winde.
Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake, kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 At the breath of God the frost is giuen, and the breadth of the waters is made narrowe.
Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 He maketh also the cloudes to labour, to water the earth, and scattereth the cloude of his light.
Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula, amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 And it is turned about by his gouernment, that they may doe whatsoeuer he commandeth them vpon the whole worlde:
Mulungu amayendetsa mitamboyo mozungulirazungulira dziko lonse lapansi kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Whether it be for punishment, or for his lande, or of mercie, he causeth it to come.
Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu, kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 Hearken vnto this, O Iob: stand and consider the wonderous workes of God.
“Abambo Yobu, tamvani izi; imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Diddest thou knowe when God disposed them? and caused the light of his cloud to shine?
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Hast thou knowen the varietie of the cloude, and the wonderous workes of him, that is perfite in knowledge?
Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo, ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 Or howe thy clothes are warme, when he maketh the earth quiet through the South winde?
Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 Hast thou stretched out the heaues, which are strong, and as a molten glasse?
kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 Tell vs what we shall say vnto him: for we can not dispose our matter because of darknes.
“Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye; sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Shall it be told him when I speake? or shall man speake when he shalbe destroyed?
Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu? Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 And nowe men see not the light, which shineth in the cloudes, but the winde passeth and clenseth them.
Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa, ndi kunyezimira mlengalenga, kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 The brightnesse commeth out of the North: the praise thereof is to God, which is terrible.
Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto; Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 It is the Almightie: we can not finde him out: he is excellent in power and iudgement, and aboundant in iustice: he afflicteth not.
Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa; pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 Let men therefore feare him: for he will not regarde any that are wise in their owne conceit.
Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri, kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”

< Job 37 >