< Job 36 >
1 Elihu also proceeded and sayde,
Ndipo Elihu anapitirira kuyankhula nati:
2 Suffer me a litle, and I will instruct thee: for I haue yet to speake on Gods behalfe.
“Mundilole pangʼono pokha ndipo ndikuonetsani kuti zilipo zambiri zoti ziyankhulidwe mʼmalo mwa Mulungu.
3 I will fetche my knowledge afarre off, and will attribute righteousnes vnto my Maker.
Nzeru zanga ndimazitenga kutali; ndidzaonetsa kulungama kwa Mlengi wanga.
4 For truely my wordes shall not be false, and he that is perfect in knowledge, speaketh with thee.
Ndithudi mawu anga si abodza; wanzeru zangwiro ali ndi inu.
5 Behold, the mighty God casteth away none that is mighty and valiant of courage.
“Mulungu ndi wamphamvu, koma sanyoza anthu; Iye ndi wamphamvu, ndipo ndi wokhazikika pa cholinga chake.
6 He mainteineth not the wicked, but he giueth iudgement to the afflicted.
Salola oyipa kuti akhalebe ndi moyo koma amapereka ufulu kwa anthu osautsidwa.
7 He withdraweth not his eyes from the righteous, but they are with Kings in ye throne, where he placeth them for euer: thus they are exalted.
Iye saleka kuyangʼanira anthu olungama; amawayika kuti alamulire pamodzi ndi mafumu ndipo amawalemekeza mpaka muyaya.
8 And if they bee bound in fetters and tyed with the cordes of affliction,
Koma ngati anthu amangidwa ndi unyolo, ndipo akondwa ndi zingwe zamasautso,
9 Then will he shewe them their worke and their sinnes, because they haue bene proude.
Iye amawafotokozera zomwe anachita, kuti iwo anachimwa modzikuza.
10 He openeth also their eare to discipline, and commandeth them that they returne from iniquity.
Mulungu amawatsekula makutu kuti amve malangizo ake ndipo amawalamula kuti alape zoyipa zawo.
11 If they obey and serue him, they shall end their dayes in prosperity, and their yeres in pleasures.
Ngati iwo amumvera ndi kumutumikira, adzatsiriza masiku a moyo wawo mwamtendere, adzatsiriza zaka zawo mosangalala.
12 But if they wil not obey, they shall passe by the sworde, and perish without knowledge.
Koma ngati samvera, adzaphedwa ndi lupanga ndipo adzafa osadziwa kanthu.
13 But the hypocrites of heart increase the wrath: for they call not when he bindeth them.
“Anthu osapembedza amasunga mkwiyo mu mtima mwawo; akawalanga, safuwulira kwa Iye kupempha thandizo.
14 Their soule dyeth in youth, and their life among the whoremongers.
Amafa akanali achinyamata, pakati pa amuna achiwerewere a kumalo azipembedzo.
15 He deliuereth the poore in his affliction, and openeth their eare in trouble.
Koma ovutika, Iye amawapulumutsa pa mavuto awo; Mulungu amawayankhula mʼmasautso awowo.
16 Euen so woulde he haue taken thee out of the streight place into a broade place and not shut vp beneath: and that which resteth vpon thy table, had bene full of fat.
“Iye akukukopani inu kuti muchoke mʼmasautso, kuti mupite ku malo aakulu kumene kulibe chokutchingani, kumalo a mpumulo kumene kuli chakudya chabwino kwambiri.
17 But thou art ful of the iudgement of the wicked, though iudgement and equitie maintaine all things.
Koma tsopano inu mwapezeka wopalamula chifukwa cha kuyipa kwanu; chiweruzo ndi chilungamo chakugwerani.
18 For Gods wrath is, least hee should take that away in thine abundance: for no multitude of giftes can deliuer thee.
Muchenjere kuti wina asakukopeni ndi chuma; musalole kuti chiphuphu chachikulu chikusocheretseni.
19 Wil he regard thy riches? he regardeth not golde, nor all them that excel in strength.
Kodi chuma chanu kapena mphamvu zanu zonse zingakusungeni kotero kuti simungakhale pa masautso?
20 Be not carefull in the night, howe he destroyeth the people out of their place.
Musalakalake kuti usiku ubwere, pakuti ndiyo nthawi imene anthu adzawonongeka.
21 Take thou heede: looke not to iniquitie: for thou hast chosen it rather then affliction.
Muchenjere kuti musatembenukire ku uchimo, chifukwa uchimowo ndiwo unabweretsa kuzunzika kwanu.
22 Beholde, God exalteth by his power: what teacher is like him?
“Taonani, Mulungu ndi wamkulu ndiponso ndi wamphamvu. Kodi ndi mphunzitsi uti amene angafanane naye?
23 Who hath appointed to him his way? or who can say, Thou hast done wickedly?
Kodi ndani amene anamuwuzapo Mulungu zoti achite, kapena kumuwuza kuti, ‘Inu mwachita chinthu cholakwa?’
24 Remember that thou magnifie his worke, which men behold.
Kumbukirani kutamanda ntchito zake zimene anthu amaziyamika mʼnyimbo.
25 All men see it, and men beholde it afarre off.
Anthu onse amaziona ntchitozo; anthuwo amaziona ali kutali.
26 Beholde, God is excellent, and we knowe him not, neither can the nomber of his yeres bee searched out.
Ndithudi, Mulungu ndi wamkulu, sitimudziwa nʼpangʼono pomwe! Chiwerengero cha zaka zake nʼchosadziwika.
27 When he restraineth the droppes of water, the rayne powreth down by the vapour thereof,
“Mulungu ndiye amakweza timadontho tamadzi kuthambo, timene timasungunuka nʼkukhala mvula;
28 Which raine the cloudes do droppe and let fall abundantly vpon man.
mitambo imagwetsa mvulayo ndipo mvulayo imavumbwa pa anthu mokwanira.
29 Who can know the diuisions of ye clouds and the thunders of his tabernacle?
Kodi ndani amene angadziwe momwe mitambo imayendera, momwe Iye amabangulira kuchokera kumalo ake?
30 Beholde, he spreadeth his light vpon it, and couereth the bottome of the sea.
Taonani momwe amawalitsira zingʼaningʼani pa malo ake onse, zimafika ngakhale pansi pa nyanja.
31 For thereby hee iudgeth the people, and giueth meate abundantly.
Umu ndi mmene Iye amalamulira mitundu ya anthu ndi kuwapatsa chakudya chochuluka.
32 He couereth the light with the clouds, and commandeth them to go against it.
Amadzaza manja ake ndi zingʼaningʼani, ndipo amazilamulira kuti zigwe pamalo pamene Iye akufuna.
33 His companion sheweth him thereof, and there is anger in rising vp.
Mabingu ake amalengeza za kubwera kwa mvula yamkuntho; ngʼombe nazo zimalengeza za kubwera kwake.