< Job 29 >

1 So Iob proceeded and continued his parable, saying,
Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:
2 Oh that I were as in times past, when God preserued me!
“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi, masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
3 When his light shined vpon mine head: and when by his light I walked thorowe the darkenesse,
pamene nyale yake inkandiwunikira ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
4 As I was in the dayes of my youth: when Gods prouidence was vpon my tabernacle:
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri, pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
5 When the almightie was yet with me, and my children round about me.
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane, ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
6 When I washed my pathes with butter, and when the rocke powred me out riuers of oyle:
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka, ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.
7 When I went out to the gate, euen to the iudgement seat, and when I caused them to prepare my seate in the streete.
“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
8 The yong men saw me, and hid themselues, and the aged arose, and stood vp.
anyamata amati akandiona ankapatuka ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
9 The princes stayed talke, and layde their hand on their mouth.
atsogoleri ankakhala chete ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 The voyce of princes was hidde, and their tongue cleaued to the roofe of their mouth.
anthu otchuka ankangoti duu, ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 And when the eare heard me, it blessed me: and when the eye sawe me, it gaue witnesse to me.
Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga, ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 For I deliuered the poore that cryed, and the fatherlesse, and him that had none to helpe him.
chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo, ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 The blessing of him that was ready to perish, came vpon me, and I caused the widowes heart to reioyce.
Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa; ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 I put on iustice, and it couered me: my iudgement was as a robe, and a crowne.
Chilungamo chinali ngati chovala changa; chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 I was the eyes to the blinde, and I was the feete to the lame.
Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya; ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 I was a father vnto the poore, and when I knewe not the cause, I sought it out diligently.
Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi; ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 I brake also the chawes of the vnrighteous man, and pluckt the praye out of his teeth.
Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.
18 Then I sayde, I shall die in my nest, and I shall multiplie my dayes as the sand.
“Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga, masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 For my roote is spread out by the water, and the dewe shall lye vpon my branche.
Mizu yanga idzatambalalira ku madzi, ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 My glory shall renue towarde me, and my bowe shall be restored in mine hand.
Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine, ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’
21 Vnto me men gaue eare, and wayted, and helde their tongue at my counsell.
“Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi, ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 After my wordes they replied not, and my talke dropped vpon them.
Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso; mawu anga ankawagwira mtima.
23 And they wayted for me, as for the raine, and they opened their mouth as for the latter rayne.
Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 If I laughed on them, they beleeued it not: neither did they cause the light of my countenance to fall.
Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira; kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 I appoynted out their way, and did sit as chiefe, and dwelt as a King in the army, and like him that comforteth the mourners.
Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu; ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo; ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

< Job 29 >