< Job 23 >

1 Bvt Iob answered and sayd,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Though my talke be this day in bitternes, and my plague greater then my groning,
“Leronso kudandaula kwanga nʼkwakukulu kwambiri; Iye akundilanga kwambiri ngakhale ndi kubuwula.
3 Would God yet I knew how to finde him, I would enter vnto his place.
Ndikanangodziwa kumene ndikanamupeza Mulungu; ndikanangopita kumene amakhalako!
4 I would pleade the cause before him, and fill my mouth with arguments.
Ndikanafotokoza mlandu wanga pamaso pake ndipo ndikanayankhula mawu odziteteza.
5 I would knowe the wordes, that he would answere me, and would vnderstand what he would say vnto me.
Ndikanadziwa mawu amene Iye akanandiyankha, ndi kulingalira bwino zimene akananena!
6 Would he plead against me with his great power? No, but he would put strength in me.
Kodi Iye akanalimbana nane mwa mphamvu zake zazikulu? Ayi, Iye sakanayankhula zinthu zotsutsana nane.
7 There the righteous might reason with him, so I shoulde be deliuered for euer from my Iudge.
Kumeneko munthu wolungama akanafotokoza mlandu wake pamaso pake, ndipo woweruzayo akanandipeza wosalakwa nthawi zonse.
8 Behold, if I go to the East, he is not there: if to the West, yet I can not perceiue him:
“Taonani, ndikapita kummawa, Iye kulibe kumeneko, ndikapita kumadzulo sinditha kumupeza kumeneko.
9 If to the North where he worketh, yet I cannot see him: he wil hide himselfe in the South, and I cannot beholde him.
Akamagwira ntchito kumpoto, sindimuona kumeneko akapita kummwera, sindimuona.
10 But he knoweth my way, and trieth mee, and I shall come forth like the gold.
Koma Iye amadziwa mmene ndimayendera; Iyeyo akandiyesa adzandipeza kuti ndili ngati golide.
11 My foote hath followed his steps: his way haue I kept, and haue not declined.
Mapazi anga akhala akuponda mʼmapazi ake; ndasunga njira yake ndipo sindinayitaye.
12 Neyther haue I departed from the commandement of his lippes, and I haue esteemed the words of his mouth more then mine appointed foode.
Sindinapatuke kusiya malamulo ochokera pakamwa pake; ndasunga mawu a pakamwa pake kupambana chakudya changa cha tsiku ndi tsiku.
13 Yet he is in one minde, and who can turne him? yea, he doeth what his minde desireth.
“Koma Iyeyo ndi wosasinthika, ndipo ndani angatsutsane naye? Iye amachita chilichonse chimene wafuna.
14 For he will performe that, which is decreed of me, and many such things are with him.
Iye amachita chimene watsimikiza kuti chindichitikire, ndipo malingaliro oterowa ali nawobe.
15 Therefore I am troubled at his presence, and in considering it, I am afraid of him.
Nʼchifukwa chake ndikuchita mantha kwambiri pamaso pake; ndikamaganiza zonsezi ndimamuopa.
16 For God hath softened mine heart, and the Almightie hath troubled me.
Mulungu walefula mtima wanga; Wamphamvuzonse wandiopseza kwambiri.
17 For I am not cut off in darknesse, but he hath hid the darkenesse from my face.
Komatu sindinachititsidwe mantha ndi mdima, ndi mdima wandiweyani umene waphimba nkhope yanga.

< Job 23 >