< Job 20 >

1 Then answered Zophar the Naamathite and saide,
Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti
2 Doubtlesse my thoughts cause me to answere, and therefore I make haste.
“Kuvutika kwa mʼmaganizo kwanga kwandifulumiza kuti ndiyankhe chifukwa ndasautsidwa kwambiri.
3 I haue heard the correction of my reproch: therefore the spirite of mine vnderstanding causeth me to answere.
Ndikumva kudzudzula kondinyoza, ndipo kumvetsetsa kwanga kwa zinthu kwandifulumiza kuti ndiyankhe.
4 Knowest thou not this of olde? and since God placed man vpon the earth,
“Ndithudi iwe ukudziwa momwe zinthu zakhala zikuchitikira kuyambira kale, kuchoka nthawi imene munthu analengedwa pa dziko lapansi,
5 That the reioycing of the wicked is short, and that the ioy of hypocrites is but a moment?
kuti chisangalalo cha woyipa nʼchosachedwa kutha, chimwemwe cha wosapembedza Mulungu nʼchakanthawi kochepa.
6 Though his excellencie mount vp to the heauen, and his head reache vnto the cloudes,
Ngakhale atamayenda mapewa ake ali mmwamba ndipo mutu wake uli nengʼaa,
7 Yet shall hee perish for euer, like his dung, and they which haue seene him, shall say, Where is hee?
iye adzatheratu monga momwe imatayikira ndowe yake yomwe; iwo amene ankamuona adzati, ‘Kodi uje uja ali kuti?’
8 He shall flee away as a dreame, and they shall not finde him, and shall passe away as a vision of the night,
Adzazimirira ngati maloto ndipo sadzapezekanso, adzachotsedwa ngati masomphenya a usiku.
9 So that the eye which had seene him, shall do so no more, and his place shall see him no more.
Diso limene linamuona silidzamuonanso; sadzapezekanso pamalo pake.
10 His children shall flatter the poore, and his hands shall restore his substance.
Ana ake adzabwezera zonse zimene iyeyo analanda anthu osauka;
11 His bones are full of the sinne of his youth, and it shall lie downe with him in the dust.
Mphamvu zaunyamata zimene zili mʼthupi mwake zidzagona naye limodzi mʼfumbi.
12 When wickednesse was sweete in his mouth, and he hid it vnder his tongue,
“Ngakhale zoyipa zili zozuna mʼkamwa mwake ndipo amazibisa kunsi kwa lilime lake,
13 And fauoured it, and would not forsake it, but kept it close in his mouth,
ngakhale salola kuzilavula, ndipo amazisunga mʼkamwa mwake,
14 Then his meat in his bowels was turned: the gall of Aspes was in the middes of him.
koma chakudya chake chidzawawasa mʼmimba mwake; chidzasanduka ngati ndulu ya njoka mʼkati mwa iyeyo.
15 He hath deuoured substance, and hee shall vomit it: for God shall drawe it out of his bellie.
Adzachisanza chuma chimene anachimeza; Mulungu adzachitulutsa mʼmimba mwa munthuyo.
16 He shall sucke the gall of Aspes, and the vipers tongue shall slay him.
Iye adzayamwa ndulu ya njoka ndipo ululu wa mphiri udzamupha.
17 He shall not see the riuers, nor the floods and streames of honie and butter.
Sadzasangalala ndi timitsinje, mitsinje yoyenda uchi ndi mafuta.
18 He shall restore the labour, and shall deuoure no more: euen according to the substance shalbe his exchange, and he shall enioy it no more.
Ayenera kubweza zimene anazigwirira ntchito osazidya; sadzasangalala ndi phindu la malonda ake.
19 For he hath vndone many: he hath forsaken the poore, and hath spoyled houses which he builded not.
Pakuti iye anapondereza anthu osauka ndipo anawasiya wopanda thandizo; iyeyo analanda nyumba zimene sanamange.
20 Surely he shall feele no quietnes in his bodie, neither shall he reserue of that which he desired.
“Chifukwa choti umbombo wake sutha, sadzatha kusunga chilichonse chimene amakondwera nacho.
21 There shall none of his meate bee left: therefore none shall hope for his goods.
Palibe chatsala kuti iye adye; chuma chake sichidzachedwa kutha.
22 When he shalbe filled with his abundance, he shalbe in paine, and the hand of all the wicked shall assaile him.
Ngakhale ndi munthu wachuma, mavuto adzamugwera; mavuto aakulu adzamugwera.
23 He shall be about to fill his belly, but God shall sende vpon him his fierce wrath, and shall cause to rayne vpon him, euen vpon his meate.
Akadya nʼkukhuta, Mulungu adzamugwetsera ukali wamoto ngati mvula yosalekeza.
24 He shall flee from the yron weapons, and the bow of steele shall strike him through.
Ngakhale athawe mkondo wachitsulo, muvi wamkuwa wosongoka udzamulasa.
25 The arrowe is drawen out, and commeth forth of the body, and shineth of his gall, so feare commeth vpon him.
Muviwo adzawutulutsira ku msana, songa yake yowala kuchoka mʼmphafa mwake. Adzagwidwa ndi mantha aakulu;
26 All darkenes shalbe hid in his secret places: the fire that is not blowen, shall deuoure him, and that which remaineth in his tabernacle, shalbe destroyed.
mdima wandiweyani ukudikira chuma chake. Moto wopanda wowukoleza udzamupsereza ndi kuwononga zonse zotsala mʼnyumba yake.
27 The heauen shall declare his wickednes, and the earth shall rise vp against him.
Zamumlengalenga zidzawulula kulakwa kwake; dziko lapansi lidzamuwukira.
28 The increase of his house shall go away: it shall flow away in the day of his wrath.
Chigumula cha madzi chidzawononga nyumba yake, katundu wake adzatengedwa pa tsiku la ukali wa Mulungu.
29 This is the portion of the wicked man from God, and the heritage that he shall haue of God for his wordes.
Izi ndi zimene Mulungu amasungira anthu oyipa, mphotho imene Mulungu amayikira iwowo.”

< Job 20 >