< Job 13 >

1 Loe, mine eye hath seene all this: mine eare hath heard, and vnderstande it.
“Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
2 I knowe also as much as you knowe: I am not inferiour vnto you.
Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
3 But I will speake to the Almightie, and I desire to dispute with God.
Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
4 For in deede ye forge lyes, and all you are physitions of no value.
Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
5 Oh, that you woulde holde your tongue, that it might be imputed to you for wisedome!
Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
6 Nowe heare my disputation, and giue eare to the arguments of my lips.
Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
7 Will ye speake wickedly for Gods defence, and talke deceitfully for his cause?
Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
8 Will ye accept his person? or will ye contende for God?
Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
9 Is it well that he shoulde seeke of you? will you make a lye for him, as one lyeth for a man?
Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
10 He will surely reprooue you, if ye doe secretly accept any person.
Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
11 Shall not his excellencie make you afraid? and his feare fall vpon you?
Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
12 Your memories may be compared vnto ashes, and your bodyes to bodyes of clay.
Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
13 Holde your tongues in my presence, that I may speake, and let come vpon what will.
“Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
14 Wherefore doe I take my flesh in my teeth, and put my soule in mine hande?
Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
15 Loe, though he slay me, yet will I trust in him, and I will reprooue my wayes in his sight.
Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
16 He shalbe my saluation also: for the hypocrite shall not come before him.
Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
17 Heare diligently my wordes, and marke my talke.
Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
18 Beholde nowe: if I prepare me to iudgement, I knowe that I shalbe iustified.
Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
19 Who is he, that will pleade with me? for if I nowe holde my tongue, I dye.
Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
20 But doe not these two things vnto me: then will I not hide my selfe from thee.
“Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
21 Withdrawe thine hande from me, and let not thy feare make me afraide.
Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
22 Then call thou, and I will answere: or let me speake, and answere thou me.
Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
23 Howe many are mine iniquities and sinnes? shewe me my rebellion, and my sinne.
Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
24 Wherefore hidest thou thy face, and takest me for thine enemie?
Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
25 Wilt thou breake a leafe driuen to and from? and wilt thou pursue the drie stubble?
Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
26 For thou writest bitter things against me, and makest me to possesse the iniquities of my youth.
Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
27 Thou puttest my feete also in the stocks, and lookest narrowly vnto all my pathes, and makest the print thereof in ye heeles of my feet.
Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
28 Such one consumeth like a rotten thing, and as a garment that is motheaten.
“Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.

< Job 13 >