< Job 12 >
1 Then Iob answered, and sayde,
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 In deede because that ye are the people onely, wisedome must dye with you.
“Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
3 But I haue vnderstanding aswel as you, and am not inferior vnto you: yea, who knoweth not such things?
Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
4 I am as one mocked of his neighbour, who calleth vpon God, and he heareth him: the iust and the vpright is laughed to scorne.
“Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
5 Hee that is readie to fall, is as a lampe despised in the opinion of the riche.
Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
6 The tabernacles of robbers doe prosper, and they are in safetie, that prouoke God, whome God hath enriched with his hand.
Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
7 Aske now the beasts, and they shall teach thee, and the foules of the heauen, and they shall tell thee:
“Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
8 Or speake to the earth, and it shall shewe thee: or the fishes of the sea, and they shall declare vnto thee.
kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
9 Who is ignorant of all these, but that the hande of the Lord hath made these?
Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
10 In whose hande is the soule of euery liuing thing, and the breath of all mankinde.
Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
11 Doeth not the eares discerne the words? and the mouth taste meate for it selfe?
Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
12 Among the ancient is wisedome, and in the length of dayes is vnderstanding.
Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
13 With him is wisedome and strength: he hath counsell and vnderstanding.
“Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
14 Beholde, he will breake downe, and it can not be built: he shutteth a man vp, and he can not be loosed.
Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
15 Beholde, he withholdeth the waters, and they drie vp: but when he sendeth them out, they destroy the earth.
Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
16 With him is strength and wisedome: hee that is deceiued, and that deceiueth, are his.
Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
17 He causeth the counsellers to goe as spoyled, and maketh the iudges fooles.
Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
18 He looseth the collar of Kings, and girdeth their loynes with a girdle.
Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
19 He leadeth away the princes as a pray, and ouerthroweth the mightie.
Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
20 He taketh away the speach from the faithfull counsellers, and taketh away the iudgement of the ancient.
Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
21 He powreth contempt vpon princes, and maketh the strength of the mightie weake.
Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
22 He discouereth the deepe places from their darkenesse, and bringeth foorth the shadowe of death to light.
Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
23 He increaseth the people, and destroyeth them: he inlargeth the nations, and bringeth them in againe.
Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
24 He taketh away the heartes of the that are the chiefe ouer the people of the earth, and maketh them to wander in the wildernes out of the way.
Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
25 They grope in the darke without light: and he maketh the to stagger like a drunken man.
Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.