< Jeremiah 51 >

1 Thus sayth the Lord, Beholde, I wil raise vp against Babel, and against the inhabitants that lift vp their heart against me, a destroying wind,
Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
2 And wil send vnto Babel fanners that shall fanne her, and shall empty her land: for in the day of trouble they shalbe against her on euery side.
Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
3 Also to the bender that bendeth his bowe, and to him that lifteth himselfe vp in his brigandine, will I say, Spare not her yong men, but destroy all her hoste.
Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
4 Thus the slaine shall fall in the lande of the Caldeans, and they that are thrust through in her streetes.
Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
5 For Israel hath bene no widowe, nor Iudah from his God, from the Lord of hostes, though their lande was filled with sinne against the holy one of Israel.
Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
6 Flee out of the middes of Babel, and deliuer euery man his soule: be not destroyed in her iniquitie: for this is the time of the Lordes vengeance he will render vnto her a recompence.
“Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
7 Babel hath bene as a golden cuppe in the Lordes hand, that made all the earth drunken: the nations haue drunken of her wine, therefore do the nations rage.
Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
8 Babel is suddenly fallen, and destroyed: howle for her, bring balme for her sore, if she may be healed.
Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
9 We would haue cured Babel, but she could not be healed: forsake her, and let vs go euery one into his owne countrey: for her iudgement is come vp vnto heauen, and is lifted vp to ye cloudes.
Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
10 The Lord hath brought forth our righteousnesse: come and let vs declare in Zion the worke of the Lord our God.
“‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
11 Make bright the arrowes: gather the shieldes: the Lord hath raised vp the spirit of the King of the Medes: for his purpose is against Babel to destroy it, because it is the vengeance of the Lord, and the vengeance of his Temple.
“Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
12 Set vp the standart vpon the walles of Babel, make the watch strong: set vp the watchmen: prepare the skoutes: for the Lord hath both deuised, and done that which he spake against the inhabitantes of Babel.
Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
13 O thou that dwellest vpon many waters, abundant in treasures, thine ende is come, euen the ende of thy couetousnes.
Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
14 The Lord of hostes hath sworne by him selfe, saying, Surely I will fill thee with men, as with caterpillers, and they shall cry and shoute against thee.
Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
15 He hath made the earth by his power, and established the world by his wisedome, and hath stretched out the heauen by his discretion.
“Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
16 Hee giueth by his voyce the multitude of waters in the heauen, and he causeth the cloudes to ascend from the endes of the earth: he turneth lightnings to raine, and bringeth forth the winde out of his treasures.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
17 Euery man is a beast by his owne knowledge: euery founder is confounded by the grauen image: for his melting is but falsehood, and there is no breath therein.
“Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
18 They are vanitie, and the worke of errours: in the time of their visitation they shall perish.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
19 The portion of Iaakob is not like them: for he is the maker of all things, and Israel is the rodde of his inheritance: the Lord of hostes is his Name.
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
20 Thou art mine hammer, and weapons of warre: for with thee will I breake the nations, and with thee wil I destroy kingdomes,
“Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
21 And by thee wil I breake horse and horseman, and by thee will I breake the charet and him that rideth therein.
ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
22 By thee also will I breake man and woman, and by thee wil I breake olde and yong, and by thee wil I breake the yong man and the mayde.
Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
23 I wil also breake by thee the shepheard and his flocke, and by thee will I breake the husband man and his yoke of oxen, and by thee will I breake the dukes and princes.
Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
24 And I will render vnto Babel, and to all the inhabitants of the Caldeans all their euil, that they haue done in Zion, euen in your sight, sayth the Lord.
“Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
25 Beholde, I come vnto thee, O destroying mountaine, sayth the Lord, which destroyest all the earth: and I will stretch out mine hand vpon thee, and rolle thee downe from the rockes, and wil make thee a burnt mountaine.
“Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
26 They shall not take of thee a stone for a corner, nor a stone for foundations, but thou shalt be destroyed for euer, sayth the Lord.
Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
27 Set vp a standard in the lande: blowe the trumpets among the nations: prepare the nations against her: call vp the kingdomes of Ararat, Minni, and Ashchenaz against her: appoynt the prince against her: cause horses to come vp as the rough caterpillers.
“Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
28 Prepare against her the nations with the Kings of the Medes, the dukes thereof, and the princes thereof, and all the land of his dominion.
Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
29 And the land shall tremble and sorow: for the deuise of the Lord shalbe performed against Babel, to make the lande of Babel waste without an inhabitant.
Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
30 The strong men of Babel haue ceased to fight: they haue remayned in their holdes: their strength hath fayled, and they were like women: they haue burnt her dwelling places, and her barres are broken.
Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
31 A post shall runne to meete the post, and a messenger to meete the messenger, to shew the King of Babel, that his citie is taken on a side thereof,
Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
32 And that the passages are stopped, and the reedes burnt with fire, and the me of war troubled.
Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
33 For thus sayth the Lord of hosts the God of Israel, the daughter of Babel is like a threshing floore: the time of her threshing is come: yet a litle while, and the time of her haruest shall come.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
34 Nebuchad-nezzar the King of Babel hath deuoured me, and destroyed me: he hath made me an emptie vessel: he swallowed mee vp like a dragon, and filled his belly with my delicates, and hath cast me out.
A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
35 The spoyle of me, and that which was left of me, is brought vnto Babel, shall the inhabitant of Zion say: and my blood vnto the inhabitantes of Caldea, shall Ierusalem say.
Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
36 Therefore thus sayth the Lord, Beholde, I will maintayne thy cause, and take vengeance for thee, and I will drie vp the sea, and drie vp her springes.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
37 And Babel shall be as heapes, a dwelling place for dragons, an astonishment, and an hissing, without an inhabitant.
Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
38 They shall rore together like lions, and yell as the lyons whelpes.
Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
39 In their heate I will make them feastes, and I wil make them drunken, that they may reioyce, and sleepe a perpetual sleepe, and not wake, sayth the Lord.
Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
40 I wil bring them downe like lambes to the slaughter, and like rams and goates.
“Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
41 How is Sheshach taken! and howe is the glory of the whole earth taken! how is Babel become an astonishment among the nations!
“Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
42 The sea is come vp vpon Babel: he is couered with the multitude of the waues thereof.
Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
43 Her cities are desolate: the land is dry and a wildernes, a land wherein no man dwelleth, neither doth the sonne of man passe thereby.
Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
44 I wil also visite Bel in Babel, and I wil bring out of his mouth, that which he hath swallowed vp, and the nations shall runne no more vnto him, and the wall of Babel shall fall.
Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
45 My people, go out of the middes of her, and deliuer yee euery man his soule from the fierce wrath of the Lord,
“Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
46 Least your heart euen faynt, and ye feare the rumour, that shalbe heard in the land: the rumour shall come this yeere, and after that in the other yeere shall come a rumour, and crueltie in the land, and ruler against ruler.
Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
47 Therefore beholde, the dayes come, that I will visite the images of Babel, and the whole land shalbe confounded, and all her slayne shall fall in the middes of her.
Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
48 Then the heauen and the earth, and all that is therein, shall reioyce for Babel: for the destroyers shall come vnto her from the North, saith the Lord.
Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
49 As Babel caused the slaine of Israel to fal, so by Babel the slaine of all the earth did fall.
“Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
50 Ye that haue escaped the sworde, goe away, stand not still: remember the Lord a farre of, and let Ierusalem come into your minde.
Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
51 Wee are confounded because wee haue heard reproch: shame hath couered our faces, for straungers are come into the Sanctuaries of the Lordes House.
Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
52 Wherefore behold, the dayes come, sayth the Lord, that I will visite her grauen images, and through all her land the wounded shall grone.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
53 Though Babel should mount vp to heauen, and though shee should defend her strength on hye, yet from mee shall her destroyers come, sayth the Lord.
Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
54 A sound of a cry commeth from Babel, and great destruction from the land of the Caldeans,
“Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
55 Because the Lord hath layde Babel waste and destroyed from her the great voyce, and her waues shall roare like great waters, and a sounde was made by their noyse:
Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
56 Because the destroyer is come vpon her, euen vpon Babel, and her strong men are taken, their bowes are broken: for the Lord God that recompenceth, shall surely recompence.
Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
57 And I will make drunke her princes, and her wise men, her dukes, and her nobles, and her strong men: and they shall sleepe a perpetuall sleepe, and not wake, sayth the King, whose Name is the Lord of hostes.
Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
58 Thus saith the Lord of hostes, The thicke wall of Babel shalbe broken, and her hie gates shall be burnt with fire, and the people shall labour in vaine, and the folke in ye fire, for they shalbe weary.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
59 The worde which Ieremiah the Prophet commanded Sheraiah the sonne of Neriiah, the sonne of Maaseiah, when he went with Zedekiah the King of Iudah into Babel, in the fourth yeere of his reigne: and this Sheraiah was a peaceable prince.
Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
60 So Ieremiah wrote in a booke all the euill that should come vpon Babel: euen al these things, that are written against Babel.
Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
61 And Ieremiah sayd to Sheraiah, Whe thou commest vnto Babel, and shalt see, and shalt reade all these wordes,
Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
62 Then shalt thou say, O Lord, thou hast spoken against this place, to destroy it, that none should remaine in it, neither man nor beast, but that it should be desolate for euer.
Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
63 And when thou hast made an ende of reading this booke, thou shalt binde a stone to it, and cast it in the middes of Euphrates,
Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
64 And shalt say, Thus shall Babel be drowned, and shall not rise from the euil, that I will bring vpon her: and they shall be weary. Thus farre are the wordes of Ieremiah.
Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.

< Jeremiah 51 >