< Jeremiah 48 >

1 Concerning Moab, thus saith ye Lord of hostes, the God of Israel, Woe vnto Nebo: for it is wasted: Kiriathaim is confounded and taken: Misgab is confounded and afraide.
Ponena za Mowabu: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Tsoka kwa mzinda wa Nebo, chifukwa wawonongedwa. Mzinda wa Kiriyataimu wachititsidwa manyazi ndipo wagonjetsedwa; linga lichititsidwa manyazi ndipo lagumulidwa.
2 Moab shall boast no more of Heshbon: for they haue deuised euill against it. Come, and let vs destroy it, that it be no more a nation: also thou shalt be destroyed, O Madmen, and the sworde shall pursue thee.
Palibenso amene akutamanda Mowabu; ku Hesiboni anthu anamupanganira zoyipa: ‘Bwerani, tiyeni timuwonongeretu kuti asakhalenso mtundu wa anthu.’ Inunso anthu a ku Madimena, adzakukhalitsani chete; ankhondo adzakupirikitsani.
3 A voyce of crying shall be from Horonaim with desolation and great destruction.
Tamvani mfuwu wa anthu a ku Horonaimu. Iwo akulira kuti, ‘Kusakazika ndi kuwonongeka kwakukulu.’
4 Moab is destroyed: her litle ones haue caused their crie to be heard.
Mowabu wawonongeka; ana ake angʼonoangʼono akulira kwambiri.
5 For at the going vp of Luhith, the mourner shall goe vp with weeping: for in the going downe of Horonaim, the enemies haue heard a cry of destruction,
Anthu akukwera chikweza cha ku Luhiti, akulira kwambiri pamene akupita. Kulira chifukwa cha chiwonongeko kukumveka pa njira yotsikira ku Horonaimu.
6 Flee and saue your liues, and be like vnto the heath in the wildernesse.
Thawani! Dzipulumutseni; khalani ngati mbidzi ya mʼchipululu.
7 For because thou hast trusted in thy workes and in thy treasures, thou shalt also be taken, and Chemosh shall goe forth into captiuitie with his Priestes and his princes together.
Popeza inu munkadalira ntchito zanu ndi chuma chanu, nanunso mudzatengedwa ukapolo, ndipo Kemosi adzapita ku ukapolo, pamodzi ndi ansembe ake ndi akuluakulu ake.
8 And the destroyer shall come vpon all cities, and no citie shall escape: the valley also shall perish and the plaine shalbe destroyed as the Lord hath spoken.
Wowononga adzabwera ndi kusakaza mzinda uliwonse, ndipo palibe mzinda umene udzapulumuke. Chigwa chidzasanduka bwinja ndipo malo athyathyathya a pamwamba pa phiri adzawonongedwa monga Yehova wayankhulira.
9 Giue wings vnto Moab, that it may flee and get away: for the cities thereof shalbe desolate, without any to dwell therein.
Mtsineni khutu Mowabu chifukwa adzasakazika; mizinda yake idzasanduka mabwinja, wopanda munthu wokhalamo.
10 Cursed be he that doeth the worke of the Lord negligently, and cursed be he that keepeth backe his sword from blood.
“Wotembereredwa munthu amene amagwira ntchito ya Yehova monyinyirika! Wotembereredwa munthu amene amaletsa lupanga lake kupha anthu!
11 Moab hath bene at rest from his youth, and he hath setled on his lees, and hath not bene powred from vessell to vessell, neither hath he gone into captiuitie: therefore his taste remained in him and his sent is not changed.
“Mowabu wakhala pa mtendere kuyambira ubwana wake, ngati vinyo wokhazikika pa masese ake, osapungulidwa kuchoka mu mtsuko wina kuthira mu mtsuko wina; iye sanatengedwepo ukapolo. Nʼchifukwa chake kukoma kwake nʼkomwe kuja ndipo fungo lake silinasinthe.
12 Therefore beholde, the dayes come, saith the Lord, that I will send vnto him such as shall carie him away, and shall emptie his vessels, and breake their bottels.
Nʼchifukwa chake masiku akubwera,” akutero Yehova, “pamene ndidzatuma anthu amene amakhuthula vinyo mʼmitsuko ndipo adzamukhutula; adzakhuthula vinyo yense mitsuko yake pambuyo pake nʼkuphwanya mitsukoyo.
13 And Moab shalbe ashamed of Chemosh as the house of Israel was ashamed of Beth-el their confidence.
Pamenepo Mowabu adzachita manyazi ndi Kemosi, monga momwe Aisraeli anachitira manyazi ndi Beteli amene ankamukhutulira.
14 Howe thinke you thus, We are mightie and strong men of warre?
“Kodi munganene bwanji kuti, ‘Ife ndife asilikali. Ife ndife ngwazi, anthu amphamvu pa nkhondo?’
15 Moab is destroyed, and his cities burnt vp, and his chose yong men are gone downe to slaughter, saith ye King, whose name is ye Lord of hostes.
Owononga Mowabu ndi mizinda yake abwera ndipo ankhondo adzalowa mʼmidzi yake; anyamata ake okongola apita kukaphedwa,” ikutero Mfumu, imene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
16 The destruction of Moab is ready to come, and his plague hasteth fast.
Kugwa kwa Mowabu kuli pafupi; masautso ake akubwera posachedwa.
17 All ye that are about him, mourne for him, and all ye that knowe his name, say, Howe is the strong staffe broken, and the beautifull rod!
Mulireni kwambiri, inu nonse amene mwamuzungulira, inu nonse amene mumadziwa za kutchuka kwake; nenani kuti, “Taonani momwe yathyokera ndodo yamphamvu yaufumu ija, taonani momwe ndodo yaulemu yathyokera!”
18 Thou daughter that doest inhabite Dibon, come downe from thy glory, and sit in thirst: for the destroyer of Moab shall come vpon thee, and he shall destroy thy strong holdes.
“Tsikani pa ulemerero wanu ndipo khalani pansi powuma, inu anthu okhala ku Diboni, pakuti wowononga Mowabu wabwera kudzamenyana nanu, wasakaza mizinda yanu yotetezedwa.
19 Thou that dwellest in Aroer, stand by the way, and beholde: aske him that fleeth and that escapeth, and say, What is done?
Inu amene mumakhala ku Aroeri, imani mʼmbali mwa msewu ndi kumaonerera. Funsani mwamuna amene akuthawa ndiponso mkazi amene wapulumuka, afunseni kuti, ‘Kodi chachitika nʼchiyani?’”
20 Moab is cofouded: for it is destroied: howle, and cry, tell ye it in Arnon, that Moab is made waste,
Iwo adzayankha kuti, “Mowabu wachititsidwa manyazi, pakuti wasakazika. Lirani mwachisoni ndipo fuwulani! Lengezani ku mtsinje wa Arinoni kuti Mowabu wawonongedwa.
21 And iudgement is come vpon the plaine countrey, vpon Holon and vpon Iahazah, and vpon Mephaath,
Chiweruzo chabwera ku mizinda ya ku mapiri, ndiyo Holoni, Yaza, Mefaati,
22 And vpon Dibon, and vpon Nebo, and vpon the house of Diblathaim,
Diboni, Nebo, Beti-Dibilataimu,
23 And vpon Kiriathaim, and vpon Beth-gamul, and vpon Beth-meon,
Kiriyataimu, Beti-Gamuli, Beti-Meoni,
24 And vpon Kerioth, and vpon Bozrah, and vpon all the cities of ye land of Moab farre or neere.
Keriyoti ndi Bozira ndi mizinda yonse ya Mowabu, yakutali ndi yapafupi yomwe.
25 The horne of Moab is cut off, and his arme is broken, saith the Lord.
Mphamvu za Mowabu zawonongeka; mkono wake wathyoka,” akutero Yehova.
26 Make ye him drunken: for he magnified himselfe against the Lord: Moab shall wallowe in his vomite, and he also shalbe in derision.
“Muledzeretseni Mowabu, chifukwa anadzikuza powukira Yehova. Mulekeni Mowabu avivinizike mʼmasanzi ake; mulekeni akhale chinthu chomachiseka.
27 For diddest not thou deride Israel, as though he had bene found among theeues? for when thou speakest of him, thou art moued.
Kodi suja Israeli anali kwa iwe ngati chinthu chomachiseka? Kodi Israeli anapezeka pakati pa akuba kuti nthawi zonse poyankhula za iye, iwe uzimupukusira mutu momunyoza?
28 O ye that dwell in Moab, leaue the cities, and dwell in the rockes, and be like the doue, that maketh her nest in the sides of the holes mouth.
Inu amene mumakhala ku Mowabu, siyani mizinda yanu ndi kukakhala pakati pa matanthwe. Khalani ngati nkhunda imene imamanga chisa chake pa khomo la phanga.
29 We haue heard the pride of Moab (hee is exceeding proude) his stoutnesse, and his arrogancie, and his pride, and the hautinesse of his heart.
“Tamva za kunyada kwa Mowabu, kunyada kwake nʼkwakukulu. Ndi wodzitama, wonyada ndi wodzitukumula. Ali ndi mtima wodzikweza.
30 I know his wrath, saith ye Lord, but it shall not be so: and his dissimulatios, for they do not right.
Ine ndikuzidziwa ntchito zake, akutero Yehova. Ntchitozo ndi nʼzosapindulitsa kanthu.
31 Therefore will I howle for Moab, and I will crie out for all Moab: mine heart shall mourne for the men of Kir-heres.
Nʼchifukwa chake ndidzamulira Mowabu, ine ndikulira chifukwa cha anthu onse a ku Mowabu, ndikubuwula chifukwa cha anthu a ku Kiri Heresi.
32 O vine of Sibmah, I will weepe for thee, as I wept for Iazer: thy plants are gone ouer the sea, they are come to the sea of Iazer: ye destroyer is fallen vpon thy somer fruites, and vpon thy vintage,
Ndikukhetsa misozi chifukwa cha inu, kupambana momwe ndinalirira Yazeri. Inu anthu a ku Sibina muli ngati mipesa imene nthambi zake zatambalala mpaka ku Nyanja; zafika mpaka ku nyanja ya Yazeri. Wowononga wasakaza zipatso zake zachilimwe ndi mpesa.
33 And ioye, and gladnesse is taken from the plentifull fielde, and from the land of Moab: and I haue caused wine to faile from the winepresse: none shall treade with shouting: their shouting shall be no shouting.
Chimwemwe ndi chisangalalo zatha ku minda ya zipatso ya ku Mowabu. Ndaletsa kuchucha kwa vinyo mopsinyira mphesa; palibe amene akufuwula mokondwa akamapsinya mphesa. Ngakhale kufuwula kulipo, koma sikufuwula kwa chimwemwe.
34 From the cry of Heshbon vnto Elaleh and vnto Iahaz haue they made their noyse from Zoar vnto Horonaim, ye heiffer of three yere old shall go lowing: for ye waters also of Nimrim shalbe wasted.
“A ku Hesiboni ndi Eleali akulira ndipo mfuwu wawo ukumveka mpaka ku Yahazi, kuchokera ku Zowari mpaka ku Horonaimu ndi ku Egilati Selisiya. Ngakhale madzi a ku Nimurimu aphwa.
35 Moreouer, I will cause to cease in Moab, saith the Lord, him that offered in the high places, and him that burneth incense to his gods.
Ndidzawaletsa anthu a ku Mowabu kupereka nsembe mʼmalo awo opembedzera ndi kufukiza lubani kwa milungu yawo,” akutero Yehova.
36 Therefore mine heart shall sounde for Moab like a shaume, and mine heart shall sound like a shaume for the men of Ker-heres, because the riches that he hath gotten, is perished.
“Nʼchifukwa chake mtima wanga ukulirira Mowabu ngati chitoliro. Mtima wanga ukulirira anthu a ku Kiri Heresi ngati chitoliro chifukwa chuma chimene anachipata chatha.
37 For euery head shalbe balde, and euery beard plucked: vpon all the handes shall be cuttings, and vpon the loynes sackecloth.
Aliyense wameta mutu wake ndi ndevu zake; manja a munthu aliyense ndi ochekacheka, ndipo munthu aliyense wavala chiguduli mʼchiwuno mwake.
38 And mourning shall be vpon all the house toppes of Moab and in all the streetes thereof: for I haue broken Moab like a vessell wherein is no pleasure, sayeth the Lord.
Pa madenga onse a ku Mowabu ndiponso mʼmisewu yake anthu akungolira, pakuti ndaphwanya Mowabu ngati mtsuko wopanda ntchito,” akutero Yehova.
39 They shall howle, saying, How is he destroyed? howe hath Moab turned the backe with shame? so shall Moab be a derision, and a feare to all them about him.
“Taonani mmene waphwanyikira! Tamvani momwe akulirira! Taonani momwe Mowabu wachititsidwira manyazi. Mowabu wasanduka chinthu chonyozeka, chinthu chochititsa mantha kwa onse amene amuzungulira.”
40 For thus saith the Lord, Beholde, he shall flee as an eagle, and shall spread his wings ouer Moab.
Yehova akuti, “Mtundu wina udzachita kuwuluka nʼkugwera pa Mowabu ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
41 The cities are taken, and the strong holdes are wonne, and ye mightie mens hearts in Moab at that day shalbe as ye heart of a woman in trauaile.
Mizinda idzagwidwa ndipo malinga adzalandidwa. Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Mowabu idzakhala ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.
42 And Moab shall be destroyed from being a people, because he hath set vp himselfe against the Lord.
Mowabu sudzakhala mtundu wa anthu chifukwa unadzikuza powukira Yehova.
43 Feare, and pit and snare shall be vpon thee, O inhabitant of Moab, saith the Lord.
Zoopsa, dzenje ndi msampha zikudikira inu anthu a ku Mowabu,” akutero Yehova.
44 He that escapeth from the feare, shall fall in the pit, and he that getteth vp out of the pit, shall be taken in the snare: for I will bring vpon it, euen vpon Moab, the yeere of their visitation, sayeth the Lord.
“Aliyense wothawa zoopsa adzagwera mʼdzenje, aliyense wotuluka mʼdzenje adzakodwa mu msampha. Ndigwetsa zimenezi pa Mowabu pa nthawi ya chilango chake,” akutero Yehova.
45 They that fled, stoode vnder the shadowe of Heshbon, because of the force: for the fire came out of Heshbon, and a flame from Sihon, and deuoured the corner of Moab, and the top of the seditious children.
“Anthu othawa nkhondo ayima pa mthunzi wa Hesiboni chifukwa chotopa. Koma moto wayaka kuchokera ku Hesiboni, malawi a moto abuka kuchokera ku nyumba ya mfumu Sihoni. Motowo ukuwononga mapiri a ku Mowabu, dziko la anthu onyada.
46 Wo be vnto thee, O Moab: the people of Chemosh perisheth: for thy sonnes are taken captiues, and thy daughters led into captiuitie.
Tsoka kwa iwe Mowabu! Anthu opembedza Kemosi awonongeka. Ana ako aamuna ndi aakazi atengedwa ukapolo.
47 Yet will I bring againe the captiuitie of Moab in the latter dayes, sayeth the Lord. Thus farre of the iudgement of Moab.
“Komabe masiku akutsogolo ndidzabwezeranso Mowabu chuma chake,” akutero Yehova. Chiweruzo cha Mowabu chathera pamenepa.

< Jeremiah 48 >