< Jeremiah 42 >
1 Then all the captaines of the hoste, and Iohanan the sonne of Kareah, and Iezaniah the sonne of Hoshaaiah, and all the people from the least vnto the most came,
Atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi Yohanani mwana wa Kareya ndi Azariya mwana wa Hosayia, ndiponso anthu onse, ana ndi akuluakulu omwe, anapita
2 And saide vnto Ieremiah the Prophete, Heare our prayer, we beseeche thee, and pray for vs vnto the Lord thy God, euen for all this remnant (for we are left, but a fewe of many, as thine eyes doe beholde)
kwa mneneri Yeremiya ndipo anamuwuza kuti, “Chonde imvani dandawulo lathu ndipo mutipempherere anthu otsalafe kwa Yehova Mulungu wanu. Pakuti monga tsopano mukuona, ngakhale kuti kale tinalipo ambiri, koma tsopano ochepa okha ndiye amene atsala.
3 That the Lord thy God may shewe vs the way wherein wee may walke, and the thing that we may doe.
Mupemphere kuti Yehova Mulungu wanu atiwuze kumene tiyenera kupita ndi chimene tiyenera kuchita.”
4 Then Ieremiah the Prophet said vnto them, I haue heard you: behold, I will pray vnto ye Lord your God according to your wordes, and whatsoeuer thing the Lord shall answere you, I will declare it vnto you: I will keepe nothing backe from you.
Mneneri Yeremiya anawayankha kuti, “Ndamva zimene mwanenazi. Ndithu ndidzapemphera kwa Yehova Mulungu wanu monga momwe mwandipemphera. Ndidzakuwuzani chilichonse chimene Yehova anene ndipo sindidzakubisirani kanthu kalikonse.”
5 Then they said to Ieremiah, The Lord be a witnesse of trueth, and faith betweene vs, if we doe not, euen according to all things for ye which the Lord thy God shall send thee to vs.
Ndipo iwo anawuza Yeremiya kuti, “Yehova akhale mboni yoona ndi yokhulupirika yodzatitsutsa ife ngati sitichita mogwirizana ndi chilichonse chimene Yehova Mulungu adzakutumani kuti mutiwuze.
6 Whether it be good or euill, we will obey the voyce of the Lord God, to whom we sende thee that it may be well with vs, when wee obey the voyce of the Lord our God.
Kaya ndi zotikomera kapena zosatikomera, ife tidzamvera Yehova Mulungu wathu, amene takutumaniko. Tidzamvera Yehova Mulungu wathu kuti zinthu zidzatiyendere bwino.”
7 And so after ten dayes came the word of the Lord vnto Ieremiah.
Patapita masiku khumi, Yehova anayankhula ndi Yeremiya.
8 Then called he Iohanan the sonne of Kareah, and all the captaines of the hoste, which were with him, and all ye people from ye least to the most,
Choncho Yeremiya anayitana Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi atsogoleri onse a ankhondo amene anali naye ndiponso anthu onse, ana ndi akulu omwe.
9 And saide vnto them, Thus saith the Lord God of Israel, vnto whom ye sent me to present your prayers before him,
Yehova, Mulungu wa Israeli amene munanditumako kuti ndikapereke madandawulo mʼdzina lanu akuti,
10 If ye will dwell in this land, then I wil build you, and not destroy you, and I will plant you, and not roote you out: for I repent me of the euill that I haue done vnto you.
“Ngati mukhala mʼdziko muno, ndiye kuti ndidzakukhazikitsani, osakuchotsani. Inde ndidzakudzalani osakuchotsani pakuti ndi kumva chisoni kwambiri chifukwa cha mavuto amene ndabweretsa pa inu.
11 Feare not for the King of Babel, of whom ye are afraide: be not afraid of him, saith the Lord: for I am with you, to saue you, and to deliuer you from his hand,
Musayiope mfumu ya ku Babuloni, imene mukuyiopa tsopano. Musachite nayo mantha, akutero Yehova, pakuti Ine ndili nanu ndipo ndidzakupulumutsani ndi kukulanditsani mʼmanja mwake.
12 And I will graunt you mercie that he may haue compassion vpon you, and he shall cause you to dwell in your owne land.
Ndidzakuchitirani chifundo, ndipo mfumuyonso idzakuchitirani chifundo ndi kukulolani kuti mukhale mʼdziko mwanumwanu.
13 But if ye say, We will not dwell in this land, neither heare the voyce of the Lord your God,
“Koma mwina simudzamvera Yehova Mulungu wanu nʼkumanena kuti, ‘Ayi ife sitidzakhala mʼdziko muno,
14 Saying, Nay, but we will goe into the land of Egypt, where we shall see no warre, nor heare the sounde of the trumpet, nor haue hunger of bread, and there will we dwell,
ndipo ngati mukunena kuti, ‘Ayi, koma tidzapita ku Igupto kumene sitidzaonako nkhondo kapena kumva kulira kwa lipenga kapenanso kusowa chakudya.’
15 (And nowe therefore heare the worde of the Lord, ye remnant of Iudah: thus sayeth the Lord of hostes the God of Israel, If ye set your faces to enter into Egypt, and goe to dwell there)
Tsono, inu otsala a ku Yuda, imvani mawu a Yehova. Iye akuti, ngati mutsimikiza zopita ku Igupto, nʼkupitadi kukakhala kumeneko,
16 Then the sworde that ye feared, shall take you there in the land of Egypt, and the famine, for the which ye care, shall there hang vpon you in Egypt, and there shall ye die.
ndiye nkhondo imene mukuyiopayo idzakugonjetsani ku Igupto komweko. Njala imene mukuyiopayo idzakupezani ku Igupto komweko ndipo mudzafera kumeneko.
17 And all the men that set their faces to enter into Egypt to dwell there, shall die by ye sword, by the famine and by the pestilence, and none of them shall remaine nor escape from the plague, that I will bring vpon them.
Kunena zoona, onse amene atsimikiza zopita ku Igupto kuti akakhale kumeneko adzafa ndi nkhondo njala ndi mliri. Palibe ndi mmodzi yemwe amene adzapulumuke kapena kuthawa mavuto amene ndidzawagwetsera.’
18 For thus saith the Lord of hostes the God of Israel, As mine anger and my wrath hath bene powred foorth vpon the inhabitants of Ierusalem: so shall my wrath be powred foorth vpon you, when ye shall enter into Egypt, and ye shall be a detestation, and an astonishment, and a curse and a reproche, and ye shall see this place no more.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Momwe ndinawakwiyira mwaukali anthu okhala mu Yerusalemu, koteronso ndidzakukwiyirani mukapita ku Igupto. Mudzasanduka chinthu chotembereredwa ndi chochititsa mantha, choseketsa ndi chonyozeka. Malo ano simudzawaonanso.’
19 O ye remnant of Iudah, the Lord hath said concerning you, Goe not into Egypt: knowe certeinely that I haue admonished you this day.
“Inu otsala a ku Yuda, Yehova wakuwuzani kuti, ‘Musapite ku Igupto.’ Dziwani chinthu ichi: Ine lero ndikukuchenjezani
20 Surely ye dissembled in your hearts When ye sent me vnto the Lord your God, saying, Pray for vs vnto the Lord our God, and declare vnto vs euen according vnto al that the Lord our God shall say, and we will doe it.
kuti munalakwitsa kwambiri. Inu munandituma kwa Yehova Mulungu wanu nʼkumati ‘Mukatipempherere kwa Yehova Mulungu wathu, nʼkudzatiwuza chimene afuna kuti tichite, ndipo ife tidzachita.’
21 Therefore I haue this day declared it you, but you haue not obeyed the voyce of the Lord your God, nor any thing for the which he hath sent me vnto you.
Ine lero ndakuwuzani, koma inu simukumverabe zonse zimene Yehova Mulungu anandituma kuti ndikuwuzeni.
22 Nowe therefore, knowe certeinely that ye shall die by the sworde, by the famine, and by the pestilence, in the place whither ye desire to goe and dwell.
Tsono dziwani ichi: mudzafadi ndi nkhondo, njala ndi mliri kumalo kumene mukufuna mukakhaleko.”