< Jeremiah 35 >
1 The worde which came vnto Ieremiah from the Lord, in the dayes of Iehoiakim the sonne of Iosiah King of Iudah, saying,
Yehova anayankhula ndi Yeremiya nthawi ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, kuti:
2 Go vnto the house of the Rechabites, and speake vnto them, and bring them into the house of the Lord into one of the chambers, and giue them wine to drinke.
“Pita ku banja la Arekabu ndipo ukawayitane kuti abwere mʼchipinda chimodzi cha Nyumba ya Yehova ndipo akafika uwapatse vinyo kuti amwe.”
3 Then tooke I Iaazaniah, the sonne of Ieremiah the sonne of Habazziniah, and his brethren, and all his sonnes, and the whole house of the Rechabites,
Choncho ndinakatenga Yaazaniya (mwana wa Yeremiya winanso amene anali mwana wa Habaziniya), abale ake, ana ake onse aamuna ndi banja lonse la Arekabu.
4 And I brought them into the House of the Lord, into the chamber of the sonnes of Hanan, the sonne of Igdaliah a man of God, which was by the chamber of the princes, which was aboue the chamber of Maaseiah the sonne of Shallum, the keeper of the treasure.
Ndinabwera nawo ku Nyumba ya Yehova, ku chipinda cha ophunzira a mneneri Hanani mwana wa Igidaliya, munthu wa Mulungu. Chipinda chimenechi chinali pafupi ndi chipinda cha akuluakulu, chimene chinali pamwamba pa chipinda cha Maaseya mwana wa Salumu, mlonda wa pa khomo.
5 And I set before the sonnes of the house of the Rechabites, pots full of wine, and cuppes, and said vnto them, Drinke wine.
Kenaka ndinayika mabotolo odzaza ndi vinyo ndi zikho zake pamaso pa Arekabu ndipo ndinawawuza kuti, “Imwani vinyoyu.”
6 But they said, We will drinke no wine: for Ionadab the sonne of Rechab our father commanded vs, saying, Ye shall drinke no wine, neither you nor your sonnes for euer.
Koma iwo anayankha kuti, “Ife sitimwa vinyo, chifukwa kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula kuti, ‘Inuyo ngakhale zidzukulu zanu, musadzamwe vinyo mpaka kalekale.
7 Neither shall ye build house, nor sow seede, nor plant vineyarde, nor haue any, but all your dayes ye shall dwell in tentes, that ye may liue a long time in the land where ye be strangers.
Musadzamange nyumba kapena kufesa mbewu, kapena kulima minda ya mpesa; musadzakhale ndi zinthu zimenezi. Mʼmalo mwake muzidzakhale mʼmatenti. Mukadzatero mudzakhala nthawi yayitali mʼdziko limene mukukhalamo.’
8 Thus haue wee obeyed the voyce of Ionadab the sonne of Rechab our father, in all that he hath charged vs, and wee drinke no wine all our dayes, neither wee, our wiues, our sonnes, nor our daughters.
Ife takhala tikumvera zonse zimene kholo lathu Yehonadabu mwana wa Rekabu anatilamula. Ife ngakhale akazi athu kapena ana athu aamuna ndi aakazi sitinamwepo vinyo
9 Neither builde wee houses for vs to dwell in, neither haue we vineyard, nor fielde, nor seede,
kapena kumanga nyumba kuti tizikhalamo kapenanso kukhala ndi minda ya mpesa, minda ina iliyonse kapena mbewu.
10 But we haue remained in tentes, and haue obeyed, and done according to all that Ionadab our father commanded vs.
Koma takhala mʼmatenti ndipo tamvera kwathunthu chilichonse chimene kholo lathu Yehonadabu anatilamula.
11 But when Nebuchad-nezzar King of Babel came vp into the land, we said, Come, and let vs go to Ierusalem, from the hoste of the Caldeans, and from the host of Aram: so we dwel at Ierusalem.
Koma pamene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anathira nkhondo dziko lino, ife tinati, ‘Tiyeni tichoke, tipite ku Yerusalemu kuti tithawe magulu ankhondo a Akasidi ndi Aaramu.’ Kotero ife takhala tikukhala mu Yerusalemu.”
12 Then came the word of the Lord vnto Ieremiah, saying,
Yehova anayankhulanso ndi Yeremiya kuti,
13 Thus saith the Lord of hostes, the God of Israel, Goe, and tell the men of Iudah, and the inhabitants of Ierusalem, Will ye not receiue doctrine to obey my wordes, saith the Lord?
“Iyeyu, Yehova Mulungu wa Israeli anawuza Yeremiya kuti: Pita ukawawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu kuti, ‘Kodi simungatengeko phunziro ndi kumvera mawu anga?’ akutero Yehova.
14 The commandement of Ionadab the sonne of Rechab that hee commanded his sonnes, that they should drinke no wine, is surely kept: for vnto this day they drinke none, but obey their fathers commandement: notwithstanding I haue spoken vnto you, rising earely, and speaking, but ye would not obey me.
‘Yehonadabu mwana wa Rekabu analamula ana ake kuti asamwe vinyo ndipo lamulo limeneli alisunga. Mpaka lero lino iwo samwa vinyo, chifukwa akumvera lamulo la kholo lawo. Koma Ine ndakhala ndikuyankhula nanu kawirikawiri kukuchenjezani, koma inu simunandimvere Ine.
15 I haue sent also vnto you all my seruants the Prophetes, rising vp earely, and sending, them, saying, Returne nowe euery man from his euill way, and amende your workes, and goe not after other gods to serue them, and ye shall dwel in the lande which I haue giuen vnto you, and to your fathers, but ye would not encline your eare, nor obey mee.
Kawirikawiri ndakhala ndikutumiza atumiki anga, aneneri, kwa inu. Iwo akhala akukuwuzani kuti, ‘Aliyense wa inu asiye ntchito zake zoyipa ndi kukonza makhalidwe ake; musatsatire milungu ina ndi kumayitumikira. Pamenepo mudzakhala mʼdziko limene ndinakupatsani ndi makolo anu.’ Komabe inu simunasamale zimenezi kapena kundimvera Ine.
16 Surely the sonnes of Ionadab the sonne of Rechab, haue kept the commandement of their father, which he gaue them, but this people hath not obeyed me.
Zidzukulu za Yehonadabu mwana wa Rekabu zakhala zikumvera lamulo limene kholo lawo anazilamula, koma inuyo simunandimvere Ine.
17 Therefore thus saith the Lord of hostes, the God of Israel, Beholde, I will bring vpon Iudah, and vpon all the inhabitants of Ierusalem, all the euill that I haue pronounced against them, because I haue spoke vnto them, but they would not heare, and I haue called vnto them, but they would not answere.
“Nʼchifukwa chake Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ndidzagwetsera pa Yuda ndi pa onse okhala mu Yerusalemu masautso onse amene ndinakonza chifukwa sanandimvere. Ndinawayitana koma iwo sanayankhe.’”
18 And Ieremiah said to the house of the Rechabites, Thus saith the Lord of hostes the God of Israel, Because ye haue obeyed the commandement of Ionadab your father, and kept all his precepts, and done according vnto all that hee hath commanded you,
Yeremiya anawuza banja la Arekabu mawu onse a Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, kuti, “Munamvera lamulo la kholo lanu Yehonadabu ndipo mwatsatira malangizo ake onse ndi kuchita chilichonse chimene anakulamulani.”
19 Therefore thus saith the Lord of hostes, the God of Israel, Ionadab the sonne of Rechab shall not want a man, to stand before me for euer.
Tsono Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Yehonadabu mwana wa Rekabu sadzasowa munthu wonditumikira Ine nthawi zonse.”