< Jeremiah 33 >
1 Moreover, the worde of the Lord came vnto Ieremiah the second time (while he was yet shut vp in the court of prison) saying,
Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati:
2 Thus sayth the Lord, the maker thereof, the Lord that formed it, and established it, the Lord is his Name.
“Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti,
3 Call vnto me, and I will answere thee, and shewe thee great and mightie things, which thou knowest not.
‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’
4 For thus saith the Lord God of Israel, concerning the houses of this citie, and concerning the houses of the Kings of Iudah, which are destroyed by the mounts, and by the sword,
Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni.
5 They come to fight with the Caldeans, but it is to fill themselues with the dead bodies of men, whome I haue slaine in mine anger and in my wrath: for I haue hid my face from this citie, because of all their wickednes.
Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.
6 Behold, I will giue it health and amendment: for I wil cure them, and will reueile vnto them the abundance of peace, and trueth.
“‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni.
7 And I wil cause the captiuitie of Iudah and the captiuitie of Israel to returne, and will build them as at the first.
Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba.
8 And I wil clense them from all their iniquitie, whereby they haue sinned against me: yea, I wil pardon all their iniquities, whereby they haue sinned against me, and whereby they haue rebelled against me.
Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira.
9 And it shalbe to me a name, a ioy, a praise, and an honour before all the nations of the earth, which shall heare all ye good that I doe vnto them: and they shall feare and tremble for all the goodnes, and for all the wealth, that I shew vnto this citie.
Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’
10 Thus sayth the Lord, Againe there shalbe heard in this place (which ye say shalbe desolate, without man, and without beast, euen in the cities of Iudah, and in the streetes of Ierusalem, that are desolate without man, and without inhabitant, and without beast)
“Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso
11 The voyce of ioy and the voyce of gladnes, the voyce of the bridegrome, and the voyce of the bride, the voyce of them that shall say, Prayse the Lord of hostes, because the Lord is good: for his mercy endureth for euer, and of them that offer the sacrifice of prayse in the House of the Lord, for I will cause to returne the captiuitie of the land, as at the first, sayth the Lord.
mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati, “Yamikani Yehova Wamphamvuzonse, popeza Iye ndi wabwino; pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.” Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.
12 Thus sayth the Lord of hostes, Againe in this place, which is desolate, without man, and without beast, and in all the cities thereof there shall be dwelling for shepheards to rest their flockes.
“Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo.
13 In the cities of the mountaines, in the cities in the plaine, and in the cities of the South, and in the land of Beniamin, and about Ierusalem, and in the cities of Iudah shall the sheepe passe againe, vnder the hand of him that telleth them, sayth the Lord.
Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.
14 Beholde, the dayes come, sayth the Lord, that I wil performe that good thing, which I haue promised vnto the house of Israel, and to the house of Iudah.
“‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.
15 In those dayes and at that time, wil I cause the branch of righteousnesse to growe vp vnto Dauid, and he shall execute iudgement, and righteousnes in the land.
“‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide; munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 In those dayes shall Iudah be saued, and Ierusalem shall dwell safely, and hee that shall call her, is the Lord our righteousnesse.
Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere. Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili: Yehova Chilungamo Chathu.’
17 For thus sayth the Lord, Dauid shall neuer want a man to sit vpon the throne of the house of Israel.
Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli,
18 Neither shall the Priests and Leuites want a man before me to offer burnt offerings, and to offer meat offerings, and to doe sacrifice continually.
ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’”
19 And the worde of the Lord came vnto Ieremiah, saying,
Yehova anawuza Yeremiya kuti:
20 Thus sayth the Lord, If you can breake my couenant of the day, and my couenant of the night, that there should not be day, and night in their season,
Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye.
21 Then may my couenant be broken with Dauid my seruant, that he should not haue a sonne to reigne vpon his throne, and with the Leuites, and Priests my ministers.
Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse.
22 As the army of heauen can not be nombred, neither the sand of the sea measured: so wil I multiplie the seede of Dauid my seruant, and the Leuites, that minister vnto me.
Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.
23 Moreouer, the worde of the Lord came to Ieremiah, saying,
Yehova anafunsa Yeremiya kuti,
24 Considerest thou not what this people haue spoken, saying, The two families, which the Lord hath chosen, hee hath euen cast them off? thus they haue despised my people, that they should be no more a nation before them.
“Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu.
25 Thus sayth the Lord, If my couenant be not with day and night, and if I haue not appointed the order of heauen and earth,
‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi,
26 Then will I cast away the seede of Iaakob and Dauid my seruant, and not take of his seede to be rulers ouer the seede of Abraham, Izhak, and Iaakob: for I wil cause their captiuitie to returne, and haue compassion on them.
monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’”