< Jeremiah 22 >
1 Thus said the Lord, Goe downe to the house of the King of Iudah, and speake there this thing,
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ku nyumba ya mfumu ya ku Yuda ndipo ukayiwuze kuti,
2 And say, Heare the worde of the Lord, O King of Iudah, that sittest vpon the throne of Dauid, thou and thy seruants, and thy people that enter in by these gates.
‘Imva mawu a Yehova, iwe mfumu ya ku Yuda, amene umakhala pa mpando waufumu wa Davide; iwe, nduna zako pamodzi ndi anthu ako amene amalowera pa zipata izi.
3 Thus saith the Lord, Execute ye iudgement and righteousnes, and deliuer the oppressed from the hande of the oppressor, and vexe not the stranger, the fatherlesse, nor the widowe: doe no violence, nor sheade innocent blood in this place.
Yehova akuti, uziweruza molungama ndi mosakondera. Uzipulumutsa munthu amene walandidwa katundu mʼdzanja la womuzunza. Usazunze kapena kupondereza mlendo, ana amasiye kapena akazi amasiye. Usaphe munthu wosalakwa pa malo pano.
4 For if ye do this thing, then shall the kings sitting vpon the throne of Dauid enter in by the gates of this House, and ride vpon charets, and vpon horses, both he and his seruants and his people.
Pakuti ngati udzamvera malamulo awa, ndiye kuti mafumu onse okhala pa mpando waufumu wa Davide azidzalowabe pa zipata za nyumba yaufumu ino, atakwera magaleta ndi akavalo, iwowo pamodzi ndi nduna zawo ndi anthu awo.
5 But if ye will not heare these wordes, I sweare by my selfe, saith the Lord, that this House shalbe waste.
Koma ngati sumvera malamulo awa, akutero Yehova, ndikulumbira pali Ine ndemwe kuti nyumba ino yaufumu idzasanduka bwinja.’”
6 For thus hath the Lord spoken vpon the Kings house of Iudah, Thou art Gilead vnto me, and the head of Lebanon, yet surely I wil make thee a wildernes and as cities not inhabited,
Pakuti zimene Yehova akunena za nyumba yaufumu ya mfumu ya ku Yuda ndi izi: “Ngakhale iwe uli ngati Giliyadi kwa Ine, ngati msonga ya phiri la Lebanoni, komabe ndidzakusandutsa chipululu, ngati mizinda yopanda anthu.
7 And I will prepare destroyers against thee, euery one with his weapons, and they shall cut downe thy chiefe cedar trees, and cast them in the fire.
Ndidzatuma anthu oti adzakuwononge, munthu aliyense ali ndi zida zake, ndipo adzadula mikungudza yako yokongola nadzayiponya pa moto.
8 And many nations shall passe by this citie, and they shall say euery man to his neighbour, Wherefore hath the Lord done thus vnto this great citie?
“Pamene anthu a mitundu ina adzadutsa pa mzinda umenewu adzafunsana kuti, ‘Chifukwa chiyani Yehova wachita chinthu chotere pa mzinda waukuluwu?’
9 Then shall they answere, Because they haue forsaken the couenant of the Lord their God, and worshipped other gods, and serued them.
Ndipo yankho lake lidzakhala lakuti, ‘Chifukwa anasiya pangano limene anapangana ndi Yehova Mulungu wawo ndipo anapembedza ndi kutumikira milungu ina.’”
10 Weepe not for the dead, and be not moued for them, but weepe for him that goeth out: for he shall returne no more, nor see his natiue countrey.
Musayilire mfumu Yosiya, musamuyimbire nyimbo womwalirayo; mʼmalo mwake, mulire kwambiri chifukwa cha Yehowahazi amene wapita ku ukapolo, chifukwa sadzabwereranso kapena kuonanso dziko lake lobadwira.
11 For thus saith ye Lord, As touching Shallum the sonne of Iosiah King of Iudah, which reigned for Iosiah his father, which went out of this place, he shall not returne thither,
Pakuti zimene Yehova akunena za Yehowahazi mwana wa Yosiya, amene anatenga mpando waufumu wa Yuda mʼmalo mwa abambo ake koma nʼkuwusiya ndi izi: “Iye sadzabwereranso.
12 But he shall die in the place, whither they haue ledde him captiue, and shall see this lande no more.
Iyeyo adzafera ku ukapoloko. Sadzalionanso dziko lino.”
13 Wo vnto him that buildeth his house by vnrighteousnesse, and his chambers without equitie: he vseth his neighbour without wages, and giueth him not for his worke.
“Tsoka kwa munthu womanga nyumba yake mopanda chilungamo, womanga zipinda zake zosanja monyenga, pogwiritsa ntchito abale ake mwathangata, osawapatsa malipiro a ntchito yawo.
14 He saith, I will build me a wide house and large chambers: so he will make him selfe large windowes, and feeling with cedar, and paint them with vermilion.
Munthuyo amati, ‘Ndidzadzimangira nyumba yayikulu ya zipinda zikuluzikulu zamʼmwamba.’ Kotero ndidzapanga mazenera akuluakulu, ndi kukhomamo matabwa a mkungudza ndi kukongoletsa ndi makaka ofiira.
15 Shalt thou reigne, because thou closest thy selfe in cedar? did not thy father eate and drinke and prosper, when he executed iudgement and iustice?
“Kodi kukhala ndi nyumba ya mkungudza wambiri zingachititse iwe kukhala mfumu? Ganiza za abambo ako. Suja anali ndi zonse zakudya ndi zakumwa. Abambo ako ankaweruza molungama ndi mosakondera, ndipo zonse zinkawayendera bwino.
16 When he iudged the cause of the afflicted and the poore, he prospered: was not this because he knewe me, saith the Lord?
Iye ankateteza anthu osauka ndi osowa, ndipo zonse zinkamuyendera bwino. Kodi zimenezi sindiye tanthauzo la kudziwa Ine?” akutero Yehova.
17 But thine eyes and thine heart are but only for thy couetousnesse, and for to sheade innocent blood, and for oppression, and for destruction, euen to doe this.
“Koma maso ako ndi mtima sizili penanso, koma zili pa phindu lachinyengo, pa zopha anthu osalakwa ndi pa kuzunza ndi pakulamulira mwankhanza.”
18 Therefore thus saith the Lord against Iehoiakim, the sonne of Iosiah king of Iudah, They shall not lament him, saying, Ah, my brother, or ah, sister: neither shall they mourne for him, saying, Ah, lord, or ah, his glorie.
Nʼchifukwa chake Yehova ponena za Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda akuti, “Anthu sadzamulira maliro kapena kunena kuti, ‘Kalanga ine, mʼbale wanga! Kalanga ine mlongo wanga! Anthu ake sadzamulira maliro kuti, Kalanga ine, mbuye wathu! Taonani ulemerero wake wapita!’
19 He shalbe buryed, as an asse is buryed, euen drawen and cast foorth without the gates of Ierusalem.
Adzayikidwa ngati bulu, kuchita kumuguguza ndi kukamutaya kunja kwa zipata za Yerusalemu.”
20 Goe vp to Lebanon, and cry: showte in Bashan and crye by the passages: for all thy louers are destroyed.
“Tsono inu anthu a ku Yerusalemu, pitani ku mapiri a Lebanoni kuti mukalire mofuwula kumeneko, mawu anu akamveke mpaka ku Basani. Mulire mofuwula muli ku Abarimu chifukwa abwenzi ako onse awonongeka.
21 I spake vnto thee when thou wast in prosperitie: but thou saidest, I will not heare: this hath bene thy maner from thy youth, that thou wouldest not obey my voyce.
Ndinakuchenjezani pamene munali pa mtendere. Koma inu munati, ‘Sindidzamvera.’ Umu ndi mmene mwakhala mukuchitira kuyambira mukali aangʼono. Simunandimvere Ine.
22 The wind shall feede all thy pastors, and thy louers shall goe into captiuitie: and then shalt thou be ashamed and confounded of al thy wickednesse.
Mphepo idzakuchotserani abusa anu onse, ndipo abwenzi anu adzatengedwa ku ukapolo. Pamenepo mudzachita manyazi ndi kunyozedwa chifukwa cha zoyipa zanu zonse.
23 Thou that dwellest in Lebanon, and makest thy nest in the cedars, howe beautiful shalt thou be when sorowes come vpon thee, as the sorowe of a woman in trauaile?
Inu amene mumakhala mʼnyumba ya ku Lebanoni, amene munamanga nyumba zanu pakati pa mikungudza, mudzabuwula kwambiri pamene zowawa zidzakugwerani, zonga za mkazi pa nthawi yake yochira!
24 As I liue, saith the Lord, though Coniah the sonne of Iehoiakim King of Iudah, were the signet of my right hand, yet would I plucke thee thence.
“Pali Ine wamoyo, akutero Yehova, ngakhale iwe, Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu mfumu ya ku Yuda, ukanakhala ngati mphete ya ku dzanja langa lamanja, ndikanakuvula nʼkukutaya.
25 And I will giue thee into the hande of them that seeke thy life, and into the hande of them, whose face thou fearest, euen into the hand of Nebuchad-nezzar king of Babel, and into the hande of the Caldeans.
Ndidzakupereka kwa amene akufuna kukupha, amene iwe umawaopa. Ndidzakupereka kwa Nebukadinezara, mfumu ya ku Babuloni ndi anthu ake.
26 And I will cause them to cary thee away, and thy mother that bare thee, into another countrey, where ye were not borne, and there shall ye die.
Iwe pamodzi ndi amayi ako amene anakubereka ndidzakupititsani ku dziko lachilendo. Ngakhale inu simunabadwire kumeneko, komabe mudzafera komweko.
27 But to the lande, whereunto they desire to returne, they shall not returne thither.
Simudzabwereranso ku dziko limene mudzafuna kubwerera.”
28 Is not this man Coniah as a despised and broken idole? or as a vessell, wherein is no pleasure? wherefore are they caryed away, hee and his seede, and cast out into a lande that they knowe not?
Kodi Yehoyakini wakhala ngati mbiya yonyozeka, yosweka imene anthu sakuyifunanso? Kodi nʼchifukwa chake iye pamodzi ndi ana ake, achotsedwa nʼkutayidwa ku dziko limene iwo sakulidziwa?
29 O earth, earth, earth, heare the worde of the Lord.
Iwe dziko, dziko, dziko, Imva mawu a Yehova!
30 Thus saith the Lord, Write this man destitute of children, a man that shall not prosper in his dayes: for there shall be no man of his seede that shall prosper and sit vpon the throne of Dauid, or beare rule any more in Iudah.
Yehova akuti, “Munthu ameneyu mumutenge ngati wopanda ana, munthu amene sadzakhala wochita bwino pamoyo wake wonse, pakuti palibe ndi mmodzi yemwe mwa zidzukulu zake zomwe zidzachita bwino. Palibe amene adzathe kukhala pa mpando waufumu wa Davide ndi kulamulira Yuda.”