< Jeremiah 12 >

1 O Lord, if I dispute with thee, thou art righteous: yet let mee talke with thee of thy iudgements: wherefore doeth the way of the wicked prosper? why are all they in wealth that rebelliously transgresse?
Yehova, Inu mumakhala wokhoza nthawi zonse ndikati nditsutsane nanu. Komabe ndikufuna kuyankhula nanu za mlandu wanga. Chifukwa chiyani anthu oyipa zinthu zimawayendera bwino? Chifukwa chiyani anthu achinyengo amakhala pabwino?
2 Thou hast planted them, and they haue taken roote: they grow, and bring forth fruite: thou art neere in their mouth, and farre from their reines.
Inu munawadzala ndipo anamera mizu; amakula ndi kubereka zipatso. Dzina lanu limakhala pakamwa pawo nthawi zonse, koma mitima yawo imakhala kutali ndi Inu.
3 But thou, Lord, knowest me: thou hast seene me, and tried mine heart towarde thee: pull them out like sheepe for the slaughter, and prepare them for the day of slaughter.
Koma Inu Yehova, ine mumandidziwa; mumandiona ndipo mumayesa zolingalira zanga. Akokeni anthu oyipawo ngati nkhosa zokaphedwa! Ayikeni padera mpaka tsiku loti akaphedwe!
4 Howe long shall the lande mourne, and the herbes of euery fielde wither, for the wickednesse of them that dwell therein? the beastes are consumed and the birdes, because they sayd, He wil not see our last ende.
Kodi dziko lidzakhala likulirabe mpaka liti ndipo udzu mʼmunda uliwonse udzakhalabe ofota mpaka liti? Nyama ndi mbalame kulibiretu chifukwa anthu amene amakhalamo ndi oyipa. Iwo amati: “Yehova sangathe kuona ntchito zathu.”
5 If thou hast runne with the footemen and they haue wearied thee, then howe canst thou match thy selfe with horses? and if thou thoughtest thy selfe safe in a peaceable lande, what wilt thou do in the swelling of Iorden?
Yehova anayankha kuti, “Ngati kukutopetsa kuthamanga pamodzi ndi anthu nanga ungapikisane bwanji ndi akavalo? Ngati ukupunthwa ndi kugwa pa malo abwino, udzatha bwanji kuthamanga mʼnkhalango za ku Yorodani?
6 For euen thy brethren, and the house of thy father, euen they haue delt vnfaithfully with thee, and they haue cryed out altogether vpon thee: but beleeue them not, though they speake faire to thee.
Ngakhale abale ako ndi anansi akuwukira, onsewo amvana zokuyimba mlandu. Usawakhulupirire, ngakhale ayankhule zabwino ndi iwe.
7 I haue forsaken mine house: I haue left mine heritage: I haue giuen the dearely beloued of my soule into the hands of her enemies.
“Ine ndawasiya anthu anga; anthu amene ndinawasankha ndawataya. Ndapereka okondedwa anga mʼmanja mwa adani awo.
8 Mine heritage is vnto mee, as a lion in the forest: it crieth out against mee, therefore haue I hated it.
Anthu amene ndinawasankha asanduka ngati mkango wa mʼnkhalango. Akundibangulira mwaukali; nʼchifukwa chake Ine ndikudana nawo.
9 Shall mine heritage bee vnto mee, as a bird of diuers colours? are not the birdes about her, saying, Come, assemble all ye beastes of the fielde, come to eate her?
Anthu anga amene ndinawasankha asanduka ngati mbalame yolusa yamawangamawanga imene akabawi ayizinga. Pitani, kasonkhanitseni nyama zakuthengo. Mubwere nazo kuti zidzadye mbalameyo.
10 Many pastors haue destroyed my vineyarde, and troden my portion vnder foote: of my pleasant portion they haue made a desolate wildernesse.
Abusa ambiri anawononga munda wanga wa mpesa, anapondereza munda wanga; munda wanga wabwino uja anawusandutsa chipululu.
11 They haue layde it waste, and it, being waste, mourneth vnto me: and the whole lande lyeth waste, because no man setteth his minde on it.
Unawusandutsadi chipululu. Ukanali wokhawokha chomwecho ukundilirira Ine. Dziko lonse lasanduka chipululu chifukwa palibe wolisamalira.
12 The destroyers are come vpon all the high places in the wildernesse: for the sworde of the Lord shall deuoure from the one end of the land, euen to the other ende of the lande: no flesh shall haue peace.
Anthu onse owononga abalalikira ku zitunda zonse za mʼchipululu. Yehova watuma ankhondo ake kudzawatha kuyambira kumalire ena a dziko mpaka ku malire enanso a dziko, ndipo palibe amene adzakhale pa mtendere.
13 They haue sowen wheate, and reaped thornes: they were sicke, and had no profite: and they were ashamed of your fruites, because of the fierce wrath of the Lord.
Anthu anafesa tirigu koma anatuta minga; anadzitopetsa kugwira ntchito koma osapeza phindu lililonse. Choncho mudzachita manyazi ndi zokolola zanu chifukwa cha mkwiyo wa Yehova.”
14 Thus sayeth the Lord against all mine euill neighbours, that touch the inheritance, which I haue caused my people Israel to inherite, Beholde, I will plucke them out of their lande, and plucke out the house of Iudah from among them.
“Anthu oyipa oyandikana ndi anthu anga Aisraeli, akuwalanda Aisraeliwo dziko, cholowa chimene ndinawapatsa. Nʼchifukwa chake ndidzawachotsa mʼdziko limenelo, ndipo ndidzachotsa banja la Yuda pakati pawo.
15 And after that I haue plucked them out, I will returne, and haue compassion on them, and will bring againe euery man to his heritage, and euery man to his land.
Komabe nditawachotsa, ndidzawachitiranso chifundo, ndipo ndidzabwezera aliyense cholowa chake ndi dziko lake.
16 And if they will learne the wayes of my people, to sweare by my Name, (The Lord liueth, as they taught my people to sweare by Baal) then shall they be built in the middes of my people.
Ndipo ngati iwo adzaphunzira bwino njira za anthu anga ndi kulumbira mʼdzina langa, namanena kuti, ‘Pali Yehova wamoyo,’ monga iwo anaphunzitsira anthu anga kulumbira mʼdzina la Baala, Ine ndidzawakhazikitsa pakati pa anthu anga.
17 But if they will not obey, then will I vtterly plucke vp, and destroy that nation, sayeth the Lord.
Koma ngati mtundu wina uliwonse sudzamvera, Ine ndidzawuchotsa ndi kuwuwonongeratu,” akutero Yehova.

< Jeremiah 12 >