< Jeremiah 1 >

1 The wordes of Ieremiah the sonne of Hilkiah one of the Priests that were at Anathoth in the lande of Beniamin.
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 To whom the worde of the Lord came in the dayes of Iosiah the sonne of Amon King of Iudah in the thirteenth yeere of his reigne:
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 And also in the dayes of Iehoiakim the sonne of Iosiah King of Iudah vnto the ende of the eleuenth yeere of Zedekiah, the sonne of Iosiah King of Iudah, euen vnto the carying away of Ierusalem captiue in the fift moneth.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 Then the worde of the Lord came vnto me, saying,
Yehova anayankhula nane kuti,
5 Before I formed thee in the wombe, I knewe thee, and before thou camest out of the wombe, I sanctified thee, and ordeined thee to be a Prophet vnto the nations.
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 Then said I, Oh, Lord God, behold, I can not speake, for I am a childe.
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 But the Lord said vnto me, Say not, I am a childe: for thou shalt goe to all that I shall send thee, and whatsoeuer I command thee, shalt thou speake.
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Be not afraide of their faces: for I am with thee to deliuer thee, saith the Lord.
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 Then the Lord stretched out his hand and touched my mouth, and the Lord said vnto me, Beholde, I haue put my wordes in thy mouth.
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 Beholde, this day haue I set thee ouer the nations and ouer the kingdomes to plucke vp, and to roote out, and to destroye and throwe downe, to builde, and to plant.
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 After this the worde of the Lord came vnto me, saying, Ieremiah, what seest thou? And I said, I see a rod of an almonde tree.
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 Then saide the Lord vnto me, Thou hast seene aright: for I will hasten my worde to performe it.
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 Againe the worde of the Lord came vnto me the second time, saying, What seest thou? And I saide, I see a seething pot looking out of the North.
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 Then saide the Lord vnto me, Out of the North shall a plague be spred vpon all the inhabitants of the land.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 For loe, I will call all the families of the kingdomes of the North, saith the Lord, and they shall come, and euery one shall set his throne in the entring of the gates of Ierusalem, and on all the walles thereof rounde about, and in all the cities of Iudah.
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 And I will declare vnto them my iudgements touching all the wickednesse of them that haue forsaken me, and haue burnt incense vnto other gods, and worshipped the workes of their owne handes.
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 Thou therefore trusse vp thy loynes, and arise and speake vnto them all that I commaund thee: be not afraide of their faces, lest I destroy thee before them.
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 For I, beholde, I this day haue made thee a defenced citie, and an yron pillar and walles of brasse against the whole lande, against the Kings of Iudah, and against the princes thereof, against the Priestes thereof and against the people of the lande.
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
19 For they shall fight against thee, but they shall not preuaile against thee: for I am with thee to deliuer thee, sayth the Lord.
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

< Jeremiah 1 >