< Isaiah 8 >

1 Moreover, the Lord sayd vnto me, Take thee a great roll, and write in it with a mans penne, Make speede to the spoyle: haste to the praye.
Yehova anati kwa ine, “Tenga cholembapo chachikulu ndipo ulembepo malemba odziwika bwino: Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.
2 Then I tooke vnto me faithfull witnesses to recorde, Vriah the Priest, and Zechariah the sonne of Ieberechiah.
Ndipo ndidzayitana wansembe Uriya ndi Zekariya mwana wa Yeberekiya kuti akhale mboni zanga zodalirika.”
3 After, I came vnto the Prophetesse, which conceiued, and bare a sonne. Then sayd the Lord to me, Call his name, Mahershalalhash-baz.
Ndipo ine ndinapita kwa mneneri wamkazi, ndipo anakhala woyembekezera nabala mwana wamwamuna. Ndipo Yehova anati kwa ine, “Umutche dzina lakuti, ‘Kusakaza-Kwamsanga Kufunkha-Kofulumira.’
4 For before the childe shall haue knowledge to crye, My father, and my mother, he shall take away the riches of Damascus and the spoyle of Samaria, before the King of Asshur.
Mwanayo asanayambe kudziwa kuyitana kuti, ‘Ababa’ kapena ‘Amama’ chuma cha Damasiko ndi zofunkha za Samariya zidzatengedwa ndi mfumu ya ku Asiriya.”
5 And the Lord spake yet againe vnto me, saying,
Yehova anayankhulanso ndi Ine;
6 Because this people hath refused the waters of Shiloah that runne softly, and reioyce with Rezin, and the sonne of Remaliah,
“Popeza anthu a dziko ili akana madzi anga oyenda mwachifatse a ku Siloamu, ndipo akukondwerera Rezini ndi mwana wa Remaliya,
7 Nowe therefore, beholde, the Lord bringeth vp vpon them the waters of the Riuer mightie and great, euen the King of Asshur with all his glory, and he shall come vp vpon all their riuers, and goe ouer all their banks,
nʼchifukwa chake Ambuye ali pafupi kubweretsa madzi amkokomo a mtsinje wa Yufurate kudzalimbana nawo; mfumu ya ku Asiriya ndi gulu lake lonse lankhondo. Madziwo adzasefukira mʼngalande zake zonse ndi mʼmagombe ake onse.
8 And shall breake into Iudah, and shall ouerflowe and passe through, and shall come vp to the necke, and the stretching out of his wings shall fill the breadth of thy land, O Immanu-el.
Ndipo adzalowa mwamphamvu mʼdziko la Yuda, adzasefukira, adzapitirira mpaka kumuyesa mʼkhosi. Mapiko ake otambasuka adzaphimba dziko lako lonse, iwe Imanueli!”
9 Gather together on heapes, O ye people, and ye shalbe broken in pieces, and hearken all ye of farre countreys: gird your selues, and you shalbe broken in pieces: gird your selues, and you shalbe broken in pieces.
Chitani phokoso lankhondo, inu mitundu ya anthu, ndipo munjenjemere! Tamverani, inu mayiko onse akutali. Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere! Konzekerani nkhondo ndipo munjenjemere!
10 Take counsell together, yet it shall be brought to nought: pronounce a decree, yet shall it not stand: for God is with vs.
Konzani kachitidwe kanu kankhondo, koma simudzaphula kanthu, kambiranani zochita, koma zidzalephereka, pakuti Mulungu ali nafe.
11 For the Lord spake thus to me in taking of mine hand, and taught me, that I should not walke in the way of this people, saying,
Yehova anandiyankhula ine mwamphamvu, ndipo anandichenjeza kuti ndisamayende mʼnjira za anthuwa. Iye anati:
12 Say ye not, A confederacie to all them, to whome this people sayth a confederacie, neither feare you their feare, nor be afrayd of them.
“Usamanene kuti ndi chiwembu, chilichonse chimene anthuwa amati ndi chiwembu usamaope zimene anthuwa amaziopa, ndipo usamachite nazo mantha.
13 Sanctifie the Lord of hostes, and let him be your feare, and let him be your dread,
Yehova Wamphamvuzonse ndiye amene uyenera kumuona kuti ndi woyera, ndiye amene uyenera kumuopa, ndiye amene uyenera kuchita naye mantha,
14 And he shalbe as a Sanctuarie: but as a stumbling stone, and as a rocke to fall vpon, to both the houses of Israel, and as a snare and as a net to the inhabitants of Ierusalem.
ndipo ndiye amene adzakhala malo opatulika; koma kwa anthu a ku Yuda ndi kwa anthu a ku Israeli adzakhala mwala wopunthwitsa, mwala umene umapunthwitsa anthu, thanthwe limene limagwetsa anthu. Ndipo kwa anthu a mu Yerusalemu adzakhala ngati msampha ndi khwekhwe.
15 And many among them shall stumble, and shall fall and shalbe broken and shalbe snared and shalbe taken.
Anthu ambiri adzapunthwapo adzagwa ndi kuthyokathyoka, adzakodwa ndi kugwidwa.”
16 Binde vp the testimonie: seale vp the Law among my disciples.
Manga umboniwu ndipo umate malamulowa pamaso pa ophunzira anga.
17 Therefore I will waite vpon the Lord that hath hid his face from the house of Iaakob, and I wil looke for him.
Ndidzayembekezera Yehova, amene akubisira nkhope yake nyumba ya Yakobo. Ine ndidzakhulupirira Iyeyo.
18 Beholde, I and the children whome the Lord hath giuen me, are as signes and as wonders in Israel, by the Lord of hostes, which dwelleth in mount Zion.
Onani, ine ndili pano pamodzi ndi ana amene Yehova wandipatsa, ndife zizindikiro ndi zodabwitsa kwa Aisraeli zochokera kwa Yehova Wamphamvuzonse, amene amakhala pa Phiri la Ziyoni.
19 And when they shall say vnto you, Enquire at them that haue a spirit of diuination, and at the soothsayers, which whisper and murmure, Should not a people enquire at their God? from the liuing to the dead?
Anthu akakuwuza kuti kafunsire kwa oyankhula ndi mizimu, amene amayankhula monongʼona ndi mongʼungʼudza, kodi anthu sayenera kukafunsira kwa Mulungu wawo? Chifukwa chiyani amafunsira kwa anthu akufa mʼmalo mwa kwa anthu amoyo,
20 To the Law, and to the testimonie, if they speake not according to this worde: it is because there is no light in them.
kuti akalandireko mawu enieni ndi malangizo? Ngati anthuwo sayankhula monga mwa mawu awa, mwa iwo mulibe kuwala.
21 Then he that is afflicted and famished, shall go to and from in it: and when he shalbe hungry, he shall euen freat himselfe, and curse his King and his gods, and shall looke vpward.
Anthu adzayendayenda mʼdziko movutika kwambiri ali ndi njala; pamene afowokeratu ndi njala, iwo adzakwiya kwambiri ndipo adzayangʼana kumwamba ndi kutemberera mfumu yawo ndi Mulungu wawo.
22 And when he shall looke to the earth, beholde trouble, and darkenes, vexation and anguish, and he is driuen to darkenes.
Ndipo akadzayangʼana pa dziko lapansi adzangoona mavuto okhaokha ndi mdima woopsa ndi wodetsa nkhawa, ndipo adzaponyedwa mu mdima wandiweyani.

< Isaiah 8 >