< Isaiah 66 >
1 Thus saith the Lord, The heauen is my throne, and the earth is my footestoole: where is that house that ye will builde vnto me? and where is that place of my rest?
Yehova akuti, “Kumwamba ndi mpando wanga waufumu ndipo dziko lapansi ndilo chopondapo mapazi anga. Tsono nyumba ili kuti yomwe mundimangire, ndipo malo ali kuti amene inu mungandikonzere kuti ndizipumuliramo?
2 For all these things hath mine hand made, and all these things haue bene, sayth the Lord: and to him will I looke, euen to him, that is poore, and of a contrite spirite and trembleth at my wordes.
Kodi si manja anga amene anapanga zinthu zonsezi, motero zonsezi ndi zanga?” Akutero Yehova. “Koma munthu amene ndimakondwera naye ndi uyu: amene ali wodzichepetsa ndi wosweka mtima, ndipo amamvera mawu anga.
3 He that killeth a bullocke, is as if he slewe a man: he that sacrificeth a sheepe, as if he cut off a dogges necke: he that offereth an oblation, as if he offered swines blood: he that remembreth incense, as if he blessed an idole: yea, they haue chosen their owne wayes, and their soule deliteth in their abominations.
Koma aliyense amene amapereka nsembe ngʼombe yayimuna amaphanso munthu, ndipo aliyense amene amapereka mwana wankhosa, amaphanso galu. Aliyense amene amapereka nsembe chopereka cha chakudya amaperekanso magazi a nkhumba. Ndipo amene amafukiza lubani pa guwa lansembe la chikumbutso amapembedzanso fano. Popeza iwo asankha njira zawozawo, ndiponso kusangalatsidwa ndi zonyansa zawo.
4 Therefore will I chuse out their delusions, and I will bring their feare vpon them, because I called, and none woulde answere: I spake and they woulde not heare: but they did euill in my sight, and chose the things which I would not.
Inenso ndawasankhira chilango chowawa ndipo ndidzabweretsa pa iwo zimene amaziopa zija. Pakuti pamene ndinawayitana palibe amene anayankha, pamene ndinayankhula palibe amene anatchera khutu. Anachita zoyipa pamaso panga ndi kusankha kuchita zimene zimandinyansa zija.”
5 Heare the worde of the Lord, all ye that tremble at his worde, Your brethren that hated you, and cast you out for my Names sake, said, Let the Lord be glorified: but he shall appeare to your ioy, and they shall be ashamed.
Imvani mawu a Yehova, inu amene mumanjenjemera ndi mawu ake: “Abale anu amene amakudani, ndi kukuchotsani pakati pawo chifukwa cha dzina langa, amanena kuti, ‘Yehova alemekezeke kuti ife tione chimwemwe chanu!’ Koma ndi iwowo amene adzachite manyazi.
6 A voyce soundeth from the citie, euen a voyce from the Temple, the voyce of the Lord, that recompenseth his enemies fully.
Imvani mfuwu mu mzinda, imvani phokoso mʼNyumba ya Mulungu! Limenelo ndi liwu la Yehova, kulanga adani ake onse.
7 Before she trauailed, she brought foorth: and before her paine came, she was deliuered of a man childe.
“Mzinda uli ngati amayi apakati amene asanayambe kumva zowawa wachira kale; asanayambe kumva ululu, wabala kale mwana wamwamuna.
8 Who hath heard such a thing? who hath seene such things? shall ye earth be brought forth in one day? or shall a nation be borne at once? for assoone as Zion trauailed, she brought foorth her children.
Ndani anamvapo zinthu zoterezi? Ndani anazionapo zinthu zoterezi? Kodi dziko nʼkupangika tsiku limodzi, kapena mtundu wa anthu nʼkubadwa tsiku limodzi? Komatu Ziyoni atangoyamba kumva zowawa nthawi yomweyo anabereka ana ake.
9 Shall I cause to trauaile, and not bring forth? shall I cause to bring forth, and shall be baren, saith thy God?
Kodi Ine ndingangofikitsa amayi apakati mpaka nthawi yake yochira, koma osalola kuti abaledi mwana?” akutero Yehova. “Kodi ndingatseke mimba pa nthawi yoti abeleke?” akutero Mulungu wako.
10 Reioyce ye with Ierusalem, and be gladde with her, all ye that loue her: reioyce for ioy with her, all ye that mourne for her,
“Kondwera nayeni Yerusalemu ndipo musangalale chifukwa cha Iye, inu nonse amene mumakonda Yerusalemu, kondwera nayeni kwambiri, nonse amene mumamulira.
11 That ye may sucke and be satisfied with the brestes of her consolation: that ye may milke out and be delited with ye brightnes of her glorie.
Pakuti mudzagawana naye ulemerero wake ngati kuyamwa ndi kukhuta mkaka wambiri wa mʼmawere a chitonthozo chake.”
12 For thus saith the Lord, Beholde, I will extend peace ouer her like a flood, and the glorie of the Gentiles like a flowing streame: then shall ye sucke, ye shall be borne vpon her sides, and be ioyfull vpon her knees.
Yehova akuti, “Ndidzamupatsa mtendere ngati mtsinje wa madzi, ndiponso chuma cha anthu a mitundu ina ngati mtsinje wosefukira. Mudzakhala ngati mwana woyamwa amene amayi ake amunyamulira pambalipa, kapena kumufungata pa miyendo yake.
13 As one whom his mother comforteth, so will I comfort you, and ye shall be comforted in Ierusalem.
Monga momwe amayi amasangalatsira mwana wawo, moteronso Ine ndidzakusangalatsani; ndipo mudzasangalala chifukwa cha Yerusalemu.”
14 And when ye see this, your hearts shall reioyce, and your bones shall flourish like an herbe: and the hand of the Lord shall be knowen among his seruants, and his indignation against his enemies.
Mukadzaona zimenezi mitima yanu idzakondwera. Mudzabiriwira ngati udzu. Zimenezi zidzakulimbikitsani ndi kukupatsani moyo wamphamvu. Mudzadziwa kuti ndimathandiza amene amanditumikira ndi kuti ndimakwiyira adani anga.
15 For beholde, the Lord will come with fire, and his charets like a whirlewinde, that he may recompence his anger with wrath, and his indignation with the flame of fire.
Taonani, Yehova akubwera ngati moto, ndipo magaleta ake ali ngati kamvuluvulu; Iye adzaonetsa mkwiyo wake nadzalanga adani ake ndi malawi amoto.
16 For the Lord will iudge with fire, and with his sworde all flesh, and the slaine of the Lord shall be many.
Pakuti Yehova adzalanga anthu onse ndi moto ndi lupanga, Yehova adzapha anthu ambiri.
17 They that sanctifie themselues, and purifie themselues in the gardens behinde one tree in the middes eating swines flesh, and such abomination, euen the mouse, shall be consumed together, sayeth the Lord.
Yehova akuti, “Amene amadzipatula ndi kudziyeretsa okha kuti apite ku minda, ali ndi mtsogoleri awo, nʼkumadya nyama ya nkhumba, mbewa ndi zinthu zina zonyansa, onsewa adzafera limodzi.”
18 For I will visite their workes, and their imaginations: for it shall come that I will gather all nations, and tongues, and they shall come, and see my glorie.
“Ndipo Ine, chifukwa cha zochita zawo ndi maganizo awo, ndili pafupi kubwera kudzasonkhanitsa mitundu yonse ya anthu ndi ziyankhulo zonse. Iwo adzabwera ndi kuona ulemerero wanga.
19 And I will set a signe among them, and will send those that escape of them, vnto the nations of Tarshish, Pul, and Lud, and to them that drawe the bowe, to Tubal and Tauan, yles afarre off, that haue not heard my fame, neither haue seene my glorie, and they shall declare my glorie among the Gentiles.
“Ndidzayika chizindikiro pakati pawo, ndipo ndidzatumiza ena mwa iwowa amene anapulumuka kuti apite kwa anthu a mitundu ina inu ku Tarisisi, ku Libiya ndi ku Ludi (akatswiri a mauta) ku Tubala ndi Grisi, ndi ku mayiko akutali a mbali mwa nyanja amene sanamvepo za mbiri yanga kapena kuona ulemerero wanga. Iwo adzalalika za ulemerero wanga pakati pa anthu a mitundu ina.
20 And they shall bring all your brethren for an offering vnto the Lord out of all nations, vpon horses, and in charets, and in horse litters, and vpon mules, and swift beastes, to Ierusalem mine holy Mountaine, saith the Lord, as the children of Israel, offer in a cleane vessell in the House of the Lord.
Ndipo adzabwera nawo abale anu onse ngati mphatso yopereka kwa Yehova kuchokera kwa anthu a mitundu yonse. Iwo adzakwera nawo kupita ku Yerusalemu, phiri langa loyera ku Yerusalemu monga nsembe kwa Yehova, atakwera akavalo, magaleta ndi ngolo, ndi pa abulu ndi ngamira,” akutero Yehova. “Adzabwera nawo ngati momwe Aisraeli amabwerera ndi zopereka zachakudya ku Nyumba ya Yehova mu ziwiya zoyeretsedwa monga mwa mwambo.
21 And I will take of them for Priestes, and for Leuites, saith the Lord.
Ndipo ndidzasankha ena mwa iwonso kukhala ansembe ndi Alevi,” akutero Yehova.
22 For as the newe heauens, and the newe earth which I will make, shall remaine before me, saith the Lord, so shall your seede and your name continue.
“Monga momwe mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano zimene ndidzapanga zidzakhala mpaka muyaya pamaso panga, ndi chonchonso dzina lanu ndi zidzukulu zanu zidzakhalire.” Akutero Yehova.
23 And from moneth to moneth, and from Sabbath to Sabbath shall all flesh come to worship before me, saith the Lord.
“Anthu a mitundu yonse adzabwera kudzandipembedza ku Yerusalemu, pa chikondwerero chilichonse cha pokhala pa mwezi watsopano ndi tsiku la Sabata lililonse,” akutero Yehova.
24 And they shall goe forth, and looke vpon the carkases of the men that haue transgressed against me: for their worme shall not dye, neither shall their fire be quenched, and they shalbe an abhorring vnto all flesh.
“Akamachoka adzaona mitembo ya anthu amene anandiwukira Ine. Mphutsi zawo sizidzafa, kapena moto wawo sudzazimitsidwa. Anthu a mitundu ina yonse powaona adzanyansidwa nawo.”