< Isaiah 58 >

1 Crye aloude, spare not: lift vp thy voyce like a trumpet, and shewe my people their transgression, and to the house of Iaakob, their sinnes.
“Fuwula kwambiri, usaleke. Mawu ako amveke ngati lipenga. Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo; uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
2 Yet they seeke me dayly, and will knowe my wayes, euen as a nation that did righteously, and had not forsaken the statutes of their God: they aske of me the ordinances of iustice: they wil drawe neere vnto God, saying,
Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine; amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna, kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake. Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
3 Wherefore haue we fasted, and thou seest it not? we haue punished our selues, and thou regardest it not. Beholde, in the day of your fast you will seeke your will, and require all your dettes.
Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala kudya pamene Inu simukulabadirapo? Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa pamene Inu simunasamalepo?’” Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani, ndipo mumazunza antchito anu onse.
4 Beholde, ye fast to strife and debate, and to smite with the fist of wickednesse: ye shall not fast as ye doe to day, to make your voyce to be heard aboue.
Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana, mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka. Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
5 Is it such a fast that I haue chosen, that a man should afflict his soule for a day, and to bowe downe his head, as a bull rush, and to lie downe in sackecloth and ashes? wilt thou call this a fasting, or an acceptable day to the Lord?
Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku, kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi? Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo? Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko, tsiku lokondweretsa Yehova?
6 Is not this the fasting, that I haue chosen, to loose the bandes of wickednes, to take off the heauie burdens, and to let the oppressed goe free, and that ye breake euery yoke?
“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna: Kumasula maunyolo ozunzizira anthu ndi kumasula zingwe za goli, kupereka ufulu kwa oponderezedwa ndi kuphwanya goli lililonse?
7 Is it not to deale thy bread to the hungry, and that thou bring the poore that wander, vnto thine house? when thou seest the naked, that thou couer him, and hide not thy selfe from thine owne flesh?
Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu? Osowa ndi ongoyendayenda, kodi mwawapatsa malo ogona? Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
8 Then shall thy light breake foorth as the morning, and thine health shall grow speedily: thy righteousnes shall goe before thee, and the glorie of the Lord shall embrace thee.
Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha, ndipo mabala anu adzachira msangamsanga; chilungamo chanu chidzakutsogolerani ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
9 Then shalt thou call, and the Lord shall answere: thou shalt cry and hee shall say, Here I am: if thou take away from the mids of thee the yoke, the putting foorth of the finger, and wicked speaking:
Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani; mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano. “Ngati muleka kuzunza anzanu, ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
10 If thou powre out thy soule to the hungrie, and refresh the troubled soule: then shall thy light spring out in the darkenes, and thy darkenes shalbe as the noone day.
Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala, ndi kuthandiza anthu oponderezedwa, pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima, ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
11 And the Lord shall guide thee continually, and satisfie thy soule in drought, and make fat thy bones: and thou shalt be like a watred garden, and like a spring of water, whose waters faile not.
Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse; adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa ndipo adzalimbitsa matupi anu. Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri, ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
12 And they shalbe of thee, that shall builde the olde waste places: thou shalt rayse vp the foundations for many generations, and thou shalt be called the repairer of the breach and the restorer of the pathes to dwell in.
Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali, ndipo adzamanganso pa maziko akalekale; inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka. Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.
13 If thou turne away thy foote from the Sabbath, from doing thy will on mine holy day, and call the Sabbath a delite, to consecrate it, as glorious to the Lord, and shalt honour him, not doing thine owne wayes, nor seeking thine owne will, nor speaking a vaine word,
“Muzisunga osaphwanya Sabata; musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika, tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo. Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza posayenda mʼnjira zanu, kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
14 Then shalt thou delite in the Lord, and I wil cause thee to mount vpon the hie places of the earth, and feede thee with the heritage of Iaakob thy father: for the mouth of ye Lord hath spoken it.
mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova, ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi. Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.” Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.

< Isaiah 58 >