< Isaiah 56 >

1 Thus saith the Lord, Keepe iudgement and doe iustice: for my saluation is at hand to come, and my righteousnes to be reueiled.
Yehova akuti, “Chitani chilungamo ndi zinthu zabwino, chifukwa chipulumutso changa chili pafupi ndipo ndidzakuwombolani posachedwapa.
2 Blessed is the man that doeth this, and the sonne of man which layeth holde on it: hee that keepeth the Sabbath and polluteth it not, and keepeth his hand from doing any euill.
Ndi wodala munthu amene amachita zimenezi, munthu amene amalimbika kuzichita, amene amasunga Sabata osaliyipitsa, ndipo amadziletsa kuchita zoyipa.”
3 And let not the sonne of the stranger, which is ioyned to the Lord, speake and say, The Lord hath surely separate me from his people: neither let the Eunuch say, Beholde, I am a drye tree.
Mlendo amene waphatikana ndi Yehova asanene kuti, “Ndithu Yehova wandichotsa pakati pa anthu ake.” Ndipo munthu wofulidwa asanene kuti, “Ine ndine mtengo wowuma basi.”
4 For thus saith the Lord vnto the Eunuches, that keepe my Sabbaths, and chuse the thing that pleaseth me, and take holde of my couenant,
Popeza Yehova akuti, “Wofulidwa amene amasunga masabata anga, nachita zokomera Ine ndi kusunga pangano langa,
5 Euen vnto them wil I giue in mine House and within my walles, a place and a name better then of the sonnes and of the daughters: I will giue them an euerlasting name, that shall not be put out.
ndidzawapatsa dzina ndi mbiri yabwino mʼkati mwa Nyumba yanga ndi makoma ake, kuposa kukhala ndi ana aamuna ndi aakazi. Ndidzawapatsa dzina labwino, losatha ndi losayiwalika.”
6 Also the strangers that cleaue vnto the Lord, to serue him, and to loue the Name of the Lord, and to be his seruants: euery one that keepeth the Sabbath, and polluteth it not and imbraceth my couenant,
Yehova akuti, “Alendo amene amadziphatika kwa Yehova, motero kuti amamutumikira Iye, amakonda dzina la Yehova, amamugwirira ntchito, komanso kusunga Sabata osaliyipitsa ndi kusunga bwino pangano langa,
7 Them wil I bring also to mine holy mountaine, and make them ioyfull in mine House of prayer: their burnt offerings and their sacrifices shall be accepted vpon mine altar: for mine House shall be called an house of prayer for all people.
amenewa Ine ndidzawafikitsa ku phiri langa lopatulika, ndidzawapatsa chimwemwe mʼnyumba yanga ya mapemphero. Zopereka zawo zopsereza ndi nsembe zawo ndidzazilandira pa guwa langa la nsembe. Paja nyumba yanga idzatchedwa nyumba ya mapemphero ya anthu a mitundu yonse.”
8 The Lord God sayth, which gathereth the scattered of Israel, Yet wil I gather to them those that are to be gathered to them.
Ambuye Yehova, amene amasonkhanitsa Aisraeli onse ali ku ukapolo akunena kuti, “Ndidzasonkhanitsano anthu ena kuwonjezera amene anasonkhana kale.”
9 All ye beastes of the fielde, come to deuoure, euen all ye beastes of the forest.
Bwerani, inu zirombo zonse zakuthengo, inu nonse zirombo zamʼnkhalango bwerani mudzadye!
10 Their watchmen are all blinde: they haue no knowledge: they are all dumme dogs: they can not barke: they lie and sleepe and delite in sleeping.
Atsogoleri onse a Israeli ndi akhungu, onse ndi opanda nzeru; onse ndi agalu opanda mawu, samatha kuwuwa: amagona pansi nʼkumalota amakonda kugona tulo.
11 And these griedy dogs can neuer haue ynough: and these shepheards cannot vnderstand: for they all looke to their owne way, euery one for his aduantage, and for his owne purpose.
Ali ngati agalu amene ali ndi njala yayikulu; sakhuta konse. Abusa nawonso samvetsa zinthu; onse amachita monga akufunira, aliyense amafunafuna zomupindulitsa iye mwini.
12 Come, I wil bring wine, and we wil fill our selues with strong drinke, and to morowe shalbe as this day, and much more abundant.
Aliyense amafuwulira mnzake kuti, “Bwera, tiye timwe vinyo! Tiyeni timwe mowa mpaka kukhuta! Mawa lidzakhala ngati leroli, kapena kuposa lero lino.”

< Isaiah 56 >