< Isaiah 5 >

1 Now will I sing to my beloued a song of my beloued to his vineyarde, My beloued had a vineyarde in a very fruitefull hill,
Ndidzamuyimbira bwenzi langa nyimbo yokamba za munda wake wa mpesa: Wokondedwa wanga anali ndi munda wamphesa pa phiri la nthaka yachonde.
2 And hee hedged it, and gathered out the stones of it, and he planted it with the best plants, and hee builte a towre in the middes thereof, and made a wine presse therein: then hee looked that it should bring foorth grapes: but it brought foorth wilde grapes.
Anatipula nachotsa miyala yonse ndipo anawokamo mipesa yabwino kwambiri. Anamanga nsanja yolondera pakati pa mundawo ndipo anasemanso mopsinyira mphesa mʼmundamo. Ndipo iye anayembekezera kuti mundawo udzabala mphesa zabwino, koma ayi, unabala mphesa zosadya.
3 Now therefore, O inhabitants of Ierusalem and men of Iudah, iudge, I pray you, betweene me, and my vineyarde.
“Tsopano, inu amene mumakhala mu Yerusalemu ndi inu anthu a ku Yuda, weruzani pakati pa ine ndi munda wanga wa mpesawu.
4 What coulde I haue done any more to my vineyard that I haue not done vnto it? why haue I looked that it should bring foorth grapes, and it bringeth foorth wilde grapes?
Kodi nʼchiyaninso china chimene ndikanachitira munda wanga wa mpesa kupambana chomwe ndawuchitira kale? Pamene ndinkayembekezera kuti udzabala mphesa zabwino, bwanji unabala mphesa zosadya?
5 And nowe I will tell you what I will do to my vineyarde: I will take away the hedge thereof, and it shall be eaten vp: I will breake the wall thereof, and it shall be troden downe:
Tsopano ndikuwuzani chimene ndidzawuchitire munda wanga wa mpesa: ndidzachotsa mpanda wake, ndipo mundawo udzawonongeka; ndidzagwetsa khoma lake, ndipo nyama zidzapondapondamo.
6 And I will laye it waste: it shall not be cut, nor digged, but briers, and thornes shall growe vp: I will also commande the cloudes that they raine no raine vpon it.
Ndidzawusandutsa tsala, udzakhala wosatengulira ndi wosalimira ndipo mudzamera mkandankhuku ndi minga ina. Ndidzalamula mitambo kuti isagwetse mvula pa mundapo.”
7 Surely the vineyard of the Lord of hostes is the house of Israel, and the men of Iudah are his pleasant plant, and hee looked for iudgement, but beholde oppression: for righteousnesse, but beholde a crying.
Munda wamphesa wa Yehova Wamphamvuzonse ndi Aisraeli, ndipo anthu a ku Yuda ndiwo minda yake yomukondweretsa. Ndipo Iye ankayembekezera chiweruzo cholungama, mʼmalo mwake anaona kuphana; mʼmalo mwa chilungamo Iye anamva kulira kwa anthu ozunzika.
8 Woe vnto them that ioyne house to house, and laye fielde to fielde, till there bee no place, that ye may be placed by your selues in the mids of the earth.
Tsoka kwa inu amene mumangokhalira kulumikiza nyumba, ndipo mumangokhalira kuwonjezera minda, mpaka mutalanda malo onse kuti muzikhalamo nokha mʼdzikomo.
9 This is in mine cares, saith the Lord of hostes. Surely many houses shall be desolate, euen great, and faire without inhabitant.
Yehova Wamphamvuzonse wayankhula ine ndikumva kuti, “Ndithudi nyumba zambirizo zidzasanduka mabwinja, nyumba zazikulu zokongolazo zidzakhala zopanda anthu.
10 For ten acres of vines shall yelde one bath, and the seede of an homer shall yelde an ephah.
Munda wamphesa wa maekala khumi udzatulutsa vinyo wodzaza mbiya imodzi, kufesa madengu khumi a mbewu, zokolola zake zidzangodzaza dengu limodzi.”
11 Wo vnto them, that rise vp early to follow drunkennes, and to them that continue vntill night, till the wine doe inflame them.
Tsoka kwa iwo amene amadzuka mmamawa nathamangira chakumwa choledzeretsa, amene amamwa mpaka usiku kufikira ataledzera kotheratu.
12 And the harpe and viole, timbrel, and pipe, and wine are in their feastes: but they regard not the worke of the Lord, neither consider the worke of his handes.
Pa maphwando awo pamakhala azeze, apangwe, matambolini, zitoliro ndi vinyo, ndipo sasamala ntchito za Yehova, salemekeza ntchito za manja ake.
13 Therefore my people is gone into captiuitie, because they had no knowledge, and the glorie thereof are men famished, and the multitude thereof is dried vp with thirst.
Motero anthu anga adzatengedwa ukapolo chifukwa cha kusamvetsa zinthu; atsogoleri awo olemekezeka adzafa ndi njala, ndipo anthu wamba ochuluka adzafa ndi ludzu.
14 Therefore hell hath inlarged it selfe, and hath opened his mouth, without measure, and their glorie, and their multitude, and their pompe, and hee that reioyceth among them, shall descend into it. (Sheol h7585)
Nʼchifukwa chake ku manda sikukhuta ndipo kwayasama kwambiri kukamwa kwake; mʼmandamo mudzagweranso anthu otchuka a mu Yerusalemu pamodzi ndi anthu wamba ochuluka; adzagweramo ali wowowo, nʼkuledzera kwawoko. (Sheol h7585)
15 And man shalbe brought downe, and man shalbe humbled, euen the eyes of the proude shalbe humbled.
Ndipo munthu aliyense adzatsitsidwa, anthu onse adzachepetsedwa, anthu odzikuza adzachita manyazi.
16 And the Lord of hostes shalbe exalted in iudgement, and the holy God shalbe sanctified in iustice.
Koma Yehova Wamphamvuzonse adzalemekezedwa chifukwa cha chiweruzo chake cholungama. Ndipo Mulungu woyera adzadzionetsa kuti ndi woyera pochita chilungamo chake.
17 Then shall the lambes feede after their maner, and the strangers shall eate the desolate places of the fat.
Tsono nkhosa zidzadya pamenepo ngati pabusa pawo; ana ankhosa adzadya mʼmabwinja a anthu olemera.
18 Woe vnto them, that draw iniquitie with cordes of vanitie, and sinne, as with cart ropes:
Tsoka kwa amene amadzikokera tchimo ndi zingwe zachinyengo, ndipo amadzikokera zoyipa ndi zingwe zokokera ngolo,
19 Which say, Let him make speede: let him hasten his worke, that wee may see it: and let the counsell of the holy one of Israel draw neere and come, that we may knowe it.
amene amanena kuti, “Yehova afulumire, agwire ntchito yake mwamsanga kuti ntchitoyo tiyione. Ntchito zionekere, zimene Woyerayo wa Israeli akufuna kuchita, zichitike kuti tizione.”
20 Woe vnto them that speake good of euill, and euill of good, which put darkenes for light, and light for darkenes, that put bitter for sweete, and sweete for sowre.
Tsoka kwa amene zoyipa amaziyesa zabwino ndipo zabwino amaziyesa zoyipa, amene mdima amawuyesa kuwala ndipo kuwala amakuyesa mdima, amene zowawasa amaziyesa zotsekemera ndipo zotsekemera amaziyesa zowawasa.
21 Woe vnto them that are wise in their owne eyes, and prudent in their owne sight.
Tsoka kwa amene amadziona ngati anzeru ndipo amadziyesa ochenjera.
22 Wo vnto them that are mightie to drinke wine, and to them that are strong to powre in strong drinke:
Tsoka kwa zidakwa zimene zimayika mtima pa vinyo ndipo ndi akatswiri posakaniza zakumwa,
23 Which iustifie the wicked for a rewarde, and take away the righteousnesse of the righteous from him.
amene amamasula olakwa chifukwa cha chiphuphu koma amayipitsa mlandu wa munthu wosalakwa.
24 Therefore as the flame of fire deuoureth the stubble, and as the chaffe is cosumed of the flame: so their roote shalbe as rottennesse, and their bud shall rise vp like dust, because they haue cast off the Lawe of the Lord of hostes, and contemned the word of the holy one of Israel.
Nʼchifukwa chake monga momwe moto umawonongera chiputu ndipo monga momwe udzu wowuma umapsera mʼmalawi a moto, momwemonso mizu yawo idzawola ndipo maluwa awo adzafota ndi kuwuluka ngati fumbi; chifukwa akana malamulo a Yehova Wamphamvuzonse, ndipo anyoza mawu a Woyerayo wa Israeli.
25 Therefore is the wrath of the Lord kindled against his people, and hee hath stretched out his hand vpon them, and hath smitten them that the mountaines did tremble: and their carkases were torne in the middes of the streetes, and for all this his wrath was not turned away, but his hande was stretched out still.
Nʼchifukwa chake mkwiyo wa Yehova wayakira anthu ake; watambasula dzanja lake pa anthuwo ndipo akuwakantha Mapiri akugwedezeka, ndipo mitembo ya anthu yangoti mbwee mʼmisewu ngati zinyalala. Komabe ngakhale watero, mkwiyo wake sunaleke, dzanja lake likanali chitambasulire;
26 And he will lift vp a signe vnto the nations a farre, and wil hisse vnto them from the ende of the earth: and beholde, they shall come hastily with speede.
Yehova wakweza mbendera kuyitana mtundu wa anthu akutali, akuyitana anthuwo ndi likhweru kuti abwere kuchokera ku mathero a dziko lapansi. Awo akubwera, akubweradi mofulumira kwambiri!
27 None shall faint nor fall among them: none shall slumber nor sleepe, neither shall the girdle of his loynes be loosed, nor the latchet of his shooes be broken:
Palibe ndi mmodzi yemwe amene akutopa kapena kupunthwa, palibe amene akusinza kapena kugona; palibe lamba wa mʼchiwuno amene akumasuka, palibe chingwe cha nsapato chimene chaduka.
28 Whose arrowes shall be sharpe, and all his bowes bent: his horse hoofes shall be thought like flint, and his wheeles like a whirlewinde.
Mivi yawo ndi yakuthwa, mauta awo onse ndi okoka, ziboda za akavalo awo nʼzolimba ngati mwala wansagalabwi, magaleta awo ndi aliwiro ngati kamvuluvulu.
29 His roaring shalbe like a lyon, and he shall roare like lyons whelpes: they shall roare, and lay holde of the praye: they shall take it away, and none shall deliuer it.
Kufuwula kwawo kuli ngati kubangula kwa mkango, amabangula ngati misona ya mkango; imadzuma pamene ikugwira nyama ndipo imapita nayo popanda ndi mmodzi yemwe woyipulumutsa.
30 And in that day they shall roare vpon them, as the roaring of the sea: and if they looke vnto the earth, beholde darkenesse, and sorowe, and the light shalbe darkened in their skie.
Tsiku limenelo mitundu ya anthu idzabangula ngati mkokomo wa madzi a mʼnyanja. Ndipo wina akakayangʼana dzikolo adzangoona mdima ndi zovuta; ngakhale kuwala kudzasanduka mdima chifukwa cha mitambo.

< Isaiah 5 >