< Isaiah 45 >
1 Thus sayeth the Lord vnto Cyrus his anointed, whose right hand I haue holden to subdue nations before him: therefore will I weaken the loynes of Kings and open the doores before him, and the gates shall not be shut:
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 I will goe before thee and make the crooked streight: I will breake the brasen doores, and burst the yron barres.
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 And I will giue thee the treasures of darkenesse, and the things hid in secret places, that thou maist know that I am the Lord which call thee by thy name, euen the God of Israel.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 For Iaakob my seruants sake, and Israel mine elect, I will euen call thee by thy name and name thee, though thou hast not knowen me.
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 I am the Lord and there is none other: there is no God besides me: I girded thee though thou hast not knowen me,
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 That they may knowe from the rising of the sunne and from the West, that there is none besides me. I am the Lord, and there is none other.
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 I forme the light and create darkenes: I make peace and create euill: I the Lord doe all these things.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Ye heauens, send the dewe from aboue, and let the cloudes droppe downe righteousnesse: let the earth open, and let saluation and iustice growe foorth: let it bring them foorth together: I the Lord haue created him.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Woe be vnto him that striueth with his maker, the potsherd with the potsherds of the earth: shall the clay say to him that facioneth it, What makest thou? or thy worke, It hath none hands?
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Woe vnto him that sayeth to his father, What hast thou begotten? or to his mother, What hast thou brought foorth?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Thus saith the Lord, the holy one of Israel, and his maker, Aske me of things to come concerning my sonnes, and concerning the workes of mine hands: commande you me.
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 I haue made the earth, and created man vpon it: I, whose hands haue spred out the heauens, I haue euen commanded all their armie.
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 I haue raised him vp in righteousnesse, and I will direct all his wayes: he shall build my citie, and he shall let goe my captiues, not for price nor rewarde, saith the Lord of hostes.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Thus sayth the Lord, The labour of Egypt, and the marchandise of Ethiopia, and of the Sabeans, men of stature shall come vnto thee, and they shall be thine: they shall follow thee, and shall goe in chaines: they shall fall downe before thee, and make supplication vnto thee, saying, Surely God is in thee, and there is none other God besides.
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Verely thou, O God, hidest thy selfe, O God, the Sauiour of Israel.
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 All they shalbe ashamed and also confounded: they shall goe to confusion together, that are the makers of images.
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 But Israel shall be saued in the Lord, with an euerlasting saluation: ye shall not be ashamed nor confounded worlde without ende.
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 For thus saith the Lord (that created heauen, God himselfe, that formed the earth, and made it: he that prepared it, he created it not in vaine: he formed it to be inhabited) I am the Lord, and there is none other.
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 I haue not spoken in secrete, neither in a place of darkenes in the earth: I saide not in vaine vnto the seede of Iaakob, Seeke you me: I the Lord doe speake righteousnesse, and declare righteous things.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Assemble your selues, and come: drawe neere together, ye abiect of the Gentiles: they haue no knowledge, that set vp the wood of their idole, and pray vnto a god, that cannot saue them.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Tell ye and bring them, and let them take counsell together, who hath declared this from the beginning? or hath tolde it of olde? Haue not I the Lord? and there is none other God beside me, a iust God, and a Sauiour: there is none beside me.
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Looke vnto me, and ye shall be saued: all the endes of the earth shall be saued: for I am God, and there is none other.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 I haue sworne by my selfe: the worde is gone out of my mouth in righteousnesse, and shall not returne, That euery knee shall bowe vnto me, and euery tongue shall sweare by me.
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 Surely he shall say, In the Lord haue I righteousnesse and strength: he shall come vnto him, and all that prouoke him, shall be ashamed.
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 The whole seede of Israel shall be iustified, and glorie in the Lord.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.