< Isaiah 40 >

1 Comfort ye, comfort ye my people, will your God say.
Atonthozeni, atonthozeni anthu anga, akutero Mulungu wanu.
2 Speake comfortably to Ierusalem, and crye vnto her, that her warrefare is accomplished, that her iniquitie is pardoned: for she hath receiued of the Lords hand double for all her sinnes.
Ayankhuleni moleza mtima anthu a ku Yerusalemu ndipo muwawuzitse kuti nthawi ya ukapolo wawo yatha, tchimo lawo lakhululukidwa. Ndawalanga mokwanira chifukwa cha machimo awo onse.
3 A voyce cryeth in the wildernesse, Prepare ye the way of the Lord: make streight in the desert a path for our God.
Mawu a wofuwula mʼchipululu akuti, “Konzani njira ya Yehova mʼchipululu; wongolani njira zake; msewu owongoka wa Mulungu wathu mʼdziko lopanda kanthu.
4 Euery valley shall be exalted, and euery mountaine and hill shall be made lowe: and the crooked shalbe streight, and the rough places plaine.
Chigwa chilichonse achidzaze. Phiri lililonse ndi chitunda chilichonse azitsitse; Dziko lokumbikakumbika alisalaze, malo azitundazitunda awasandutse zidikha.
5 And the glory of the Lord shalbe reueiled, and all flesh shall see it together: for the mouth of the Lord hath spoken it.
Ndipo ulemerero wa Yehova udzaonekera, ndipo mitundu yonse ya anthu idzawuona, pakuti wanena zimenezi ndi Yehova.”
6 A voyce saide, Crie. And he saide, What shall I crie? All flesh is grasse, and all the grace thereof is as the floure of the fielde.
Wina ananena kuti, “Lengeza.” Ndipo ine ndinati, “Kodi ndifuwule chiyani? “Pakuti anthu onse ali ngati udzu ndipo kukongola kwawo kuli ngati maluwa akuthengo.
7 The grasse withereth, the floure fadeth, because the Spirite of the Lord bloweth vpon it: surely the people is grasse.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota chifukwa cha kuwomba kwa mpweya wa Yehova.” Mawu aja anatinso, “Ndithudi anthu sasiyana ndi udzu.
8 The grasse withereth, the floure fadeth: but the worde of our God shall stand for euer.
Udzu umanyala ndipo maluwa amafota, koma mawu a Mulungu wathu adzakhalapo mpaka muyaya.”
9 O Zion, that bringest good tidings, get thee vp into the hie mountaine: O Ierusalem, that bringest good tidings, lift vp thy voyce with strength: lift it vp, be not afraide: say vnto the cities of Iudah, Beholde your God.
Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Ziyoni, kwera pa phiri lalitali. Iwe amene ukulengeza nkhani yabwino ku Yerusalemu, fuwula kwambiri, kweza mawu, usachite mantha; uza mizinda ya ku Yuda kuti, “Mulungu wanu akubwera!”
10 Beholde, the Lord God will come with power, and his arme shall rule for him: beholde, his rewarde is with him, and his worke before him,
Taonani, Ambuye Yehova akubwera mwamphamvu, ndipo dzanja lake likulamulira, taonani akubwera ndi mphotho yake watsogoza zofunkha zako za ku nkhondo.
11 He shall feede his flocke like a shepheard: he shall gather the lambes with his arme, and cary them in his bosome, and shall guide them with young.
Iye adzasamalira nkhosa zake ngati mʼbusa: Iye adzasonkhanitsa ana ankhosa aakazi mʼmanja mwake ndipo Iye akuwanyamula pachifuwa chake ndi kutsogolera bwinobwino nkhosa zoyamwitsa.
12 Who hath measured the waters in his fist? and counted heauen with the spanne, and comprehended the dust of the earth in a measure? and weighed ye mountaines in a weight, and the hilles in a balance?
Kodi ndani akhoza kuyeza kuchuluka kwa madzi a mʼnyanja ndi chikhatho chake, kapena kuyeza kutalika kwa mlengalenga ndi dzanja lake? Ndani akhoza kuyeza dothi lonse la dziko lapansi mʼdengu, kapena kuyeza kulemera kwa mapiri ndi zitunda ndi pasikelo?
13 Who hath instructed ye Spirit of the Lord? or was his counseler or taught him?
Ndani anapereka malangizo kwa Mzimu wa Yehova kapena kumuphunzitsa Iye monga phungu wake?
14 Of whom tooke he counsell, and who instructed him and taught him in the way of iudgement? or taught him knowledge, and shewed vnto him the way of vnderstanding?
Kodi Yehova anapemphapo nzeru kwa yani kuti akhale wopenya, kapena kuti aphunzire njira yoyenera ndi nzeru? Iye anapempha nzeru kwa yani ndi njira ya kumvetsa zinthu?
15 Beholde, the nations are as a drop of a bucket, and are counted as the dust of the balance: beholde, he taketh away the yles as a litle dust.
Ndithudi mitundu ya anthu ili ngati dontho la madzi ochoka mu mtsuko. Iwo akungoyesedwa ngati fumbi chabe pa sikelo; mʼmanja mwa Yehova zilumba nʼzopepuka ngati fumbi.
16 And Lebanon is not sufficient for fire, nor the beastes thereof sufficient for a burnt offering.
Nkhalango ya ku Lebanoni singakwanire nkhuni zosonkhera moto pa guwa lansembe, ngakhale nyama zake sizingakwanire kupereka nsembe zopsereza.
17 All nations before him are as nothing, and they are counted to him, lesse then nothing, and vanitie.
Pamaso pa Yehova mitundu yonse ya anthu ili ngati chinthu chopandapake; Iye amayiwerengera ngati chinthu chopanda phindu ndi cha chabechabe.
18 To whom then wil ye liken God? or what similitude will ye set vp vnto him?
Kodi tsono Mulungu mungamuyerekeze ndi yani? Kodi mungamufanizire ndi chiyani?
19 The workeman melteth an image, or the goldsmith beateth it out in golde, or the goldesmith maketh siluer plates.
Likakhala fano, mʼmisiri ndiye analipanga ndipo mʼmisiri wa golide amalikuta ndi golide naliveka mkanda wasiliva.
20 Doeth not the poore chuse out a tree that will not rot, for an oblation? he seeketh also vnto him a cunning workeman, to prepare an image, that shall not be moued.
Mʼmphawi amene sangathe kupeza ngakhale chopereka nsembe chotere amasankha mtengo umene sudzawola, nafunafuna mʼmisiri waluso woti amupangire fano limene silingasunthike.
21 Know ye nothing? haue ye not heard it? hath it not bene tolde you from the beginning? haue ye not vnderstand it by the foundation of the earth?
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Kodi sanakuwuzeni kuyambira pachiyambi pomwe? Kodi simunamvetsetse chiyambire cha dziko lapansi?
22 He sitteth vpon the circle of the earth, and the inhabitants thereof are as grashoppers, hee stretcheth out ye heauens, as a curtaine, and spreadeth them out, as a tent to dwell in.
Yehova amene amakhala pa mpando wake waufumu kumwamba ndiye analenga dziko lapansi, Iye amaona anthu a dziko lapansi ngati ziwala. Ndipo anafunyulula mlengalenga ngati nsalu yotchinga, nayikunga ngati tenti yokhalamo.
23 He bringeth the princes to nothing, and maketh the iudges of the earth, as vanitie,
Amatsitsa pansi mafumu amphamvu nasandutsa olamula a dziko kukhala achabechabe.
24 As though they were not plated, as though they were not sowen, as though their stocke tooke no roote in the earth: for he did euen blow vpon them, and they withered, and the whirlewinde will take them away as stubble.
Inde, iwo ali ngati mbewu zimene zangodzalidwa kumene kapena kufesedwa chapompano, ndi kungoyamba kuzika mizu kumene ndi pamene mphepo imawombapo nʼkuziwumitsa ndipo kamvuluvulu amaziwulutsa ngati mankhusu.
25 To whom nowe will ye liken me, that I should be like him, saith the Holy one?
Woyera uja akuti, “Kodi mudzandiyerekeza Ine ndi yani? Kapena kodi alipo wofanana nane?”
26 Lift vp your eyes on hie, and beholde who hath created these things, and bringeth out their armies by nomber, and calleth them all by names? by the greatnesse of his power and mightie strength nothing faileth.
Tayangʼanani mlengalenga ndipo onani. Kodi ndani analenga zonsezi mukuzionazi? Yehova ndiye amene amazitsogolera ngati gulu la ankhondo, nayitana iliyonse ndi dzina lake. Ndipo popeza Iye ali ndi nyonga zambiri, palibe ndi imodzi yomwe imene inasowapo.
27 Why sayest thou, O Iaakob, and speakest O Israel, My way is hid from the Lord, and my iudgement is passed ouer of my God?
Iwe Yakobo, chifukwa chiyani umanena ndi kumadandaula iwe Israeli, kuti, “Yehova sakudziwa mavuto anga, Mulungu wanga sakusamala zomwe zikundichitikira ine?”
28 Knowest thou not? or hast thou not heard, that the euerlasting God, the Lord hath created the endes of the earth? he neither fainteth, nor is wearie: there is no searching of his vnderstanding.
Kodi simukudziwa? Kodi simunamve? Yehova ndiye Mulungu wamuyaya, ndiyenso Mlengi wa dziko lonse lapansi. Iye sadzatopa kapena kufowoka ndipo palibe amene angadziwe maganizo ake.
29 But he giueth strength vnto him that fainteth, and vnto him that hath no strength, he encreaseth power.
Iye amalimbitsa ofowoka ndipo otopa amawawonjezera mphamvu.
30 Euen the yong men shall faint, and be wearie, and the yong men shall stumble and fall.
Ngakhale achinyamata amalefuka ndi kufowoka, ndipo achinyamata amapunthwa ndi kugwa;
31 But they that waite vpon the Lord, shall renue their strength: they shall lift vp the wings as the eagles: they shall runne, and not be wearie, and they shall walke and not faint.
koma iwo amene amakhulupirira Yehova adzalandira mphamvu zatsopano. Adzawuluka ngati chiwombankhanga; adzathamanga koma sadzalefuka, adzayenda koma sadzatopa konse.

< Isaiah 40 >