< Isaiah 39 >
1 At the same time, Merodach Baladan, the sonne of Baladan, King of Babel, sent letters, and a present to Hezekiah: for he had heard that he had bene sicke, and was recouered.
Nthawi imeneyo Merodaki-Baladani, mwana wa Baladani mfumu ya ku Babuloni anatumiza nthumwi kwa Hezekiya nawapatsira makalata ndi mphatso, pakuti anamva za kudwala kwake ndi kuti anachira.
2 And Hezekiah was glad of them, and shewed them the house of the treasures, the siluer, and the golde, and the spices, and the precious ointment, and all the house of his armour, and all that was founde in his treasures: there was nothing in his house, nor in all his kingdome that Hezekiah shewed them not.
Hezekiya anawalandira mwasangala ndipo anawaonetsa zonse zimene zinali mʼnyumba zake zosungiramo siliva, golide, zokometsera zakudya, mafuta abwino kwambiri, zida zonse zankhondo ndiponso zonse zimene zinkapezeka mʼnyumba zake zosungiramo chuma. Panalibe kanthu kalikonse ka mʼnyumba yaufumu kapena mu ufumu wake onse kamene sanawaonetse.
3 Then came Isaiah the Prophet vnto King Hezekiah, and said vnto him, What said these men? and from whence came they to thee? And Hezekiah saide, They are come from a farre countrey vnto me, from Babel.
Tsono mneneri Yesaya anapita kwa mfumu Hezekiya ndipo anamufunsa kuti, “Kodi anthu aja anakuwuzani chiyani, ndipo anachokera kuti?” Hezekiya anayankha kuti, “Anachokera ku dziko lakutali, ku Babuloni.”
4 Then saide he, What haue they seene in thine house? And Hezekiah answered, All that is in mine house haue they seene: there is nothing among my treasures, that I haue not shewed them.
Mneneri anafunsanso kuti, “Kodi mʼnyumba yanu yaufumu anaonamo chiyani?” Hezekiya anati, “Anaona chilichonse cha mʼnyumba yanga yaufumu. Palibe ndi chimodzi chomwe za mʼnyumba yosungiramo chuma changa chimene sindinawaonetse.”
5 And Isaiah saide to Hezekiah, Heare the worde of the Lord of hostes,
Pamenepo Yesaya anati kwa Hezekiya, “Imvani mawu a Yehova Wamphamvuzonse:
6 Beholde, the dayes come, that all that is in thine house, and which thy fathers haue layed vp in store vntill this day, shall be caried to Babel: nothing shall be left, sayeth the Lord.
Yehova akuti, nthawi idzafika ndithu pamene zonse za mʼnyumba mwanu ndi zonse zimene makolo anu anazisonkhanitsa mpaka lero lino, zidzatengedwa kupita nazo ku Babuloni. Sipadzatsalapo ndi kanthu kamodzi komwe.
7 And of thy sonnes, that shall proceede out of thee, and which thou shalt beget, shall they take away, and they shall be eunuches in the palace of the King of Babel.
Ndipo ena mwa ana anu, obala inu amene adzatengedwanso, ndipo adzawasandutsa adindo ofulidwa mʼnyumba ya mfumu ya ku Babuloni.”
8 Then said Hezekiah to Isaiah, The worde of the Lord is good, which thou hast spoken: and he saide, Yet let there be peace, and trueth in my dayes.
Hezekiya anayankha kuti, “Mawu a Yehova amene mwayankhula ndi abwino.” Ponena izi iye ankaganiza kuti, “Padzakhala mtendere ndi chitetezo masiku a moyo wanga onse.”