< Isaiah 38 >
1 About that time was Hezekiah sicke vnto the death, and the Prophet Isaiah sonne of Amoz came vnto him, and sayd vnto him, Thus sayth the Lord, Put thine house in an order, for thou shalt dye, and not liue.
Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
2 Then Hezekiah turned his face to the wall, and prayed to the Lord,
Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
3 And saide, I beseeche thee, Lord, remember nowe howe I haue walked before thee in trueth, and with a perfite heart, and haue done that which is good in thy sight: and Hezekiah wept sore.
“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
4 Then came the worde of the Lord to Isaiah, saying,
Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
5 Goe, and say vnto Hezekiah, Thus saith the Lord God of Dauid thy father, I haue heard thy prayer, and seene thy teares: behold, I will adde vnto thy dayes fifteene yeeres.
“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
6 And I will deliuer thee out of the hand of the King of Asshur, and this citie: for I will defende this citie.
Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 And this signe shalt thou haue of ye Lord, that ye Lord will do this thing that he hath spoken,
“‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
8 Beholde, I will bring againe the shadowe of the degrees (whereby it is gone downe in the diall of Ahaz by the sunne) ten degrees backeward: so the sunne returned by tenne degrees, by the which degrees it was gone downe.
Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 The writing of Hezekiah King of Iudah, when he had bene sicke, and was recouered of his sickenesse.
Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 I saide in the cutting off of my dayes, I shall goe to the gates of the graue: I am depriued of the residue of my yeeres. (Sheol )
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
11 I said, I shall not see the Lord, euen the Lord in the land of the liuing: I shall see man no more among the inhabitants of the world.
Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Mine habitation is departed, and is remoued from me, like a shepheards tent: I haue cut off like a weauer my life: he will cut me off from the height: from day to night, thou wilt make an ende of me.
Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 I rekoned to the morning: but he brake all my bones, like a lion: from day to night wilt thou make an ende of me.
Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Like a crane or a swallow, so did I chatter: I did mourne as a doue: mine eies were lift vp on high: O Lord, it hath oppressed me, comfort me.
Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 What shall I say? for he hath said it to me, and he hath done it: I shall walke weakely all my yeeres in the bitternesse of my soule.
Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 O Lord, to them that ouerliue them, and to all that are in them, the life of my spirite shalbe knowen, that thou causedst me to sleepe and hast giuen life to me.
Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17 Beholde, for felicitie I had bitter griefe, but it was thy pleasure to deliuer my soule from the pit of corruption: for thou hast cast all my sinnes behinde thy backe.
Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
18 For the graue cannot confesse thee: death cannot praise thee: they that goe downe into the pit, cannot hope for thy trueth. (Sheol )
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
19 But the liuing, the liuing, he shall confesse thee, as I doe this day: the father to the children shall declare thy trueth.
Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
20 The Lord was ready to saue me: therefore we will sing my song, all the dayes of our life in the House of the Lord.
Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
21 Then said Isaiah, Take a lumpe of drye figs and lay it vpon the boyle, and he shall recouer.
Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
22 Also Hezekiah had said, What is ye signe, that I shall goe vp into the House of the Lord?
Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”